Miyambo 23 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 23:1-35

1Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira,

uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,

2ngati ndiwe munthu wadyera

udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.

3Usasirire zakudya zake,

pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.

4Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma,

ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.

5Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo.

Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi

ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.

6Usadye chakudya cha munthu waumbombo,

usalakalake zakudya zake zokoma;

7paja iye ndi munthu amene

nthawi zonse amaganizira za mtengo wake

ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,”

koma sakondweretsedwa nawe.

8Udzasanza zimene wadyazo

ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.

9Usayankhule munthu wopusa akumva,

pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.

10Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale

kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,

11paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu;

iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.

12Mtima wako uzikhala pa malangizo

ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.

13Usaleke kumulangiza mwana;

ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.

14Ukamukwapula ndi tsatsa

udzapulumutsa moyo wake.

15Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru,

inenso mtima wanga udzakondwera.

16Mtima wanga udzakondwera

pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.

17Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa,

koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.

18Ndithu za mʼtsogolo zilipo

ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.

19Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru,

mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.

20Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera

kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.

21Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi

ndipo aulesi adzavala sanza.

22Mvera abambo ako amene anakubala,

usanyoze amayi ako pamene akalamba.

23Gula choonadi ndipo usachigulitse;

ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.

24Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu;

Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.

25Abambo ndi amayi ako asangalale;

amene anakubereka akondwere!

26Mwana wanga, undikhulupirire

ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.

27Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama;

ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.

28Amabisala ngati mbala yachifwamba,

ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.

29Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni?

Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo?

Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?

30Ndi amene amakhalitsa pa mowa,

amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.

31Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo,

pamene akuwira mʼchikho

pamene akumweka bwino!

32Potsiriza pake amaluma ngati njoka,

ndipo amajompha ngati mphiri.

33Maso ako adzaona zinthu zachilendo

ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.

34Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja,

kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.

35Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe!

Andimenya koma sindinamve kanthu!

Kodi ndidzuka nthawi yanji?

Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”