Miyambo 22 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 22:1-29

1Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri;

kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.

2Wolemera ndi wosauka ndi ofanana;

onsewa anawalenga ndi Yehova.

3Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala,

koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.

4Mphotho ya munthu wodzichepetsa

ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.

5Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha,

koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.

6Mwana muzimuphunzitsa njira yake,

ndipo akadzakalamba sadzachokamo.

7Wolemera amalamulira wosauka,

ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.

8Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto,

ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.

9Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika,

pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.

10Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha;

mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.

11Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino,

adzakhala bwenzi la mfumu.

12Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu,

koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.

13Munthu waulesi amati,

“Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”

14Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama;

amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.

15Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana,

koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.

16Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake,

ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.

Malangizo a Anthu Anzeru

17Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru;

uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.

18Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako

ndi wokonzeka kuziyankhula.

19Ndakuphunzitsa zimenezi lero

koma makamaka uziopa Yehova.

20Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu

okuchenjeza ndi okupatsa nzeru,

21malangizo okudziwitsa zolungama

ndi zoona

ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?

22Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka,

ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,

23pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo

ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.

24Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima

ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya

25kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake

ndi kukodwa mu msampha.

26Usakhale munthu wopereka chikole

kapena kukhala mboni pa ngongole;

27ngati ulephera kupeza njira yolipirira

adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.

28Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale

amene anayikidwa ndi makolo ako.

29Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake?

Iye adzatumikira mafumu;

sadzatumikira anthu wamba.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

箴言 22:1-29

1美名胜过巨富,

恩宠比金银宝贵。

2富人和穷人相同:

都由耶和华所造。

3明哲人遇祸躲避,

愚昧人前往受害。

4心存谦卑、敬畏耶和华,

必得财富、尊荣和生命。

5奸徒之道有荆棘和陷阱,

想保全生命的必须远避。

6教导孩童走正路,

他到老也不偏离。

7富人管辖穷人,

欠债的是债主的仆人。

8播种不义的必收灾祸,

他的恶势力终必瓦解。

9慷慨的人必蒙福,

因他给穷人食物。

10赶走嘲讽者,纷争平息,

争吵和羞辱也会消除。

11喜爱清心、口吐恩言的人,

必与君王为友。

12耶和华的眼目护卫真理,

祂必推翻奸徒的言论。

13懒惰人说:“外面有狮子,

我会丧命街头。”

14淫妇的口是深坑,

耶和华憎恶的人必陷进去。

15愚昧缠住孩童的心,

教棍能远远赶走它。

16靠压榨穷人敛财和送礼给富人的,

都必穷困潦倒。

智者之言

17你要侧耳听智者之言,

专心领受我的教诲,

18铭记在心、随时诵咏,

方为美事。

19今天我将这些指示你,

为要使你倚靠耶和华。

20关于谋略和知识,

我已写给你三十条,

21要使你认识真理,

能准确答复差你来的人。

22不可仗势剥削贫穷人,

法庭上不可欺凌弱者,

23因为耶和华必为他们申冤,

夺去掠夺他们之人的性命。

24不可结交脾气暴躁者,

不要跟易怒之人来往,

25免得你沾染他们的恶习,

不能自拔。

26不要为人击掌作保,

不要为欠债的抵押。

27如果你还不起,

连你的床也会被抬走。

28不可移动祖先定下的界石。

29你看那精明能干的人,

他必侍立在君王面前,

不会效力于泛泛之辈。