Miyambo 21 – CCL & NAV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 21:1-31

1Mtima wa mfumu uli ngati mtsinje wamadzi mʼdzanja la Yehova;

Iye amautsongolera pa chilichonse chimene akufuna.

2Makhalidwe a munthu amaoneka olungama kwa mwini wakeyo,

koma Yehova ndiye amayesa mtima wake.

3Za chilungamo ndi zolondola

ndi zomwe zimakondweretsa Yehova kuposa kupereka nsembe.

4Maso odzikuza ndi mtima wonyada,

zimatsogolera anthu oyipa ngati nyale nʼchifukwa chake amachimwa.

5Zolinga za munthu wakhama zimachulukitsa zinthu zake;

koma aliyense wochita zinthu mofulumira amadzakhala wosauka.

6Chuma chochipeza ndi mawu onyenga ndi chosakhalitsa

ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.

7Chiwawa cha anthu oyipa chidzawawononga,

pakuti iwo amakana kuchita zolungama.

8Njira ya munthu wolakwa ndi yokhotakhota,

koma makhalidwe a munthu wosalakwa ndi olungama.

9Nʼkwabwino kukhala wekha pa ngodya ya denga la nyumba,

kuposa kukhala mʼnyumba pamodzi ndi mkazi wolongolola.

10Munthu woyipa amalakalaka zoyipa;

sachitira chifundo mnansi wake wovutika.

11Munthu wonyoza akalangidwa, anthu opusa amapeza nzeru;

koma munthu wanzeru akalangizidwa, amapeza chidziwitso.

12Zolingalira za munthu woyipa nʼzosabisika pamaso pa Yehova,

ndipo Iye adzawononga woyipayo.

13Amene atsekera mʼkhutu mwake wosauka akamalira,

nayenso adzalira koma palibe adzamuyankhe.

14Mphatso yoperekedwa mseri imathetsa mkwiyo,

ndipo chiphuphu choperekedwa mobisa chimathetsa mphamvu ya ukali woopsa.

15Chilungamo chikachitika anthu olungama amasangalala,

koma anthu oyipa amaopsedwa nazo.

16Munthu amene amachoka pa njira ya anthu anzeru

adzapezeka mʼgulu la anthu akufa.

17Aliyense wokonda zisangalalo adzasanduka mʼmphawi,

ndipo wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.

18Anthu oyipa adzakhala chowombolera cha anthu olungama

ndipo osakhulupirika chowombolera anthu olungama mtima.

19Nʼkwabwino kukhala mʼchipululu

kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wopsa mtima msanga.

20Munthu wanzeru samwaza chuma chake,

koma wopusa amachiwononga.

21Amene amatsata chilungamo ndi kukhulupirika,

amapeza moyo ndi ulemerero.

22Munthu wanzeru amagonjetsa mzinda wa anthu amphamvu

ndi kugwetsa linga limene iwo amalidalira.

23Amene amagwira pakamwa pake ndi lilime lake

sapeza mavuto.

24Munthu wonyada ndi wodzikuza amamutcha, “Mnyodoli,”

iye amachita zinthu modzitama kwambiri.

25Chilakolako cha munthu waulesi chidzamupha yekha

chifukwa manja ake amangokhala goba osagwira ntchito.

26Tsiku lonse anthu oyipa amasirira zambiri,

koma anthu olungama amapereka mowolowamanja.

27Nsembe ya anthu oyipa imamunyansa Yehova,

nanji akayipereka ndi cholinga choyipa!

28Mboni yonama idzawonongeka,

koma mawu a munthu wakumva adzakhala nthawi zonse.

29Munthu woyipa amafuna kudzionetsa ngati wolimba mtima,

koma munthu wowongoka amaganizira njira zake.

30Palibe nzeru, palibe kumvetsa bwino, palibenso uphungu,

zimene zingapambane Yehova.

31Kavalo amamukonzera tsiku la nkhondo,

koma ndi Yehova amene amapambanitsa.

Ketab El Hayat

الأمثال 21:1-31

1قَلْبُ الْمَلِكِ فِي يَدِ الرَّبِّ كَجَدَاوِلِ مِيَاهٍ يُمِيلُهُ حَيْثُمَا شَاءَ. 2جَمِيعُ تَصَرُّفَاتِ الإِنْسَانِ تَبْدُو نَقِيَّةً فِي عَيْنَيْ نَفْسِهِ، وَلَكِنَّ الرَّبَّ مُطَّلِعٌ عَلَى حَوَافِزِ الْقُلُوبِ. 3إِجْرَاءُ الْعَدْلِ وَالْحَقِّ أَكْثَرُ قُبُولاً عِنْدَ الرَّبِّ مِنَ الذَّبِيحَةِ. 4تَشَامُخُ الْعَيْنَيْنِ مِنْ غَطْرَسَةِ الْقَلْبِ، وَسِرَاجُ الأَشْرَارِ خَطِيئَةٌ. 5خُطَطُ الْمُجْتَهِدِ تُفْضِي حَتْماً إِلَى الْخِصْبِ، وَالْعَجُولُ مَصِيرُهُ الْعَوَزُ. 6ادِّخَارُ الْكُنُوزِ بِلِسَانٍ مُنَافِقٍ، دُخَانٌ مَتَلاشٍ وَفَخٌّ مُمِيتٌ. 7جَوْرُ الأَشْرَارِ يَجْرُفُهُمْ لِرَفْضِهِمْ إِجْرَاءَ الْعَدْلِ. 8طَرِيقُ الْمُذْنِبِ مُعَوَّجَةٌ، أَمَّا تَصَرُّفُ الزَّكِيِّ فَقَوِيمٌ. 9الإِقَامَةُ فِي رُكْنِ سَطْحٍ خَيْرٌ مِنْ مُشَاطَرَةِ بَيْتٍ مَعَ زَوْجَةٍ نَكِدَةٍ. 10نَفْسُ الْمُنَافِقِ تَشْتَهِي الشَّرَّ، وَقَرِيبُهُ لَا يَحْظَى بِرِضَاهُ. 11إِذَا عُوقِبَ الْمُسْتَهْزِئُ صَارَ الْجَاهِلُ حَكِيماً، وَإِنْ أُرْشِدَ الْحَكِيمُ اكْتَسَبَ مَعْرِفَةً.

