Miyambo 18 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 18:1-24

1Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha;

iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.

2Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu,

koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.

3Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera.

Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.

4Mawu a munthu ali ngati madzi akuya,

kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.

5Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu;

kapena kupondereza munthu wosalakwa.

6Mawu a chitsiru amautsa mkangano;

pakamwa pake pamayitana mkwapulo.

7Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake,

ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.

8Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma;

amalowa mʼmimba mwa munthu.

9Munthu waulesi pa ntchito yake

ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.

10Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba;

wolungama amathawiramo napulumuka.

11Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba;

chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.

12Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada,

koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.

13Ukayankha usanamvetse bwino nkhani,

umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.

14Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda,

koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.

15Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina;

amafunafuna kudziwa bwino zinthu.

16Mphatso ya munthu imamutsekulira njira

yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.

17Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye

mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.

18Kuchita maere kumathetsa mikangano;

amalekanitsa okangana amphamvu.

19Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba,

koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.

20Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake.

Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.

21Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo.

Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.

22Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino

ndipo Yehova amamukomera mtima.

23Munthu wosauka amapempha

koma munthu wolemera amayankha mwaukali.

24Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso,

koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.

New Russian Translation

Притчи 18:1-24

1Живущий обособленно потакает себе во всем,

а на всякое здравое слово бранится18:1 Смысл этого места в еврейском тексте неясен..

2Нет глупцу радости в понимании –

рад он лишь высказать свое мнение.

3Вслед за нечестием идет презрение,

а со срамом приходит бесславие.

4Слова человеческих уст – глубокие воды18:4 Глубокие воды – это выражение можно понимать двояко: 1) слова людей, зачастую, скрытны, неоднозначны, темны как глубокие воды; 2) слова, сказанные мудрым человеком, несут в себе глубокие мысли.;

источник мудрости – текущий поток.

5Нехорошо быть пристрастным к злодею

и лишать правосудия невиновного18:5 Или: «праведника»..

6Язык глупца ведет его к ссоре,

его уста навлекают побои.

7Уста глупца – его гибель,

его язык – для него же западня.

8Слова сплетен – как лакомые куски,

что проходят вовнутрь чрева.

9Ленивый в своей работе –

брат разрушителя.

10Имя18:10 Имя – в древности имя несло в себе важную информацию, будучи большим, чем просто личное название кого-либо. Оно говорило, кем является данная личность, раскрывая его природу и характер. Другими словами, имя Господне – Сам Господь. Господне – крепкая башня;

убежит в нее праведник – и будет спасен.

11Состояние богатого – укрепленный город;

высокой стеной представляется ему оно.

12Перед падением человеческое сердце заносится,

а смирение предшествует славе.

13Отвечать, не выслушав,

это глупость и стыд.

14Дух человека подкрепляет его в болезни,

но если дух сокрушен – кто в силах снести его?

15Разум рассудительного приобретает знание,

и уши мудрых ищут его.

16Подарок открывает человеку путь

и приводит его к вельможам.

17Кто первым изложит дело, тот выглядит правым,

пока другой не придет и его не расспросит.

18Жребий решает споры,

и разнимает сильных соперников.

19Обиженный брат неприступнее крепости;

ссоры разделяют подобно засовам ворот.

20Красноречием человек может наполнять свой желудок,

Словами своими – зарабатывать себе на жизнь18:20 Букв.: «Плодами уст человек может наполнять свой желудок; он насыщается жатвой своего языка»..

21У языка – сила жизни и смерти,

те, кто любит его, будут вкушать его плоды.

22Нашедший жену нашел благо

и приобрел от Господа расположение.

23Бедняк о милости молит,

а богач отвечает грубо.

24Есть друзья, с которыми лучше не знаться18:24 Или: «Иные друзья лишь играют в дружбу». Смысл этого места в еврейском тексте неясен.,

но истинный друг ближе иного брата.