Miyambo 13 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 13:1-25

1Mwana wanzeru amamvera malangizo a abambo ake,

koma mwana wonyoza samamvetsera chidzudzulo.

2Munthu amapeza zinthu zabwino chifukwa cha mawu ake,

koma anthu osakhulupirika amalakalaka zachiwawa basi.

3Iye amene amagwira pakamwa pake amateteza moyo wake,

koma amene amayankhula zopanda pake adzawonongeka.

4Munthu waulesi amakhumbira zinthu koma sapeza kanthu,

koma munthu wakhama adzalemera.

5Munthu wolungama amadana ndi zabodza,

koma zochita za munthu woyipa zimanyansa ndiponso zimachititsa manyazi.

6Chilungamo chimateteza munthu wangwiro,

koma tchimo limagwetsa munthu wochimwa.

7Wina amadziyesa kuti ndi wolemera chonsecho alibe kanthu kalikonse;

munthu wina amaoneka ngati wosauka chonsecho ali ndi chuma chambiri.

8Chuma cha munthu wolemera chitha kuwombola moyo wake,

koma munthu wosauka amamva chidzudzulo.

9Nyale ya munthu wolungama ndi yokondweretsa,

koma nyale ya munthu woyipa imazimitsidwa.

10Chipongwe chosamalabadirako za anthu ena chimadzetsa mikangano,

koma womva malangizo a anzawo ndiwo ali ndi nzeru.

11Chuma chochipeza mofulumira chidzatha pangʼonopangʼono

koma chuma chosonkhanitsidwa pangʼonopangʼono chidzachulukirachulukira.

12Chinthu chochiyembekezera chikalephereka chimalefula mtima,

koma chinthu chochilakalaka chikachitikadi chimakhala ngati mtengo wamoyo.

13Amene amanyoza malangizo adzawonongeka,

koma amene amasamala lamulo amalandira mphotho.

14Malangizo a munthu wanzeru ali ngati kasupe wamoyo;

amathandiza munthu kuti asakondwe mu msampha wa imfa.

15Munthu wa nzeru zabwino amapeza kuyanja pakati pa anthu,

koma munthu wosakhulupirika adzawonongeka.

16Munthu wochenjera amachita zinthu mwanzeru,

koma chitsiru chimaonetsa poyera uchitsiru wake.

17Wamthenga woyipa amagwetsa anthu mʼmavuto,

koma nthumwi yodalirika imabweretsa mtendere.

18Wokana mwambo adzasauka ndi kunyozedwa,

koma wosamala chidzudzulo adzalemekezedwa.

19Chinthu chochilakalaka chikachitika chimasangalatsa mtima,

koma zitsiru zimadana ndi kuleka zoyipa.

20Woyenda ndi anthu anzeru nayenso adzakhala wanzeru;

koma woyenda ndi zitsiru adzapwetekeka.

21Choyipa chitsata mwini,

koma wochita zolungama adzalandira mphotho yabwino.

22Munthu wabwino amasiyira zidzukulu zake cholowa,

koma chuma cha munthu wochimwa amachilandira ndi olungama.

23Tsala la munthu wosauka limalola chakudya chambiri,

koma anthu opanda chilungamo amachilanda.

24Amene sakwapula mwana wake, ndiye kuti amamuda,

koma wokonda mwana wake sazengereza kumulanga.

25Munthu wolungama amakhala ndi zakudya zoti adye nʼkukhuta,

koma mʼmimba mwa munthu woyipa mumakhala pululu ndi njala.

Luganda Contemporary Bible

Engero 13:1-25

Ensibuko y’Obugagga Obungi

113:1 Nge 10:1Omwana omugezi assaayo omwoyo eri ebiragiro bya kitaawe,

naye omunyoomi tafaayo ku kunenyezebwa.

213:2 Nge 12:14Omuntu asanyuka olw’ebirungi ebiva mu bibala bya kamwa ke,

naye atali mwesigwa yeegomba kuleeta ntalo.

313:3 a Yak 3:2 b Nge 21:23 c Nge 18:7, 20-21Oyo eyeegendereza by’ayogera akuuma obulamu bwe,

naye oyo amala googera, alizikirira.

4Omuntu omugayaavu yeegomba kyokka n’atabaako ky’afuna,

naye omunyiikivu byayagala byonna abifuna.

5Omuntu omutuukirivu akyawa obulimba,

naye omukozi w’ebibi yeereetera kunyoomebwa.

613:6 Nge 11:3, 5Obutuukirivu bukuuma omuntu omwesimbu,

naye okukola ebibi kuzikiriza omwonoonyi.

713:7 2Ko 6:10Omuntu omu ayinza okwefuula omugagga ate nga taliiko ky’alina,

ate omulala ne yeefuula okuba omwavu so nga mugagga nnyo.

8Obugagga bw’omuntu buyinza okumununula,

naye omwavu talina ky’atya.

913:9 Yob 18:5; Nge 4:18-19; 24:20Ekitangaala ky’abatuukirivu kyaka nnyo,

naye ettaala y’abakozi b’ebibi ezikira.

10Amalala gazaala buzaazi nnyombo,

naye amagezi gasangibwa mu abo abakkiriza okulabulwa.

1113:11 Nge 10:2Ensimbi enkumpanye ziggwaawo,

naye ezijja empolampola zeeyongera obungi.

12Essuubi erirwawo okutuukirira lirwaza omutima,

naye ekyegombebwa bwe kituukirira kiba muti gwa bulamu.

1313:13 Kbl 15:31; 2By 36:16Omuntu anyooma ebiragiro aligwa mu mitawaana,

naye oyo awuliriza ebimulagirwa aliweebwa empeera.

1413:14 a Nge 10:11 b Nge 14:27Okuyigiriza kw’omuntu alina amagezi nsulo ya bulamu,

era kuggya omuntu mu mitego gy’okufa.

15Okutegeera okulungi kuleeta okuganja,

naye ekkubo ly’abateesigibwa liba zzibu.

1613:16 Nge 12:23Omuntu omwegendereza akola amaze kulowooza,

naye omusirusiru alaga obutamanya bwe.

1713:17 Nge 25:13Omubaka omubi yeesuula mu mitawaana,

naye omubaka omwesigwa aleeta kuwonyezebwa.

1813:18 Nge 15:5, 31-32Anyooma okukangavvulwa yeereetako obwavu n’obuswavu,

naye oyo assaayo omwoyo ku kunenyezebwa aweebwa ekitiibwa.

19Ekyegombebwa bwe kituukirira kisanyusa omutima,

naye okulekayo okukola ebibi kya muzizo eri abasirusiru.

2013:20 Nge 15:31Oyo atambula n’abantu abagezi ageziwala,

naye oyo atambula n’abasirusiru alaba ennaku.

2113:21 Zab 32:10Emitawaana gigoberera aboonoonyi,

naye okukulaakulana y’empeera y’abatuukirivu.

2213:22 Yob 27:17; Mub 2:26Omuntu omulungi alekera bazzukulu be ebyobusika,

naye obugagga bw’omwonoonyi buterekerwa omutuukirivu.

23Ennimiro z’abaavu ziyinza okuvaamu emmere nnyingi,

naye obutali bwenkanya ne bugyera yonna.

2413:24 Nge 19:18; 22:15; 23:13-14; 29:15, 17; Beb 12:7Atakozesa kaggo akyawa omwana we,

naye oyo amwagala afaayo okumukangavvula.

2513:25 Zab 34:10; Nge 10:3Omutuukirivu alya emmere ye n’akkuta,

naye abakozi b’ebibi basigala nga bayala.