Miyambo 20 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 20:1-30

1Vinyo amachititsa munthu kukhala wonyoza ndipo chakumwa choledzeretsa chimachititsa munthu kukhala wolongolola;

aliyense wosochera nazo zimenezi alibe nzeru.

2Ukali wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango;

amene amawuputa mkwiyowo amataya moyo wake.

3Nʼchaulemu kwa munthu kupewa mikangano,

koma chitsiru chilichonse chimafulumira kulongolola.

4Munthu waulesi satipula mʼmunda pa nthawi yoyenera;

kotero pa nthawi yokolola adzafunafuna zinthu koma sadzapeza kanthu kalikonse.

5Zolinga za mtima wa munthu zili ngati madzi akuya,

munthu womvetsa zinthu ndiye yekha angawatunge.

6Anthu ambiri amayankhula za kukhulupirika kwawo,

koma munthu wokhulupirika angamupeze ndani?

7Munthu wolungama amakhala ndi makhalidwe abwino;

odala ndi ana ake amene amatsanzira moyo wake.

8Mfumu ikhala pa mpando wake wa chiweruzo,

imapeta ndi maso ake anthu onse oyipa.

9Ndani amene anganene kuti, “Ndawuyeretsa mtima wanga;

ndilibe tchimo lililonse?”

10Masikelo ndi miyeso ya zinthu imene ili yachinyengo

zonsezi Yehova zimamunyansa.

11Ngakhale mwana amadziwika ndi zochita zake,

ngati zochita zake zili zoyera ndi zoyenera.

12Makutu amene amamva ndi maso amene amaona,

zonsezi anazilenga ndi Yehova.

13Usakonde tulo ungasauke;

khala maso ndipo udzakhala ndi chakudya chambiri.

14Munthu wogula chinthu amati, “Sichabwino, sichabwino.”

Koma akagula nʼkuchokapo amayamba kudzitama.

15Pali golide ndi miyala yamtengowapatali,

koma milomo yoyankhula zanzeru ndi yamtengowapatali koposa zonsezi.

16Utenge chovala cha munthu amene waperekera mlendo chikole;

kuti chikhale chikole chako chifukwa waperekera chikole munthu wachilendo.

17Chakudya chochipeza mwachinyengo chimukomera munthu,

koma pa mapeto pake chimasanduka ngati mchenga mʼkamwa mwake.

18Zokonzekera zimapindula utafunsira uphungu;

ndipo usanamenye nkhondo yamba wapempha malangizo oyenera.

19Amene amanka nanena miseche amawulula zachinsinsi.

Choncho usamagwirizane naye munthu woyankhula zopusayo.

20Ngati munthu atemberera abambo ake kapena amayi ake,

moyo wake udzazimitsidwa ngati nyale mu mdima wandiweyani.

21Cholowa chochipeza mofulumira poyamba,

sichidzakhala dalitso pa mapeto pake.

22Usanene kuti, “Ine ndidzabwezera choyipa chimenechi!”

Dikira Yehova, ndipo Iye adzakupulumutsa.

23Miyeso yosintha imamunyansa Yehova;

ndipo masikelo onyenga si abwino.

24Mayendedwe a munthu amawalamulira ndi Yehova,

tsono munthu angadziwe bwanji njira yake?

25Ndi msampha kwa munthu kuyankhula mofulumira kuti “Chinthu ichi nʼchopatulika kwa Yehova,”

popeza mwina atha kusintha maganizo utalumbira kale.

26Mfumu ya nzeru imapeta kwathunthu

anthu oyipa.

27Mpweya wa munthu uli ngati nyale ya Yehova;

imafufuza ziwalo zake zonse zamʼkati.

28Kukoma mtima ndi kukhulupirika ndizo zimasunga mfumu;

chilungamo chimalimbikitsa mpando wake waufumu.

29Ulemerero wa achinyamata uli mu mphamvu zawo,

imvi ndi ulemerero wa anthu okalamba.

30Mikwingwirima yopweteka ndiyo imachotsa zoyipa,

ndipo mikwapulo ndiyo imachotsa zamʼkatikati mwa munthu.

New Serbian Translation

Приче Соломонове 20:1-30

1Вино је подсмевач и жестоко пиће свађалица,

немудар је ко се због њих тетура.

2Царево је насиље као рика лавића,

ко га раздражује себи самом шкоди.

3На част је човеку да се клони свађе,

а сваки се безумник избезуми.

4Кад је јесен – ленштина не оре,

кад је жетва – он проси и оскудева.

5Дубока је вода замисао човековог срца,

ал’ је црпсти може само човек разборити.

6Многи људи објављују свима своју доброту,

али ко ће наћи оданог човека?

7Праведник живи честитост своју

и како су само благословена деца након њега!

8Цар који седи на судском престолу

погледом својим све зло расипа.

9Може ли ко рећи: „Срце сам своје очистио,

чист сам од греха свога“?

10Неједнаки тегови и мера двојака –

обоје су огавни Господу.

11И дете се по делима својим препознаје,

да ли су му дела исправна и чиста.20,11 Овај стих може и овако да се преведе: Чак и дете делима својим сакрива своје праве мотиве, да не знаш јесу ли му дела исправна и чиста.

12И ухо што чује и око што види,

и једно и друго створио је Господ.

13Не воли спавање да не осиромашиш,

пробуди се и најешћеш се хлеба.

14„Безвредно! Безвредно!“ – говори купац –

а онда се хвали када оде својим путем.

15Постоји злато и мноштво драгуља,

али учене усне су као драгоцени накит.

16Узми хаљину ономе што јамчи за туђинца,

и залог му узми кад јамчи за незнанца.

17Човеку је сладак непоштени хлеб,

али су му после уста песка пуна.

18Намере осмисли саветом

и мудрим вођењем ратуј.

19Оговарач скита и одаје тајне,

зато се не петљај са брбљивцем.

20Ко проклиње и оца и мајку,

светиљка му догорева у најцрњој тами.

21У почетку нагло згрнуто наследство

остаје неблагословено на свом крају.

22Немој рећи: „Узвратићу злу!“

Чекај Господа да те избави.

23Господу су мрски неједнаки тегови

и страшне су теразије неједнаке.

24Од Господа су човекови кораци,

па како би неко докучио свој властити пут?

25Човеку је замка кад непромишљено каже да је нешто посвећено,

а да после завете разматра.

26Цар ће мудар развејати зликовце,

вршидбеним точком преко њих ће прећи.

27Светиљка Господња је човеков дах,

испитује дубине нутрине.

28Оданост и истина чувају цара,

он оданошћу остаје на престолу своме.

29Младићу је част у његовој снази

а седа је коса достојанство старих.

30Ране и маснице чисте од зла,

а шиба чисти дубине нутрине.