Miyambo 2 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 2:1-22

Ubwino Wanzeru

1Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga

ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,

2ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru

ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;

3ngati upempha kuti uzindikire zinthu

inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,

4ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva

ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,

5ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova;

ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.

6Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru,

ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.

7Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo.

Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,

8pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama.

Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.

9Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo,

kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.

10Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako,

kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.

11Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga;

kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.

12Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa,

kwa anthu amabodza,

13amene amasiya njira zolungama

namayenda mʼnjira zamdima,

14amene amakondwera pochita zoyipa

namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.

15Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota,

ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.

16Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo;

kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,

17amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake

ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.

18Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa;

njira zake zimamufikitsa ku manda.

19Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera

kapena kupezanso njira zamoyo.

20Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino,

uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.

21Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko

ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;

22Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo,

ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

箴言 2:1-22

智慧的益處

1孩子啊,

你若接受我的教誨,

珍愛我的誡命,

2側耳聆聽智慧,

傾心渴慕悟性;

3你若呼求洞見,

竭力追求悟性,

4尋它如尋銀子,

找它如找寶藏,

5你就會懂得敬畏耶和華,

認識上帝。

6因為耶和華賜人智慧,

知識和悟性出自祂的口。

7祂使正直人充滿智慧,

是行為純全者的盾牌。

8祂看守正義之路,

護衛虔誠人的道。

9這樣,你就明白何為仁義、

公平和正直,

懂得一切美善之道。

10因為智慧必進入你心,

知識必令你的靈歡快。

11明辨力必護佑你,

悟性必看顧你。

12智慧必救你遠離惡道,

脫離言語荒謬的人。

13他們捨棄正道,走上黑路,

14以行惡為樂,喜愛惡人的邪僻;

15他們的道路歪邪,行徑扭曲。

16智慧要救你脫離淫婦,

脫離花言巧語的妓女。

17她撇棄了年輕時的丈夫,

忘了在上帝面前立的約。

18她的家通向死亡,

她的路直達陰間。

19到她那裡的人都有去無回,

找不到生命之道。

20所以你要行善人的路,

守義人的道。

21因為在地上,

正直人必安居,

純全無過的人必長存,

22惡人必遭滅絕,

奸徒必被剷除。