Miyambo 11 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 11:1-31

1Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa,

koma amakondwera ndi muyeso woyenera.

2Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi,

koma pamene pali kudzichepetsa pameneponso pali nzeru.

3Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera,

koma anthu osakhulupirika amawonongeka ndi chinyengo chawo.

4Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu,

koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.

5Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo,

koma ntchito zoyipa zimagwetsa mwini wake yemweyo.

6Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa,

koma anthu onyenga adzagwidwa ndi zilakolako zawo zomwe.

7Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso.

Chiyembekezo cha munthu wosalungama chimawonongeka.

8Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto,

koma mʼmalo mwake amagwa mʼmavutomo ndi anthu oyipa.

9Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake,

koma munthu wolungama amapulumuka chifukwa cha kudziwa zinthu.

10Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera,

ndipo oyipa akamawonongeka anthu amafuwula mwachimwemwe.

11Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima,

koma umawonongedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oyipa.

12Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru,

koma munthu wanzeru zomvetsa zinthu amakhala chete.

13Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi;

koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.

14Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa;

koma pakakhala aphungu ambiri pamakhalanso chipulumutso.

15Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto,

koma wodana ndi za chikole amakhala pa mtendere.

16Mkazi wodekha amalandira ulemu,

koma amuna ankhanza amangopata chuma.

17Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino

koma munthu wankhanza amadzibweretsera mavuto.

18Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu,

koma wochita chilungamo amakolola mphotho yeniyeni.

19Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo,

koma wothamangira zoyipa adzafa.

20Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota

koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro.

21Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa,

koma anthu olungama adzapulumuka.

22Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba,

ndi momwenso amaonekera mkazi wokongola wamʼkamwa.

23Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha,

koma chiyembekezo cha anthu oyipa chimathera mu ukali wa Mulungu.

24Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe;

wina amamana chomwe akanatha kupereka, koma kumanka nasawukabe.

25Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera;

iye amene amathandiza ena iyenso adzathandizidwa.

26Anthu amatemberera womana anzake chakudya,

koma madalitso amakhala pamutu pa munthu amene amagulitsa chakudyacho.

27Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo,

koma wofunafuna zoyipa zidzamupeza.

28Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota,

koma wolungama adzaphukira ngati tsamba lobiriwira.

29Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto,

ndipo chitsiru chidzakhala kapolo wa munthu wa nzeru.

30Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo,

ndipo kusatsata malamulo kumawonongetsa moyo.

31Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi,

kuli bwanji anthu osapembedza ndi ochimwa!

Luganda Contemporary Bible

Engero 11:1-31

111:1 a Lv 19:36; Ma 25:13-16; Nge 20:10, 23 b Nge 16:11Minzaani eteri ya mazima ya muzizo eri Mukama,

naye ebipimo ebituufu bye bimusanyusa.

211:2 a Nge 16:18 b Nge 18:12; 29:23Amalala bwe gajja, ng’obuswavu butuuse,

naye obwetoowaze buleeta amagezi.

311:3 Nge 13:6Obwesimbu bw’abatuukirivu bubaluŋŋamya,

naye enkwe z’abatali beesigwa zibazikirizisa.

411:4 a Ez 7:19; Zef 1:18 b Lub 7:1; Nge 10:2Obugagga tebugasa ku lunaku olw’okusalirwako omusango,

naye obutuukirivu buwonya okufa.

511:5 Nge 5:21-23Obutuukirivu bw’abalongoofu bubatambuliza mu kkubo eggolokofu

naye abakozi b’ebibi bagwa olw’ebikolwa byabwe ebibi.

6Obutuukirivu bw’abagolokofu bubawonya,

naye abatali beesigwa bagwa mu mutego olw’okwegomba ebibi.

711:7 Nge 10:28Omukozi w’ebibi bw’afa, essuubi lye libula,

ne byonna bye yasuubira mu maanyi bikoma.

811:8 Nge 21:18Omutuukirivu aggyibwa mu mitawaana,

naye jjijjira omukozi w’ebibi.

9Akamwa k’oyo atatya Katonda, kazikiriza muliraanwa,

naye olw’okumanya, abatuukirivu bawona.

