Miyambo 2 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 2:1-22

Ubwino Wanzeru

1Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga

ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,

2ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru

ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;

3ngati upempha kuti uzindikire zinthu

inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,

4ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva

ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,

5ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova;

ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.

6Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru,

ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.

7Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo.

Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,

8pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama.

Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.

9Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo,

kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.

10Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako,

kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.

11Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga;

kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.

12Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa,

kwa anthu amabodza,

13amene amasiya njira zolungama

namayenda mʼnjira zamdima,

14amene amakondwera pochita zoyipa

namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.

15Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota,

ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.

16Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo;

kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,

17amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake

ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.

18Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa;

njira zake zimamufikitsa ku manda.

19Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera

kapena kupezanso njira zamoyo.

20Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino,

uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.

21Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko

ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;

22Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo,

ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.

Nova Versão Internacional

Provérbios 2:1-22

O Valor da Sabedoria

1Meu filho, se você aceitar as minhas palavras

e guardar no coração os meus mandamentos;

2se der ouvidos à sabedoria

e inclinar o coração para o discernimento;

3se clamar por entendimento

e por discernimento gritar bem alto;

4se procurar a sabedoria como se procura a prata

e buscá-la como quem busca um tesouro escondido,

5então você entenderá o que é temer o Senhor

e achará o conhecimento de Deus.

6Pois o Senhor é quem dá sabedoria;

de sua boca procedem o conhecimento e o discernimento.

7Ele reserva a sensatez para o justo;

como um escudo protege quem anda com integridade,

8pois guarda a vereda do justo

e protege o caminho de seus fiéis.

9Então você entenderá o que é justo, direito e certo

e aprenderá os caminhos do bem.

10Pois a sabedoria entrará em seu coração,

e o conhecimento será agradável à sua alma.

11O bom senso o guardará,

e o discernimento o protegerá.

12A sabedoria o livrará do caminho dos maus,

dos homens de palavras perversas—

13que abandonam as veredas retas

para andarem por caminhos de trevas—,

14têm prazer em fazer o mal,

exultam com a maldade dos perversos,

15andam por veredas tortuosas

e no caminho se extraviam.

16Ela também o livrará da mulher imoral,

da pervertida2.16 Hebraico: estrangeira. que seduz com suas palavras,

17que abandona aquele que desde a juventude foi seu companheiro

e ignora a aliança que fez diante de Deus2.17 Ou aliança de seu Deus.

18A mulher imoral se dirige para a morte, que é a sua casa,

e os seus caminhos levam às sombras2.18 Hebraico: refaim. Isto é, os espíritos dos mortos..

19Os que a procuram jamais voltarão,

nem tornarão a encontrar as veredas da vida.

20A sabedoria o fará andar nos caminhos dos homens de bem

e manter-se nas veredas dos justos.

21Pois os justos habitarão na terra,

e os íntegros nela permanecerão;

22mas os ímpios serão eliminados da terra,

e dela os infiéis serão arrancados.