Miyambo 22 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 22:1-29

1Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri;

kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.

2Wolemera ndi wosauka ndi ofanana;

onsewa anawalenga ndi Yehova.

3Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala,

koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.

4Mphotho ya munthu wodzichepetsa

ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.

5Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha,

koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.

6Mwana muzimuphunzitsa njira yake,

ndipo akadzakalamba sadzachokamo.

7Wolemera amalamulira wosauka,

ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.

8Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto,

ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.

9Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika,

pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.

10Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha;

mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.

11Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino,

adzakhala bwenzi la mfumu.

12Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu,

koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.

13Munthu waulesi amati,

“Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”

14Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama;

amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.

15Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana,

koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.

16Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake,

ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.

Malangizo a Anthu Anzeru

17Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru;

uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.

18Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako

ndi wokonzeka kuziyankhula.

19Ndakuphunzitsa zimenezi lero

koma makamaka uziopa Yehova.

20Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu

okuchenjeza ndi okupatsa nzeru,

21malangizo okudziwitsa zolungama

ndi zoona

ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?

22Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka,

ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,

23pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo

ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.

24Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima

ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya

25kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake

ndi kukodwa mu msampha.

26Usakhale munthu wopereka chikole

kapena kukhala mboni pa ngongole;

27ngati ulephera kupeza njira yolipirira

adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.

28Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale

amene anayikidwa ndi makolo ako.

29Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake?

Iye adzatumikira mafumu;

sadzatumikira anthu wamba.

Luganda Contemporary Bible

Engero 22:1-29

Omugaso gw’Erinnya Eddungi

122:1 Mub 7:1Erinnya eddungi lyagalibwa okusinga eby’obugagga ebingi,

n’okuganja kusinga ffeeza oba zaabu.

222:2 Yob 31:15Abagagga n’abaavu balina kimu ekibagatta,

Mukama ye Mutonzi waabwe bonna.

322:3 a Nge 14:16 b Nge 27:12Omuntu omutegeevu bw’alaba akabi yeekweka,

naye abatalina magezi bagenda bugenzi mu maaso ne balumizibwa.

4Obugagga n’ekitiibwa n’obulamu

y’empeera ey’okwetoowazanga n’okutyanga Mukama.

522:5 Nge 15:19Amaggwa n’emitego biri mu kkubo ly’omubambaavu;

naye oyo akuuma emmeeme ye anaabyewalanga.

622:6 Bef 6:4Manyiiriza omwana mu kkubo erimugwanira okutambulirangamu,

ne bw’alikula talirivaamu.

7Omugagga afuga abaavu,

naye eyeewola aba muddu w’oyo amuwola.

822:8 a Yob 4:8 b Zab 125:3Asiga obutali butuukirivu akungula mitawaana,

n’oluga olw’obusungu bwe lulizikirizibwa.

922:9 a 2Ko 9:6 b Nge 19:17Omuntu omugabi anaabanga n’omukisa,

kubanga emmere ye agirya n’abaavu.

1022:10 Nge 18:6; 26:20Goba omunyoomi, entalo zinaagenda,

ennyombo n’okuvumagana binaakoma.

1122:11 Nge 16:13; Mat 5:8Omuntu eyeegomba omutima omulongoofu

era ayogera n’eggonjebwa, talirema kuganja ewa kabaka.

12Amaaso ga Mukama galabirira amazima,

era adibya entegeka z’abatali beesigwa.

1322:13 Nge 26:13Omugayaavu ayogera nti, “Ebweru eriyo empologoma,”

oba nti, “Nnyinza okutemulirwa mu kkubo.”

1422:14 a Nge 2:16; 5:3-5; 7:5; 23:27 b Mub 7:26Malaaya mutego gwa kabi,

akolimiddwa Mukama mw’afiira.

1522:15 Nge 13:24; 23:14Obusirusiru busibiddwa ku mutima gw’omwana omuto,

naye omuggo ogukangavvula gulimuwonyeza ddala.

16Omuntu atulugunya abaavu ne yeeyongera okugaggawala,

n’oyo agabira omugagga awa abagagga enguzi, enkomerero ya bombi bwavu.

1722:17 Nge 5:1Ossangayo omwoyo okuwuliriza ebigambo by’omugezi,

n’omutima gwo eri ebyo bye njigiriza.

18Kibeera kya ssanyu bw’obikwata ku mutima gwo,

n’oba mwetegefu okubiddamu byonna.

19Mbikumanyisa leero ggwe,

obwesige bwo bubeerenga mu Mukama.

20Kale sikuwandiikidde ebintu amakumi asatu ebikuwabula

era ebikuwa okumanya?

2122:21 Luk 1:3-4; 1Pe 3:15Sikulaze ekirungi n’ekituufu,

olyoke obe n’eky’okuddamu eri oyo eyakutuma?

2222:22 a Zek 7:10 b Kuv 23:6; Mal 3:5Tonyaganga mwavu, kubanga mwavu,

oba okutulugunyanga aleeteddwa mu mbuga.

2322:23 a Zab 12:5 b 1Sa 25:39; Nge 23:10-11Kubanga Mukama alibawolereza,

n’abo ababanyaga alibanyaga.

24Tokwananga muntu wa busungu,

oba okuyitanga n’omuntu anyiiganyiiga amangu,

2522:25 1Ko 15:33oleme okuyiga amakubo ge

ne weesuula mu mitawaana.

2622:26 Nge 11:15Teweegattanga ku abo abeeyama,

newaakubadde ku abo abeeyimirira ab’amabanja.

2722:27 Nge 17:18Bw’oliba nga tolina kya kusasula

ekitanda kyo kyennyini kye kirikuggyibwako.

2822:28 Ma 19:14; Nge 23:10Tojjululanga nsalo

bajjajjaabo gye bassaawo edda.

2922:29 Lub 41:46Omanyi omuntu omunyiikivu era omukugu mu mulimu gwe?

Aliweereza bakabaka; taliweereza bantu batamanyiddwa.