Miyambo 24 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 24:1-34

1Usachitire nsanje anthu oyipa,

usalakalake kuti uzikhala nawo,

2pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa,

ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.

3Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru,

ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;

4Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake

ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.

5Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri,

ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.

6Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo.

Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.

7Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru;

chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.

8Amene amakonzekera kuchita zoyipa

adzatchedwa mvundulamadzi.

9Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo,

ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.

10Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti

mphamvu yako ndi yochepadi!

11Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe;

uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.

12Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,”

kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi?

Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi?

Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?

13Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino;

uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.

14Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako;

ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo,

ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.

15Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa.

Usachite nayo nkhondo nyumba yake;

16paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso.

Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.

17Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako.

Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.

18Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo,

angaleke kukwiyira mdaniyo.

19Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa

kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,

20paja munthu woyipa alibe tsogolo.

Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.

21Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu,

ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,

22awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi.

Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?

Malangizo Enanso a Anthu Anzeru

23Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa:

Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:

24Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,”

anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.

25Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino

ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.

26Woyankhula mawu owona

ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.

27Ugwiriretu ntchito zako zonse,

makamaka za ku munda

ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.

28Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa,

kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.

29Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine;

ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”

30Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi

ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.

31Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga,

mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa,

ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.

32Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga

ndipo ndinatolapo phunziro ili:

33Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,”

kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”

34umphawi udzafika pa iwe ngati mbala

ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.

Священное Писание

Мудрые изречения 24:1-34

1Не завидуй неправедным людям,

к обществу их не стремись,

2ведь насилие у них на уме,

и уста их говорят о злодействе.

3Мудростью строится дом

и разумом утверждается;

4знание наполняет его комнаты

дорогим и красивым добром.

5Мудрый воин – силён,

человек знающий укрепляется в силе,

6ведь чтобы воевать, тебе нужно мудрое руководство,

и для победы – много советников.

7Мудрость слишком возвышенна для глупцов;

в собрании у ворот24:7 Ворота города были центром всей общественной жизни, около них проходили и судебные разбирательства. нечего им сказать.

8Кто замышляет дурное,

того назовут злоумышленником.

9Замыслы глупости – грех,

и глумливого гнушаются люди.

10Если ты дал слабину в день беды,

то сила твоя ничтожна.

11Освобождай ведомых на смерть безвинно,

бредущих на убой спасай.

12Ты можешь сказать: «Ой, мы об этом не знали»,

но разве Взвешивающий сердца не поймёт?

Разве Хранящий твою жизнь не узнает?

И разве Он не воздаст каждому по делам?

13Ешь мёд, сын мой, ведь он хорош;

сотовый мёд тебе сладок.

14Знай: так же сладка твоей душе мудрость;

если найдёшь её – есть у тебя будущее,

и надежда твоя не погибнет.

15Не устраивай, как разбойник, засады у дома праведника,

не разоряй его крова,

16ведь праведник, пусть семь раз упадёт, поднимется,

а злодеев беда погубит.

17Не радуйся, когда враг твой упал

и когда он споткнулся, пусть сердце твоё не ликует;

18иначе Вечный увидит, и это будет Ему неугодно,

и Он отвратит от него Свой гнев.

19Не раздражайся из-за злодеев

и не завидуй нечестивым,

20ведь у злодея нет будущего,

и жизнь нечестивых как гаснущий светильник.

21Сын мой, бойся Вечного и царя

и не общайся с мятежниками,

22ведь от них обоих внезапно придёт к мятежникам беда,

и кто знает, какие невзгоды они им пошлют?

Дополнительные изречения мудрецов

23Вот ещё изречения мудрецов:

Выказывать лицеприятие на суде нехорошо.

24На сказавшего виноватому: «Ты невиновен» –

будут слать проклятия народы,

и племена будут негодовать.

25А осудившие виновного будут преуспевать,

и придёт на них благословение.

26Честный ответ –

что поцелуй в губы.

27Заверши работу на улице,

приведи в порядок свои поля,

а потом можешь строить дом свой24:27 Или: «заводить семью»..

28Не лжесвидетельствуй против ближнего твоего

и не лги своими устами.

29Не говори: «Поступлю с ним, как он со мной;

отплачу ему за то, что он сделал».

30Я шёл мимо поля лентяя,

мимо виноградника человека неразумного:

31всё поросло колючкой,

сорняками зарос участок,

и ограда из камня рухнула.

32Я глядел и думал об этом,

я смотрел и понял урок:

33немного поспишь, немного подремлешь,

немного, руки сложив, полежишь,

34и придёт к тебе нищета, как грабитель24:34 Или: «как бродяга».,

настигнет нужда, как разбойник24:34 Или: «как попрошайка»..