Miyambo 19 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 19:1-29

1Ndi wabwino munthu wosauka amene amayenda mu ungwiro,

aposa munthu wopusa woyankhula zokhota.

2Si bwino kuti munthu akhale wopanda nzeru;

ndipo munthu woyenda mofulumira amaphonya njira.

3Uchitsiru wa munthu umamubweretsera zovuta,

mtima wake umakwiyira Yehova.

4Chuma chimachulukitsa abwenzi;

koma munthu wosauka bwenzi lake limamuthawa.

5Mboni yonama sidzalephera kulangidwa;

ndipo iye amene amanena mabodza sadzapulumuka.

6Anthu ambiri amafuna munthu wopatsa kuti awakomere mtima,

ndipo munthu amene amapereka mphatso ndi bwenzi la munthu aliyense.

7Ngati munthu wosauka abale ake omwe amadana naye,

nanji abwenzi ake tsono!

Iwo adzamuthawa kupita kutali.

Amayesa kuwatsatira mowapembedza koma iwo samapezeka konse.

8Iye amene amapeza nzeru ndiye kuti amakonda moyo wake.

Wosamalitsa kukhala wanzeru, zinthu zimamuyendera bwino.

9Mboni yonama sidzalephera kulangidwa,

ndipo iye amene amanena mabodza adzawonongeka.

10Nʼkosayenera kuti chitsiru chizikhala ndi moyo wamanyado,

nanjinso kuti kapolo azilamulira akalonga!

11Nzeru zimapangitsa munthu kukhala wosakwiya msanga;

ulemerero wake uli posalabadira kuchitiridwa zoyipa.

12Mkwiyo wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango,

koma kukoma mtima kwake kuli ngati mame pa udzu.

13Mwana wopusa ndiye tsoka la abambo ake

ndipo mkazi wolongolola ndi wotopetsa ngati mvula yamvumbi.

14Nyumba ndi chuma ndiye cholowa chochokera kwa makolo;

koma mkazi wanzeru ndi wochokera kwa Yehova.

15Ulesi umagonetsa tulo tofa nato

ndipo munthu wosatakataka amakhala ndi njala.

16Amene amamvera malangizo amasunga moyo wake,

koma amene sasamala malamulo a Yehova adzafa.

17Amene amakomera mtima osauka amachita ngati wakongoletsa Yehova,

ndipo Yehovayo ndiye adzamubwezere.

18Langa mwana wako, chiyembekezo chikanalipo;

ngati sutero udzawononga moyo wake.

19Munthu waukali woopsa ayenera kulandira chilango;

pakuti akamulekelera ndiye zidzayipa kuposa kale.

20Mvera uphungu ndipo landira malangizo;

pa mapeto pake udzakhala wanzeru.

21Munthu amakonzekera zambiri mu mtima mwake,

koma cholinga cha Yehova ndiye chidzachitike.

22Chimene munthu amafuna ndi chikondi chosatha;

nʼkwabwino kukhala wosauka kusiyana ndi kukhala wabodza.

23Kuopa Yehova kumabweretsa moyo;

wotereyo amakhala mu mtendere; ndiye kuti choyipa sichidzamugwera.

24Munthu waulesi amapisa dzanja lake mʼmbale;

koma sangathe kufikitsa dzanja lakelo pakamwa pake.

25Menya munthu wonyoza, ndipo anthu opanda nzeru adzachenjererapo;

dzudzula munthu wozindikira zinthu, ndipo iye adzapezapo chidziwitso.

26Mwana wochita ndewu ndi abambo ake ndi kuthamangitsa amayi ake,

ndi mwana wochititsa manyazi ndi wonyozetsa.

27Mwana wanga, ukaleka kumvera malangizo,

udzapatukana ndi mawu opatsa nzeru.

28Mboni yopanda pake imanyoza cholungama,

ndipo pakamwa pa anthu oyipa pamameza zoyipa.

