Miyambo 16 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 16:1-33

1Zolinga za mu mtima ndi za munthu,

koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.

2Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake,

koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.

3Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova,

ndipo zolinga zako zidzachitikadi.

4Yehova amachita zonse ndi cholinga chake,

ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.

5Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova.

Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.

6Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake;

chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.

7Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova,

ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.

8Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo,

kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.

9Mtima wa munthu umalingalira zochita,

koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.

10Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu;

ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.

11Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova;

miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.

12Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu,

pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.

13Mawu owona amakondweretsa mfumu.

Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.

14Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa,

koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.

15Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo;

ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.

16Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide.

Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.

17Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa;

wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.

18Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko,

ndipo munthu wodzikuza adzagwa.

19Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa,

kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.

20Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino,

ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.

21A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu,

ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.

22Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako,

koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.

23Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru,

ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.

24Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi,

amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.

25Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu

koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.

26Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira;

njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.

27Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa

ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.

28Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano,

ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.

29Munthu wandewu amakopa mnansi wake,

ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.

30Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota;

amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.

31Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero;

munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.

32Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo,

munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.

33Maere amaponyedwa pa mfunga,

koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

箴言 16:1-33

1心中的策劃在於人,

應對之言來自耶和華。

2人看自己的行為都純全,

但是耶和華卻衡量人心。

3把你的事交托耶和華,

你的計劃必實現。

4耶和華所造的萬物各有其用,

連惡人也是為災難之日所造。

5耶和華厭惡心驕氣傲者,

他們必逃不過祂的責罰。

6慈愛和忠信可讓罪惡得贖,

敬畏耶和華使人遠離罪惡。

7人所行的若蒙耶和華喜悅,

耶和華必使仇敵與他和好。

8財物雖少但行事公義,

勝過家財萬貫卻不公義。

9人心中籌畫自己的道路,

但耶和華決定他的腳步。

10王口中有上帝的話,

斷案時必無差錯。

11公道的秤與天平屬於耶和華,

袋中一切的法碼由祂制定。

12君王憎恨惡行,

因王位靠公義而立。

13王喜愛公義的言詞,

器重說話正直的人。

14王的烈怒如死亡使者,

然而智者能平息王怒。

15王的笑容帶給人生命,

他的恩惠像春雨之雲。

16得智慧勝過得黃金,

獲悟性勝過獲白銀。

17正直人的大道遠離罪惡,

堅守正道的保全性命。

18驕橫是淪亡的前奏,

狂傲是敗落的預兆。

19寧可謙卑地與貧寒人相處,

也不跟狂傲人共享戰利品。

20聽從訓言的人受益匪淺,

信靠耶和華的人蒙祝福。

21智者以明辨著稱,

甜言能說服人心。

22智慧是智者的生命泉,

愚昧為愚人帶來懲罰。

23智者三思而後言,

其言使人長見識。

24良言如蜜,

使人心靈甘甜、身體康健。

25有一條路看似正確,

最終卻通向死亡。

26工人的胃口促他工作,

口腹之需是他的動力。

27不務正業的人圖謀惡事,

他的口舌如烈焰般危險。

28邪僻的人散播紛爭,

造謠的人破壞友情。

29殘暴之徒引誘鄰舍走入歧途。

30惡人眯起眼睛圖謀不軌,

歹徒咬著嘴唇策劃惡事。

31白髮是榮耀的冠冕,

行為公義方能得到。

32不輕易發怒者勝過勇士,

能自我控制勝過攻陷城池。

33人可以搖籤求問,

但耶和華決定一切。