Miyambo 21 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 21:1-31

1Mtima wa mfumu uli ngati mtsinje wamadzi mʼdzanja la Yehova;

Iye amautsongolera pa chilichonse chimene akufuna.

2Makhalidwe a munthu amaoneka olungama kwa mwini wakeyo,

koma Yehova ndiye amayesa mtima wake.

3Za chilungamo ndi zolondola

ndi zomwe zimakondweretsa Yehova kuposa kupereka nsembe.

4Maso odzikuza ndi mtima wonyada,

zimatsogolera anthu oyipa ngati nyale nʼchifukwa chake amachimwa.

5Zolinga za munthu wakhama zimachulukitsa zinthu zake;

koma aliyense wochita zinthu mofulumira amadzakhala wosauka.

6Chuma chochipeza ndi mawu onyenga ndi chosakhalitsa

ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.

7Chiwawa cha anthu oyipa chidzawawononga,

pakuti iwo amakana kuchita zolungama.

8Njira ya munthu wolakwa ndi yokhotakhota,

koma makhalidwe a munthu wosalakwa ndi olungama.

9Nʼkwabwino kukhala wekha pa ngodya ya denga la nyumba,

kuposa kukhala mʼnyumba pamodzi ndi mkazi wolongolola.

10Munthu woyipa amalakalaka zoyipa;

sachitira chifundo mnansi wake wovutika.

11Munthu wonyoza akalangidwa, anthu opusa amapeza nzeru;

koma munthu wanzeru akalangizidwa, amapeza chidziwitso.

12Zolingalira za munthu woyipa nʼzosabisika pamaso pa Yehova,

ndipo Iye adzawononga woyipayo.

13Amene atsekera mʼkhutu mwake wosauka akamalira,

nayenso adzalira koma palibe adzamuyankhe.

14Mphatso yoperekedwa mseri imathetsa mkwiyo,

ndipo chiphuphu choperekedwa mobisa chimathetsa mphamvu ya ukali woopsa.

15Chilungamo chikachitika anthu olungama amasangalala,

koma anthu oyipa amaopsedwa nazo.

16Munthu amene amachoka pa njira ya anthu anzeru

adzapezeka mʼgulu la anthu akufa.

17Aliyense wokonda zisangalalo adzasanduka mʼmphawi,

ndipo wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.

18Anthu oyipa adzakhala chowombolera cha anthu olungama

ndipo osakhulupirika chowombolera anthu olungama mtima.

19Nʼkwabwino kukhala mʼchipululu

kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wopsa mtima msanga.

20Munthu wanzeru samwaza chuma chake,

koma wopusa amachiwononga.

21Amene amatsata chilungamo ndi kukhulupirika,

amapeza moyo ndi ulemerero.

22Munthu wanzeru amagonjetsa mzinda wa anthu amphamvu

ndi kugwetsa linga limene iwo amalidalira.

23Amene amagwira pakamwa pake ndi lilime lake

sapeza mavuto.

24Munthu wonyada ndi wodzikuza amamutcha, “Mnyodoli,”

iye amachita zinthu modzitama kwambiri.

25Chilakolako cha munthu waulesi chidzamupha yekha

chifukwa manja ake amangokhala goba osagwira ntchito.

26Tsiku lonse anthu oyipa amasirira zambiri,

koma anthu olungama amapereka mowolowamanja.

27Nsembe ya anthu oyipa imamunyansa Yehova,

nanji akayipereka ndi cholinga choyipa!

28Mboni yonama idzawonongeka,

koma mawu a munthu wakumva adzakhala nthawi zonse.

29Munthu woyipa amafuna kudzionetsa ngati wolimba mtima,

koma munthu wowongoka amaganizira njira zake.

30Palibe nzeru, palibe kumvetsa bwino, palibenso uphungu,

zimene zingapambane Yehova.

31Kavalo amamukonzera tsiku la nkhondo,

koma ndi Yehova amene amapambanitsa.

King James Version

Proverbs 21:1-31

1The king’s heart is in the hand of the LORD, as the rivers of water: he turneth it whithersoever he will. 2Every way of a man is right in his own eyes: but the LORD pondereth the hearts. 3To do justice and judgment is more acceptable to the LORD than sacrifice. 4An high look, and a proud heart, and the plowing of the wicked, is sin.21.4 An…: Heb. Haughtiness of eyes21.4 the plowing: or, the light 5The thoughts of the diligent tend only to plenteousness; but of every one that is hasty only to want. 6The getting of treasures by a lying tongue is a vanity tossed to and fro of them that seek death. 7The robbery of the wicked shall destroy them; because they refuse to do judgment.21.7 destroy…: Heb. saw them, or, dwell with them 8The way of man is froward and strange: but as for the pure, his work is right. 9It is better to dwell in a corner of the housetop, than with a brawling woman in a wide house.21.9 a brawling…: Heb. a woman of contentions21.9 a wide…: Heb. an house of society 10The soul of the wicked desireth evil: his neighbour findeth no favour in his eyes.21.10 findeth…: Heb. is not favoured 11When the scorner is punished, the simple is made wise: and when the wise is instructed, he receiveth knowledge. 12The righteous man wisely considereth the house of the wicked: but God overthroweth the wicked for their wickedness. 13Whoso stoppeth his ears at the cry of the poor, he also shall cry himself, but shall not be heard. 14A gift in secret pacifieth anger: and a reward in the bosom strong wrath. 15It is joy to the just to do judgment: but destruction shall be to the workers of iniquity. 16The man that wandereth out of the way of understanding shall remain in the congregation of the dead. 17He that loveth pleasure shall be a poor man: he that loveth wine and oil shall not be rich.21.17 pleasure: or, sport 18The wicked shall be a ransom for the righteous, and the transgressor for the upright. 19It is better to dwell in the wilderness, than with a contentious and an angry woman.21.19 in…: Heb. in the land of the desert 20There is treasure to be desired and oil in the dwelling of the wise; but a foolish man spendeth it up. 21He that followeth after righteousness and mercy findeth life, righteousness, and honour. 22A wise man scaleth the city of the mighty, and casteth down the strength of the confidence thereof. 23Whoso keepeth his mouth and his tongue keepeth his soul from troubles. 24Proud and haughty scorner is his name, who dealeth in proud wrath.21.24 in proud…: Heb. in the wrath of pride

25The desire of the slothful killeth him; for his hands refuse to labour. 26He coveteth greedily all the day long: but the righteous giveth and spareth not. 27The sacrifice of the wicked is abomination: how much more, when he bringeth it with a wicked mind?21.27 with…: Heb. in wickedness? 28A false witness shall perish: but the man that heareth speaketh constantly.21.28 A…: Heb. A witness of lies 29A wicked man hardeneth his face: but as for the upright, he directeth his way.21.29 directeth: or, considereth

30There is no wisdom nor understanding nor counsel against the LORD. 31The horse is prepared against the day of battle: but safety is of the LORD.21.31 safety: or, victory