29Chilango chakonzedwa kale kuti chigwere anthu oyipa,

ndipo mkwapulo wakonzedwa kale kuti ukwapule misana ya anthu opusa.

Korean Living Bible

잠언 19:1-29

1가난하지만 진실하게 사는 사람이 입술이 거짓되고 미련한 사람보다 낫다.

2지식 없는 19:2 또는 ‘영혼은’열심은 좋지 못하고 성급한 사람은 잘못이 많다.

3사람은 자기가 미련해서 앞길을 망치고서도 마음으로는 하나님을 원망한다.

4부유하면 새로운 친구가 계속 늘어나지만 가난하면 있던 친구도 떠나고 만다.

5거짓 증인은 벌을 면치 못할 것이며 거짓말을 토하는 자도 무사하지 못할 것이다.

6너그러운 사람에게 은혜를 구하는 자가 많고 선물을 주기 좋아하는 자에게 사람마다 친구가 되고 싶어한다.

7사람이 가난하면 형제들에게도 업신여김을 받는데 어찌 그 친구들이 그를 멀리하지 않겠는가! 아무리 가까이해 보려고 해도 그들을 만나기가 어려울 것이다.

8지혜를 얻는 사람이 자기 영혼을 사랑하고 통찰력을 가진 사람이 성공할 것이다.

9거짓 증인은 벌을 면치 못할 것이며 거짓말쟁이는 망하고 말 것이다.

10미련한 자가 사치하는 것이 마땅치 않으며 종이 귀족을 다스리는 것도 마땅치 못하다.

11분노를 참는 것이 사람의 슬기이며 남의 허물을 덮어 주는 것이 자기의 영광이다.

12왕의 분노는 사자의 부르짖음 같고 왕의 은혜는 풀밭의 이슬 같다.

13미련한 아들은 그 아버지의 파멸이며 잔소리 심한 아내는 쉴 사이 없이 떨어지는 물방울과 같다.

14집과 재산은 부모에게서 물려받지만 슬기로운 아내는 여호와께서 주시는 선물이다.

15사람이 게으르면 잠은 실컷 잘지 모르지만 결국 굶주리게 될 것이다.

16계명을 지키는 사람은 자기 영혼을 지키지만 자기 행실을 조심하지 않는 사람은 죽게 될 것이다.

17가난한 사람을 돕는 것은 여호와께 빌려 주는 것이니 여호와께서 그의 선행을 반드시 갚아 주실 것이다.

18아직 희망이 있을 때 자녀를 징계하라. 그러나 죽일 마음은 품지 말아라.

19성질이 불 같은 사람은 그 결과에 대해서 자신이 책임을 지게 하라. 만일 그런 사람을 한번 구해 주게 되면 계속해서 그를 구해 주어야 할 것이다.

20남의 충고를 귀담아 듣고 훌륭한 사람들의 가르침을 잘 받아라. 그러면 네가 지혜롭게 될 것이다.

21사람이 여러 가지 계획을 세워도 여호와의 뜻만 이루어진다.

22탐심은 부끄러운 것이니 가난한 자가 거짓말쟁이보다 낫다.

23여호와를 두려워하는 것이 사는 길이다. 여호와를 두려워하는 사람은 재앙을 받지 않고 만족한 삶을 누릴 것이다.

24게으른 자는 손을 그릇에 넣고도 입에 갖다 넣기를 싫어한다.

25거만한 자를 벌하라. 어리석은 자가 각성할 것이다. 식별력이 있는 사람을 책망하라. 그러면 그가 지혜로운 사람이 될 것이다.

26자기 아버지를 구박하고 자기 어머니를 쫓아내는 자는 파렴치한 아들이다.

27내 아들아, 지식의 말씀에서 떠나게 하는 교훈을 듣지 말아라.

28악한 증인은 진실을 무시하고 죄 짓는 일을 물 먹듯이 한다.

29형벌은 거만한 자를 위해 마련되었고 채찍은 어리석은 자의 등을 위해 마련되었다.