Miyambo 14 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 14:1-35

1Mkazi wanzeru amamanga banja lake,

koma mkazi wopusa amalimasula ndi manja ake omwe.

2Amene amayenda molungama amaopa Yehova,

koma amene njira zake ndi zoyipa amanyoza Yehova.

3Kuyankhula kwa chitsiru kumamuyitanira ndodo pa msana,

koma milomo ya munthu wanzeru imamuteteza.

4Pakasowa ngʼombe zolima gome limakhala lopanda chakudya,

koma pakakhala ngʼombe zamphamvu zakudya zimachulukanso.

5Mboni yokhulupirika sinama,

koma mboni yonyenga imayankhula zabodza.

6Wonyoza anzake amafunafuna nzeru koma osayipeza,

koma munthu womvetsa bwino amadziwa zinthu msanga.

7Khala kutali ndi munthu wopusa

chifukwa sudzapeza mawu a nzeru.

8Nzeru za munthu wochenjera zagona pakuzindikira njira zake.

Koma uchitsiru wa zitsiru umapusitsidwa ndi chinyengo chawo chomwe.

9Zitsiru zimanyoza za kulapa machimo, awo,

koma kufuna kwabwino kumapezeka mwa anthu olungama.

10Mtima uliwonse umadziwa wokha zowawa zake,

ndipo palibe wina aliyense angadziwe kukondwa kwake.

11Nyumba ya munthu woyipa idzapasuka,

koma tenti ya munthu wowongoka mtima idzakhazikika.

12Pali njira ina yooneka ngati yabwino kwa munthu,

koma kumatsiriziro kwake ndi ku imfa.

13Ngakhale poseka mtima utha kumva kuwawa,

ndipo mathero achimwemwe akhoza kukhala chisoni.

14Munthu wosakhulupirika adzalandira zogwirizana ndi ntchito yake,

koma munthu wabwino adzalandira mphotho ya ntchito yake.

15Munthu wopusa amakhulupirira chilichonse,

koma munthu wochenjera amaganizira bwino mayendedwe ake.

16Munthu wanzeru amaopa Mulungu ndipo amapewa zoyipa,

koma munthu wopusa ndi wokula mtima amakhala wosasamala.

17Munthu wopsa mtima msanga amachita zinthu za uchitsiru,

ndipo anthu amadana ndi munthu wachinyengo.

18Anthu opusa amalandira uchitsiru,

koma anthu ochenjera amavekedwa chipewa cha ulemerero wa kudziwa zinthu.

19Anthu oyipa adzagwada pamaso pa anthu abwino,

ndipo anthu oyipa adzapempha thandizo kwa anthu olungama.

20Munthu wosauka ngakhale anansi ake omwe amamuda,

koma munthu wolemera ali ndi abwenzi ambiri.

21Wonyoza mnansi wake ndi wochimwa

koma ndi wodala amene amachitira chifundo anthu osowa.

22Kodi amene amakonzekera zoyipa sasochera?

Koma amene amakonzekera zabwino anthu amawaonetsa chikondi ndi kukhulupirika.

23Ntchito iliyonse imakhala ndi phindu,

koma kuyankhulayankhula kumabweretsa umphawi.

24Chipewa chaulemu cha anthu a nzeru ndi chuma chawo chomwe,

koma malipiro a zitsiru ndi uchitsiru.

25Mboni yokhulupirika imapulumutsa miyoyo,

koma mboni yabodza imaphetsa.

26Amene amaopa Yehova ali ndi chitetezo chokwanira

ndipo iye adzakhala pothawira pa ana ake.

27Kuopa Yehova ndiye kasupe wamoyo,

kumathandiza munthu kuti apewe msampha wa imfa.

28Gulu lalikulu la anthu ndiye ulemerero wa mfumu,

koma popanda anthu kalonga amawonongeka.

29Munthu wosapsa mtima msanga amamvetsa zinthu kwambiri,

koma munthu wopsa mtima msanga amaonetsa uchitsiru wake.

30Mtima wodekha umapatsa thupi moyo,

koma nsanje imawoletsa mafupa.

31Amene amapondereza mʼmphawi amanyoza mlengi wake,

koma wochitira chifundo munthu wosowa amalemekeza Mulungu.

32Anthu oyipa adzakanthidwa chifukwa cha ntchito zawo zomwe,

koma olungama adzatetezedwa mwa imfa yawo.

33Nzeru zimakhala mu mtima mwa anthu omvetsa zinthu,

koma nzeru sipezeka mu mtima mwa zitsiru.

34Chilungamo chimakweza mtundu wa anthu,

koma uchimo umachititsa manyazi mtundu uliwonse.

35Mfumu imasangalatsidwa ndi wantchito wanzeru,

koma imachitira ukali wantchito wochititsa manyazi.

Luganda Contemporary Bible

Engero 14:1-35

114:1 Nge 24:3Omukazi ow’amagezi yeezimbira ennyumba ye,

naye omusirusiru eyiye agyemenyera n’emikono gye.

2Omuntu atambulira mu bugolokofu atya Mukama,

naye ow’amakubo amakyamu anyooma Mukama.

