Miyambo 18 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 18:1-24

1Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha;

iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.

2Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu,

koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.

3Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera.

Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.

4Mawu a munthu ali ngati madzi akuya,

kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.

5Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu;

kapena kupondereza munthu wosalakwa.

6Mawu a chitsiru amautsa mkangano;

pakamwa pake pamayitana mkwapulo.

7Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake,

ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.

8Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma;

amalowa mʼmimba mwa munthu.

9Munthu waulesi pa ntchito yake

ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.

10Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba;

wolungama amathawiramo napulumuka.

11Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba;

chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.

12Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada,

koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.

13Ukayankha usanamvetse bwino nkhani,

umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.

14Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda,

koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.

15Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina;

amafunafuna kudziwa bwino zinthu.

16Mphatso ya munthu imamutsekulira njira

yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.

17Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye

mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.

18Kuchita maere kumathetsa mikangano;

amalekanitsa okangana amphamvu.

19Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba,

koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.

20Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake.

Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.

21Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo.

Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.

22Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino

ndipo Yehova amamukomera mtima.

23Munthu wosauka amapempha

koma munthu wolemera amayankha mwaukali.

24Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso,

koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Proverbios 18:1-24

1El egoísta busca su propio bien;

contra todo sano juicio se rebela.

2Al necio no le complace el discernimiento;

tan solo hace alarde de su propia opinión.

3Con la maldad viene el desprecio,

y con la vergüenza llega el oprobio.

4Las palabras del hombre son aguas profundas,

arroyo de aguas vivas, fuente de sabiduría.

5No está bien declarar inocente al18:5 declarar inocente al. Lit. levantar el rostro del. malvado

y dejar de lado los derechos del justo.

6Los labios del necio son causa de contienda;

su boca incita a la riña.

7La boca del necio es su perdición;

sus labios son para él una trampa mortal.

8Los chismes son deliciosos manjares;

penetran hasta lo más íntimo del ser.

9El que es negligente en su trabajo

confraterniza con el que es destructivo.

10Torre inexpugnable es el nombre del Señor;

a ella corren los justos y se ponen a salvo.

11Ciudad amurallada es la riqueza para el rico,

y este cree que sus muros son inexpugnables.

12Al fracaso lo precede la soberbia humana;

a los honores los precede la humildad.

13Es necio y vergonzoso

responder antes de escuchar.

14En la enfermedad, el ánimo levanta al enfermo;

¿pero quién podrá levantar al abatido?

15El corazón prudente adquiere conocimiento;

los oídos de los sabios procuran hallarlo.

16Con regalos se abren todas las puertas

y se llega a la presencia de gente importante.

17El primero en presentar su caso parece inocente,

hasta que llega la otra parte y lo refuta.

18El echar suertes pone fin a los litigios

y decide entre las partes en pugna.

19Más resiste el hermano ofendido que una ciudad amurallada;

los litigios son como cerrojos de ciudadela.

20Cada uno se llena con lo que dice

y se sacia con lo que habla.

21En la lengua hay poder de vida y muerte;

quienes la aman comerán de su fruto.

22Quien halla esposa halla la felicidad:

muestras de su favor le ha dado el Señor.

23El pobre habla en tono suplicante;

el rico responde con aspereza.

24Hay amigos18:24 Hay amigos (LXX, Siríaca y Targum); Hombre de amigos (TM). que llevan a la ruina,

y hay amigos más fieles que un hermano.