Miyambo 12 – CCL & NAV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 12:1-28

1Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu,

koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.

2Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova,

koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.

3Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa,

koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.

4Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake,

koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.

5Maganizo a anthu olungama ndi owongoka,

koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.

6Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa,

koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.

7Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika,

koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.

8Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake,

koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.

9Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika,

kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.

10Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake,

koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.

11Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka,

koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.

12Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa,

koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.

13Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa;

koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.

14Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake

ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.

15Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino,

koma munthu wanzeru amamvera malangizo.

16Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo,

koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.

17Woyankhula zoona amapereka umboni woona,

koma mboni yabodza imafotokoza zonama.

18Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga,

koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.

19Mawu woona amakhala mpaka muyaya

koma mawu abodza sakhalitsa.

20Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo;

koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.

21Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama,

koma munthu woyipa mavuto samuthera.

22Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova,

koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.

23Munthu wochenjera amabisa nzeru zake,

koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.

24Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira,

koma aulesi adzakhala ngati kapolo.

25Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu,

koma mawu abwino amamusangalatsa.

26Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake,

koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.

27Munthu waulesi sapeza chimene akufuna,

koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.

28Mʼnjira yachilungamo muli moyo;

koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.

Ketab El Hayat

الأمثال 12:1-28

1مَنْ يُحِبُّ التَّأْدِيبَ يُحِبُّ الْمَعْرِفَةَ، وَمَنْ يَمْقُتُ التَّأْنِيبَ غَبِيٌّ. 2الصَّالِحُ يَحْظَى بِرِضَى الرَّبِّ، وَرَجُلُ الْمَكَائِدِ يَسْتَجْلِبُ قَضَاءَهُ. 3لَا يَثْبُتُ الإِنْسَانُ بِالشَّرِّ، أَمَّا أَصْلُ الصِّدِّيقِ فَلا يَتَزَعْزَعُ. 4الْمَرْأَةُ الْفَاضِلَةُ تَاجٌ لِزَوْجِهَا، أَمَّا جَالِبَةُ الْخِزْيِ فَكَنَخْرٍ فِي عِظَامِهِ. 5مَقَاصِدُ الصِّدِّيقِ شَرِيفَةٌ، وَتَدَابِيرُ الشِّرِّيرِ غَادِرَةٌ. 6كَلامُ الأَشْرَارِ يَتَرَبَّصُ لِسَفْكِ الدَّمِ، وَأَقْوَالُ الْمُسْتَقِيمِينَ تَسْعَى لِلإِنْقَاذِ. 7مَصِيرُ الأَشْرَارِ الانْهِيَارُ وَالتَّلاشِي، أَمَّا صَرْحُ الصِّدِّيقِينَ فَيَثْبُتُ رَاسِخاً. 8يُحْمَدُ الْمَرْءُ لِتَعَقُّلِهِ، وَيُزْدَرَى ذُو الْقَلْبِ الْمُلْتَوِي. 9الْحَقِيرُ الْكَادِحُ خَيْرٌ مِنَ الْمُتَعَاظِمِ الْمُفْتَقِرِ لِلُقْمَةِ الْخُبْزِ.

10الصِّدِّيقُ يُرَاعِي نَفْسَ بَهِيمَتِهِ، أَمَّا الشِّرِّيرُ فَأَرَقُّ مَرَاحِمِهِ تَتَّسِمُ بِالْقَسْوَةِ. 11مَنْ يُفْلِحْ أَرْضَهُ، تَكْثُرْ غَلَّةُ خُبْزِهِ، وَمَنْ يُلاحِقُ الأَوْهَامَ فَهُوَ أَحْمَقُ. 12يَشْتَهِي الشِّرِّيرُ مَنَاهِبَ الإِثْمِ، أَمَّا الصِّدِّيقُ فَيَزْدَهِرُ. 13يَقَعُ الشِّرِّيرُ فِي فَخِّ أَكَاذِيبِ لِسَانِهِ، أَمَّا الصِّدِّيقُ فَيُفْلِتُ مِنَ الضِّيقِ. 14مِنْ ثَمَرِ صِدْقِ أَقْوَالِهِ يَشْبَعُ الإِنْسَانُ خَيْراً، كَمَا تُرَدُّ لَهُ ثِمَارُ أَعْمَالِ يَدَيْهِ.

15يَبْدُو سَبِيلُ الأَحْمَقِ صَالِحاً فِي عَيْنَيْهِ، أَمَّا الْحَكِيمُ فَيَسْتَمِعُ إِلَى الْمَشُورَةِ. 16يُبْدِي الأَحْمَقُ غَيْظَهُ فِي لَحْظَةٍ، أَمَّا الْعَاقِلُ فَيَتَجَاهَلُ الإِهَانَةَ. 17مَنْ يَنْطِقْ بِالصِّدْقِ يَشْهَدْ بِالْحَقِّ، أَمَّا شَاهِدُ الزُّورِ فَيَتَكَلَّمُ بِالْكَذِبِ. 18رُبَّ مِهْذَارٍ تَنْفُذُ كَلِمَاتُهُ كَطَعْنَاتِ السَّيْفِ، وَفِي أَقْوَالِ فَمِ الْحُكَمَاءِ شِفَاءٌ. 19أَقْوَالُ الشِّفَاهِ الصَّادِقَةِ تَدُومُ إِلَى الأَبَدِ، أَمَّا أَكَاذِيبُ لِسَانِ الزُّورِ فَتَنْفَضِحُ فِي لَحْظَةٍ. 20يَكْمُنُ الْغِشُّ فِي قُلُوبِ مُدَبِّرِي الشَّرِّ، أَمَّا الْفَرَحُ فَيَمْلأُ صُدُورَ السَّاعِينَ إِلَى السَّلامِ. 21لَا يُصِيبُ الصِّدِّيقَ سُوءٌ، أَمَّا الأَشْرَارُ فَيَحِيقُ بِهِمُ الأَذَى. 22الشِّفَاهُ الْكَاذِبَةُ رِجْسٌ لَدَى الرَّبِّ، وَمَسَرَّتُهُ بِالْعَامِلِينَ بِالصِّدْقِ.

23الْعَاقِلُ يَحْتَفِظُ بِعِلْمِهِ، وَقُلُوبُ الْجُهَّالِ تَفْضَحُ مَا فِيهَا مِنْ سَفَاهَةٍ. 24ذُو الْيَدِ الْمُجْتَهِدَةِ يَسُودُ، وَالْكَسُولُ ذُو الْيَدِ الْمُرْتَخِيَةِ يَخْدُمُ تَحْتَ الْجِزْيَةِ. 25الْقَلْبُ الْقَلِقُ الْجَزِعُ يُوْهِنُ الإِنْسَانَ، وَالْكَلِمَةُ الطَّيِّبَةُ تُفَرِّحُهُ. 26الصِّدِّيقُ يَهْدِي صَاحِبَهُ، أَمَّا طَرِيقُ الأَشْرَارِ فَتُضِلُّهُ. 27الْمُتَقَاعِسُ لَا يَحْظَى بِصَيْدٍ، وَأَثْمَنُ مَا لَدَى الإِنْسَانِ هُوَ اجْتِهَادُهُ. 28سَبِيلُ الْبِرِّ يُفْضِي إِلَى الْحَيَاةِ، وَفِي طَرِيقِهِ خُلُودٌ.