314:3 Nge 12:6Ebigambo by’omusirusiru bye bimuviirako okukubwa,

naye eby’abatuukirivu binaabakuumanga.

4Awataba nte nnume ezirima ebyagi biba bikalu,

naye emmere ennyingi eva mu maanyi gaazo.

514:5 Nge 6:19; 12:17Omujulizi ow’amazima talimba,

naye ow’obulimba ayogera bya bulimba.

6Omukudaazi anoonya amagezi n’atagalaba,

naye okumanya kwanguyira omuntu ategeera.

7Teweeretereza muntu musirusiru,

kubanga tewali by’amagezi biva mu kamwa ke.

814:8 nny 24Omutegeevu mugezi kubanga afaayo okutegeera by’akola,

naye atalina magezi musirusiru kubanga yeerimba nti amanyi.

9Abasirusiru banyooma okugololwa nga bakoze ensobi,

naye abalongoofu baagala emirembe.

10Buli mutima gumanya okulumwa kwagwo,

tewali ayinza kugusanyukirako.

1114:11 Nge 3:33; 12:7Ennyumba y’abakozi b’ebibi erizikirizibwa,

naye eweema y’abatuukirivu erikulaakulana.

1214:12 a Nge 12:15 b Nge 16:25Waliwo ekkubo erirabika nga ttuufu eri omuntu,

naye ng’enkomerero yaalyo kufa.

1314:13 Mub 2:2Enseko zandibaawo naye ng’omutima gujjudde ennaku,

era n’enkomerero y’essanyu eyinza okufuuka obuyinike.

1414:14 a Nge 1:31 b Nge 12:14Omuntu atalina kukkiriza alisasulwa empeera emusaanira olw’ebikolwa bye,

n’omuntu omulungi naye alisasulwa eyiye.

15Ow’amagezi amatono amala gakkiriza buli kigambo ky’awulira,

naye omuntu omutegeevu yeegendereza amakubo ge.

1614:16 Nge 22:3Omuntu ow’amagezi atya Mukama n’aleka okukola ebibi,

naye omusirusiru yeepankapanka era teyeegendereza.

1714:17 nny 29Omuntu asunguwala amangu akola eby’obusirusiru,

n’omukalabakalaba akyayibwa.

18Abatalina magezi basikira butaliimu,

naye abategeevu batikkirwa engule ey’okumanya.

1914:19 Nge 11:29Abakozi b’ebibi balivuunamira abatuukirivu,

n’aboonoonyi ne bavuunama mu miryango gy’abatuukirivu.

Omugagga n’Omwavu

2014:20 Nge 19:4, 7Omwavu alagajjalirwa abantu nga ne muliraanwa we omutwaliddemu,

naye abagagga baba n’emikwano mingi.

2114:21 a Nge 11:12 b Zab 41:1; Nge 19:17Anyooma muliraanwa we akola kibi,

naye alina omukisa oyo asaasira abaavu.

22Abateekateeka okukola ebibi, tebawaba?

Naye okwagala n’amazima binaabeeranga n’abo abateesa okukola obulungi.

23Buli mulimu ogukolebwa n’amaanyi gubaako amagoba,

naye okwogera obwogezi kireeta bwavu bwokka.

24Abagezi bafuna engule ey’obugagga,

naye obusirusiru bw’abatalina magezi buzaala busirusiru.

2514:25 nny 5Omujulizi ow’amazima awonya obulamu bw’abantu,

naye omujulizi ow’obulimba aba mulimba.

2614:26 Nge 18:10; 19:23; Is 33:6Atya Mukama alina ekiddukiro eky’amaanyi,

era n’abaana be balibeera n’obuddukiro.

2714:27 Nge 13:14Okutya Mukama ye nsulo y’obulamu,

kuleetera omuntu okwewala emitego gy’okufa.

28Ekitiibwa kya kabaka kiri mu kuba n’abantu bangi,

naye omukulembeze ataba n’abantu abeera mu kabi.

2914:29 Mub 7:8-9; Yak 1:19Omuntu omugumiikiriza aba n’okutegeera kungi,

naye oyo asunguwala amangu ayolesa obusirusiru.

3014:30 Nge 12:4Omutima ogulina emirembe guwangaaza omuntu,

naye obuggya buvunza amagumba ge.

3114:31 Nge 17:5Omuntu atulugunya abaavu anyooma oyo eyabatonda,

naye buli abakwatirwa ekisa, agulumiza Katonda.

3214:32 a Nge 6:15 b Yob 13:15; 2Ti 4:18Akacwano bwe kajja, omukozi w’ebibi agwa,

naye omutuukirivu ne mu kufa aba n’obuddukiro.

3314:33 Nge 2:6-10Amagezi gabeera mu mutima gw’omuntu alina okutegeera,

era yeeyoleka ne mu basirusiru.

3414:34 Nge 11:11Obutuukirivu buzimba eggwanga,

naye ekibi kiswaza abantu ab’engeri zonna.

3514:35 Mat 24:45-51; 25:14-30Kabaka asanyukira omuddu akola eby’amagezi,

naye obusungu bwa kabaka bunaabuubuukiranga ku oyo akola ebiswaza.