12يَتَأَمَّلُ الصِّدِّيقُ فِي بَيْتِ الشِّرِّيرِ، (فَيَرَاهُ) يُلْقَى بِهِ إِلَى الْبَلايَا.

كنوز الحكيم

13مَنْ أَصَمَّ أُذُنَهُ عَنْ صُرَاخِ الْمِسْكِينِ، يَصْرُخُ هُوَ أَيْضاً وَلا مِنْ مُجِيبٍ. 14الْهَدِيَّةُ فِي الْخَفَاءِ تُخْمِدُ الْغَضَبَ، وَالرِّشْوَةُ فِي الْحِضْنِ تُسَكِّنُ السَّخَطَ. 15الْحُكْمُ بِالْعَدْلِ فَرَحٌ لِلصِّدِّيقِ، وَرُعْبٌ لِفَاعِلِي الإِثْمِ. 16الرَّجُلُ الشَّارِدُ عَنْ طَرِيقِ الْمَعْرِفَةِ يَسْكُنُ بَيْنَ جَمَاعَةِ الْمَوْتَى. 17عَاشِقُ اللَّذَّةِ فَقِيرٌ، وَالْمُوْلَعُ بِالْخَمْرِ وَالطِّيبِ لَا يَغْتَنِي. 18الشِّرِّيرُ فِدَاءٌ عَنِ الصِّدِّيقِ، وَالْغَادِرُ عَنِ الْمُسْتَقِيمِينَ. 19الإِقَامَةُ فِي أَرْضٍ مُقْفِرَةٍ خَيْرٌ مِنَ السُّكْنَى مَعَ امْرَأَةٍ مُشَاكِسَةٍ شَرِسَةٍ. 20فِي بَيْتِ الْحَكِيمِ كُنُوزٌ وَزَيْتٌ مُدَّخَرَةٌ، أَمَّا الإِنْسَانُ الْجَاهِلُ فَيُتْلِفُ مَا لَدَيْهِ. 21مَنِ اتَّبَعَ الْعَدْلَ وَالرَّحْمَةَ يَلْقَى الْحَيَاةَ وَالْحَقَّ وَالْمَجْدَ. 22الْحَكِيمُ يَتَسَلَّقُ سُورَ مَدِينَةِ الْجَبَابِرَةِ وَيُدَمِّرُ مَعْقِلَ اعْتِمَادِهِمْ 23مَنْ يَصُونُ فَمَهُ وَلِسَانَهُ عَنِ اللَّغْوِ يَحْفَظُ نَفْسَهُ مِنَ الْمَتَاعِبِ. 24الْمُتَشَامِخُ الْمُنْتَفِخُ يُدْعَى الْمُسْتَهْزِئَ لأَنَّهُ يَتَصَرَّفُ بِغُرُورِ الْكِبْرِيَاءِ. 25أَوْهَامُ الْكَسُولِ تَقْتُلُهُ لأَنَّ يَدَيْهِ تَأْبَيَانِ الْعَمَلَ. 26يَظَلُّ طَوَالَ النَّهَارِ مُتَشَهِّياً مُتَمَنِّياً، أَمَّا الصِّدِّيقُ فَيَسْخُو وَلا يَضِنُّ 27ذَبِيحَةُ الشِّرِّيرِ رِجْسٌ عِنْدَ الرَّبِّ، فَكَمْ بِالْحَرِيِّ إِنْ قَرَّبَهَا بِنِيَّةٍ أَثِيمَةٍ؟ 28شَاهِدُ الزُّورِ يَهْلِكُ، أَمَّا أَقْوَالُ الرَّجُلِ الْحَرِيصِ عَلَى الاسْتِمَاعِ فَتَدُومُ. 29الرَّجُلُ الشِّرِّيرُ يُغْلِظُ وَجْهَهُ، أَمَّا الْمُسْتَقِيمُ فَيَعْمَلُ عَلَى تَقْوِيمِ طُرُقِهِ. 30لَيْسَ مِنْ حِكْمَةٍ، وَلا مِنْ مَشُورَةٍ، وَلا مِنْ فِطْنَةٍ بِقَادِرَةٍ عَلَى مُقَاوَمَةِ اللهِ. 31مَعَ أَنَّ الْفَرَسَ مُعَدٌّ لِيَوْمِ الْقِتَالِ، فَإِنَّ النَّصْرَ هُوَ مِنْ عِنْدِ اللهِ.