Miyambo 17 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 17:1-28

1Nʼkwabwino kudya mkute koma pali mtendere,

kuposa kuchita madyerero mʼnyumba mʼmene muli mikangano.

2Kapolo wanzeru adzalamulira mwana wochititsa manyazi,

ndipo kapoloyo adzagawana nawo cholowa ngati mmodzi mwa abale.

3Siliva amamuyesa mʼngʼanjo ndipo golide amamuyesa mʼngʼanjo,

koma Yehova amayesa mitima.

4Munthu woyipa amamvera malangizo oyipa;

munthu wabodza amatchera khutu mawu osakaza.

5Iye amene amalalatira mʼmphawi amanyoza mlengi wake;

amene amakondwerera tsoka la mnzake sadzakhala osalangidwa.

6Zidzukulu ndiye ulemu wa anthu okalamba,

ndipo makolo ndiye ulemerero wa ana.

7Kuyankhula bwino sikuyenerana ndi chitsiru,

nanji kuyankhula bodza kungayenerane kodi ndi mfumu?

8Chiphuphu chili ngati mankhwala amwayi kwa wochiperekayo;

kulikonse kumene amapita zinthu zimamuyendera.

9Iye amene amakhululukira zolakwa za wina, amafunitsitsa chikondi;

wobwerezabwereza nkhani amapha chibwenzi.

10Munthu wanzeru amamva kamodzi kokha,

munthu wopanda nzeru ndi samvamkunkhu.

11Munthu woyipa maganizo ake ali pa kuwukira basi;

ndipo bwana adzamutumizira wamthenga wankhanza.

12Nʼkwabwino kukumana ndi chimbalangondo cholandidwa ana ake

kusiyana ndi kukumana ndi chitsiru mu uchitsiru wake.

13Ngati munthu abwezera choyipa kusinthana ndi zabwino,

ndiye choyipa sichidzachoka mʼnyumba mwake.

14Chiyambi cha mikangano chili ngati kukhamulira madzi,

choncho uzichokapo mkangano usanayambe.

15Kumasula munthu wolakwa kapena kumanga munthu wosalakwa,

zonse ziwirizi Yehova zimamunyansa.

16Ndalama zogulira nzeru zili ndi phindu lanji mʼmanja mwa chitsiru

poti iyeyo mutu wake sumayenda bwino?

17Bwenzi lako limakukonda nthawi zonse,

ndipo mʼbale wako anabadwa kuti azikuthandiza pamavuto.

18Munthu wopanda nzeru amavomereza zopereka chikole

ndipo iyeyo amasanduka chikole cha mnansi wake.

19Wokonda zolakwa amakonda mkangano,

ndipo wokonda kuyankhula zonyada amadziyitanira chiwonongeko.

20Munthu wamtima woyipa zinthu sizimuyendera bwino;

ndipo woyankhula zachinyengo amagwa mʼmavuto.

21Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake,

abambo a chitsiru sakhala ndi chimwemwe.

22Mtima wosangalala uli ngati mankhwala abwino,

koma mtima wokhumudwa umafowoketsa mafupa.

23Munthu woyipa amalandira chiphuphu chamseri

kuti apotoze chiweruzo cholungama.

24Munthu wozindikira zinthu, maso ake amakhala pa nzeru,

koma chitsiru chimwazamwaza maso ake pa dziko lonse lapansi.

25Mwana wopusa amamvetsa chisoni abambo ake

ndipo amapweteketsa mtima amayi ake.

26Sibwino kulipitsa munthu wosalakwa,

kapena kulanga anthu osalakwa.

27Munthu wosunga pakamwa ndiye wodziwa zinthu,

ndipo wodekha mtima ndiye womvetsa bwino zinthu.

28Ngakhale chitsiru chimakhala ngati chanzeru chikakhala chete;

ndipo chikatseka pakamwa chimakhala ngati munthu wochenjera.

New International Reader’s Version

Proverbs 17:1-28

1It is better to eat a dry crust of bread in peace and quiet

than to eat a big dinner in a house full of fighting.

2A wise servant will rule over a shameful child.

He will be given part of the property as if he were a family member.

3Fire tests silver, and heat tests gold.

But the Lord tests our hearts.

4Evil people listen to lies.

Lying people listen to evil.

5Anyone who laughs at those who are poor makes fun of their Maker.

Anyone who is happy when others suffer will be punished.

6Grandchildren are like a crown to older people.

And children are proud of their parents.

7Fancy words don’t belong in the mouths of ungodly fools.

And lies certainly don’t belong in the mouths of rulers!

8Those who give money think it will buy them favors.

They think that no matter where they turn, they will succeed.

9Whoever wants to show love forgives a wrong.

But those who talk about it separate close friends.

10A person who understands what is right learns more from just a warning

than a foolish person learns from 100 strokes with a whip.

11An evil person tries to keep others from obeying God.

The messenger of death will be sent against them.

12It is better to meet a bear whose cubs have been stolen

than to meet a foolish person who is acting foolishly.

13Evil will never leave the house

of anyone who pays back evil for good.

14Starting to argue is like making a crack in a dam.

So drop the matter before a fight breaks out.

15The Lord hates two things.

He hates it when the guilty are set free.

He also hates it when those who aren’t guilty are punished.

16Why should a foolish person try to buy wisdom?

They are not even able to understand it.

17A friend loves at all times.

They are there to help when trouble comes.

18A person who has no sense agrees to pay what other people owe.

It isn’t wise to promise to pay other people’s bills.

19The one who loves to argue loves to sin.

The one who builds a high gate is just asking to be destroyed.

20If your heart is twisted, you won’t succeed.

If your tongue tells lies, you will get into trouble.

21It is sad to have a foolish child.

The parents of a godless fool have no joy.

22A cheerful heart makes you healthy.

But a broken spirit dries you up.

23Anyone who does wrong accepts favors in secret.

Then they turn what is right into what is wrong.

24Anyone who understands what is right keeps wisdom in view.

But the eyes of a foolish person look everywhere else.

25A foolish child makes his father sad

and his mother sorry.

26It isn’t good to fine those who aren’t guilty.

So it certainly isn’t good to whip officials just because they are honest.

27Anyone who has knowledge controls their words.

Anyone who has understanding is not easily upset.

28We think even foolish people are wise if they keep silent.

We think they understand what is right if they control their tongues.