1011:10 Nge 28:12Abatuukirivu bwe bakulaakulana ekibuga kijaguza;

abakozi b’ebibi bwe bazikirira wawulirwawo amaloboozi ag’essanyu.

1111:11 Nge 29:8Omukisa gw’abatuukirivu gukulaakulanya ekibuga:

naye olw’akamwa k’abakozi b’ebibi, ekibuga kizikirizibwa.

Abeesigwa n’Abatambuza Eŋŋambo

1211:12 Nge 14:21Omuntu atalina magezi anyooma muliraanwa we,

naye omuntu ategeera akuuma olulimi lwe.

1311:13 Lv 19:16; Nge 20:19; 1Ti 5:13Aseetula olugambo atta obwesigwa,

naye omuntu omwesigwa akuuma ekyama.

1411:14 a Nge 20:18 b Nge 15:22; 24:6Awatali kuluŋŋamizibwa eggwanga lidobonkana,

naye abawi b’amagezi abangi baleeta obuwanguzi.

1511:15 Nge 6:1Eyeeyimirira omuntu gw’atamanyiko alibonaabona,

naye oyo akyawa okweyimirira aliba bulungi.

1611:16 Nge 31:31Omukazi ow’ekisa aweebwa ekitiibwa,

naye abasajja ab’amawaggali bakoma ku bugagga bwokka.

17Omusajja alina ekisa aganyulwa,

naye alina ettima yeereetako akabi.

1811:18 Kos 10:12-13Omukozi w’ebibi afuna empeera ey’obukuusa,

naye oyo asiga eby’obutuukirivu akungula empeera eya nnama ddala.

19Omuntu omutuukirivu ddala alifuna obulamu,

naye oyo akola ebitali bya butuukirivu alifa.

2011:20 1By 29:17; Zab 119:1; Nge 12:2, 22Mukama akyawa abantu abalina emitima emikyamu,

naye ab’amakubo amagolokofu be bamusanyusa.

2111:21 Nge 16:5Mutegeerere ddala ng’abakozi b’ebibi tebalirema kubonerezebwa,

naye bazzukulu b’abatuukirivu tebalibaako musango.

22Ng’empeta ya zaabu mu nnyindo y’embizzi,

bw’atyo bw’abeera omukazi omulungi atalaba njawulo wakati w’ekirungi n’ekibi.

23Abatuukirivu bye beegomba bivaamu birungi byereere,

naye abakozi b’ebibi bye bakola bisunguwaza.

Omuntu Omugabi

24Omuntu agaba obuteerekereza, yeeyongera bweyongezi kugaggawala;

naye akwatirira kye yandigabye, yeeyongera kwavuwala.

2511:25 Mat 5:7; 2Ko 9:6-9Omuntu agaba anagaggawalanga,

n’oyo ayamba talibulako amuyamba.

26Abantu bakolimira oyo akweka eŋŋaano mu kiseera eky’obwetaavu,

naye oyo agitunda mu kiseera ekyo afuna emikisa.

2711:27 Es 7:10; Zab 7:15-16Oyo anyiikira okukola obulungi afuna okuganja,

naye oyo anoonya ekibi, kimujjira.

2811:28 a Yob 31:24-28; Zab 49:6; 52:7; Mak 10:25; 1Ti 6:17 b Zab 1:3; 92:12-14; Yer 17:8Oyo eyeesiga obugagga bwe aligwa,

naye abatuukirivu banaakulaakulananga ne baba ng’amalagala amalamu.

2911:29 Nge 14:19Omuntu aleeta emitawaana mu maka g’ewaabwe, alisikira mpewo;

era n’omusirusiru aliba muddu w’oyo alina omutima ogw’amagezi.

3011:30 Yak 5:20Ekibala ky’omutuukirivu muti gwa bulamu,

era n’oyo asikiriza emyoyo gy’abantu ne balokoka wa magezi.

3111:31 Nge 13:21; Yer 25:29; 1Pe 4:18Obanga omutuukirivu alifuna ekimusaanidde ku nsi kuno,

oyo atatya Katonda n’omwonoonyi balirema obutafuna ekibasaanidde?