Miyambo 15 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 15:1-33

1Kuyankha kofatsa kumathetsa mkwiyo,

koma mawu ozaza amautsa ukali.

2Munthu wanzeru amayankhula zinthu za nzeru,

koma pakamwa pa zitsiru pamatulutsa za uchitsiru.

3Maso a Yehova ali ponseponse,

amayangʼana pa oyipa ndi abwino omwe.

4Kuyankhula kodekha kuli ngati mtengo wopatsa moyo,

koma kuyankhula kopotoka kumapweteka mtima.

5Chitsiru chimanyoza mwambo wa abambo ake,

koma wochenjera amasamala chidzudzulo.

6Munthu wolungama amakhala ndi chuma chambiri,

zimene woyipa amapindula nazo zimamugwetsa mʼmavuto.

7Pakamwa pa anthu anzeru pamafalitsa nzeru;

koma mitima ya zitsiru sitero.

8Nsembe za anthu oyipa zimamunyansa Yehova,

koma amakondwera ndi pemphero la anthu owona mtima.

9Ntchito za anthu oyipa zimamunyansa Yehova

koma amakonda amene amafunafuna chilungamo.

10Amene amasiya njira yabwino adzalangidwa koopsa.

Odana ndi chidzudzulo adzafa.

11Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova,

nanji mitima ya anthu!

12Wonyoza sakonda kudzudzulidwa;

iye sapita kwa anthu anzeru.

13Mtima wokondwa umachititsa nkhope kukhala yachimwemwe,

koma mtima wosweka umawawitsa moyo.

14Mtima wa munthu wozindikira zinthu umafunafuna nzeru,

koma pakamwa pa zitsiru pamadya uchitsiru wawo.

15Munthu woponderezedwa masiku ake onse amakhala oyipa,

koma mtima wachimwemwe umakhala pa chisangalalo nthawi zonse.

16Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono nʼkumaopa Yehova,

kusiyana ndi kukhala ndi chuma chambiri uli pamavuto.

17Kuli bwino kudyera ndiwo zamasamba pamene pali chikondi,

kusiyana ndi kudyera nyama yangʼombe yonenepa pamene pali udani.

18Munthu wopsa mtima msanga amayambitsa mikangano,

koma munthu woleza mtima amathetsa ndewu.

19Njira ya munthu waulesi ndi yowirira ndi mtengo waminga,

koma njira ya munthu wolungama ili ngati msewu waukulu.

20Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake,

koma mwana wopusa amanyoza amayi ake.

21Uchitsiru umakondweretsa munthu wopanda nzeru,

koma munthu womvetsa zinthu amayenda mowongoka.

22Popanda uphungu zolinga zako munthu zimalephereka,

koma pakakhala aphungu ambiri zolinga zimatheka.

23Munthu amakondwera ndi kuyankha koyenera,

ndipo mawu onena pa nthawi yake ndi okoma.

24Munthu wanzeru amatsata njira yopita ku moyo

kuti apewe malo okhala anthu akufa.

25Yehova amapasula nyumba ya munthu wonyada

koma amasamalira malo a mkazi wamasiye.

26Maganizo a anthu oyipa amamunyansa Yehova,

koma mawu a anthu oyera mtima amamusangalatsa.

27Munthu wofuna phindu mwachinyengo amavutitsa banja lake,

koma wodana ndi ziphuphu adzakhala ndi moyo.

28Munthu wolungama amaganizira za mmene ayankhire,

koma pakamwa pa munthu woyipa pamatulutsa mawu oyipa.

29Yehova amakhala kutali ndi anthu oyipa,

koma amamva pemphero la anthu olungama.

30Kuwala kwa maso kumasangalatsa mtima

ndipo uthenga wabwino umalimbitsa munthu.

31Womvera mawu a chidzudzulo amene apatsa moyo

adzakhala pakati pa anthu anzeru.

32Amene amanyoza mwambo amadzinyoza yekha,

koma womvera mawu a chidzudzulo amapeza nzeru zomvetsa zinthu.

33Kuopa Yehova kumaphunzitsa munthu nzeru,

ndipo kudzichepetsa ndi ulemu chili patsogolo ndi kudzichepetsa.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Proverbios 15:1-33

1La respuesta amable calma el enojo,

pero la agresiva echa leña al fuego.

2La lengua de los sabios destila conocimiento;15:2 destila conocimiento (LXX); hace bien al conocimiento (TM).

la boca de los necios escupe necedades.

3Los ojos del Señor están en todo lugar,

vigilando a los buenos y a los malos.

4La lengua que brinda alivio15:4 que brinda alivio. Lit. que sana. es árbol de vida;

la lengua insidiosa deprime el espíritu.

5El necio desdeña la corrección de su padre;

el que la acepta demuestra prudencia.

6En la casa del justo hay gran abundancia;

en las ganancias del malvado, grandes problemas.

7Los labios de los sabios esparcen conocimiento;

el corazón de los necios ni piensa en ello.

8El Señor aborrece las ofrendas de los malvados,

pero se complace en la oración de los justos.

9El Señor aborrece el camino de los malvados,

pero ama a quienes siguen la justicia.

10Para el descarriado, disciplina severa;

para el que aborrece la corrección, la muerte.

11Si ante el Señor están el sepulcro y la muerte,

¡cuánto más el corazón humano!

12Al insolente no le gusta que lo corrijan,

ni busca la compañía de los sabios.

13El corazón alegre se refleja en el rostro,

el corazón dolido deprime el espíritu.

14El corazón entendido va tras el conocimiento;

la boca de los necios se nutre de tonterías.

15Para el afligido todos los días son malos;

para el que es feliz todos son de fiesta.

16Más vale tener poco con temor del Señor

que muchas riquezas con grandes angustias.

17Más vale comer verduras sazonadas con amor

que un festín de carne15:17 que un festín de carne. Lit. que toro engordado. sazonada con odio.

18El que es iracundo provoca contiendas;

el que es paciente las apacigua.

19El camino del perezoso está plagado de espinas,

pero la senda del justo es como una calzada.

20El hijo sabio alegra a su padre;

el hijo necio menosprecia a su madre.

21Al necio le divierte su falta de juicio;

el entendido endereza sus propios pasos.

22Cuando falta el consejo, fracasan los planes;

cuando abunda el consejo, prosperan.

23Es muy grato dar la respuesta adecuada,

y más grato aún cuando es oportuna.

24El sabio sube por el sendero de vida,

para librarse de caer en el sepulcro.

25El Señor derriba la casa de los soberbios,

pero mantiene intactos los linderos de las viudas.

26El Señor aborrece los planes de los malvados,

pero se complace en las palabras puras.

27El ambicioso acarrea mal sobre su familia;

el que aborrece el soborno vivirá.

28El corazón del justo medita sus respuestas,

pero la boca del malvado rebosa de maldad.

29El Señor se mantiene lejos de los impíos,

pero escucha las oraciones de los justos.

30Una mirada radiante alegra el corazón,

y las buenas noticias renuevan las fuerzas.15:30 las fuerzas. Lit. los huesos.

31El que atiende a la crítica edificante

habitará entre los sabios.

32El que rechaza la corrección se desprecia a sí mismo;

el que la atiende gana entendimiento.

33El temor del Señor imparte sabiduría;

la humildad precede a la honra.