Miyambo 10 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 10:1-32

Miyambo ya Solomoni

1Miyambo ya Solomoni:

Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake,

koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.

2Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa,

koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.

3Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala;

koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.

4Wochita zinthu mwaulesi amasauka,

koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.

5Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru,

koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.

6Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama,

koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.

7Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso,

koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.

8Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo,

koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.

9Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka;

koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.

10Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto,

koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.

11Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo,

koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.

12Udani umawutsa mikangano,

koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.

13Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu,

koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.

14Anzeru amasunga chidziwitso

koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.

15Chuma cha munthu wolemera

ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.

16Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama,

koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.

17Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo,

koma wonyoza chidzudzulo amasochera.

18Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama,

ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.

19Mawu akachuluka zolakwa sizisowa,

koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.

20Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri,

koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.

21Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri;

koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.

22Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma,

ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.

23Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa,

koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.

24Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira;

chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.

25Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa,

koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.

26Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso,

ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.

27Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo;

koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.

28Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe,

koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.

29Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino,

koma wochita zoyipa adzawonongeka.

30Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake

koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.

31Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru,

koma lilime lokhota lidzadulidwa.

32Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula,

koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.

New Serbian Translation

Приче Соломонове 10:1-32

Приче Соломонове

1Мудре приче Соломона:

Мудар син радује свог оца,

а безуман син је жалост мајци својој.

2Бескорисно је непоштено богатство,

а праведност избавља од смрти.

3Не да Господ да је гладна душа праведника,

а жудњу зликовца одбацује.

4Сиромах је ко год ради рукама лењивим,

а богатство стичу руке марљивих.

5Мудар је син који лети сакупља,

а срамотно ради син што о жетви спава.

6Благослови су над главом праведника,

а уста зликоваца насиље скривају.

7Блажено је сећање на праведника,

а спомен на зликовца ће иструлити.

8Човек мудрог срца прихвата заповести,

а блебетави безумник ће сатрвен бити.

9Спокојно живи ко честито живи,

а ко накарадно живи биће разоткривен.

10Јад задаје ко оком намигује,

а блебетало ће сатрвено бити.

11Уста су праведникова врело живота,

а уста зликоваца насиље скривају.

12Мржња замеће свађу,

а љубав све грехе покрива.

13Мудрост ћеш наћи на уснама оштроумног,

а батина је за леђа безумнога.

14Мудри људи сабирају знање,

а брбљива уста близу су пропасти.

15Богатство је богатоме попут утврђења,

а сиромасима сиромаштво њихово попут рушевине.

16Праведнику је живот награда,

а казна за грехе накнада зликовцу.

17На стази живота је онај ко пази на опомену,

а тумара онај ко не мари за укор.

18Безумник је ко прикрива мржњу лажљивим уснама,

а шири клевету.

19Кад је речи много, грех је неизбежан;

разборито чини онај ко заузда уста.

20Сребро је пробрано праведников језик,

а срце зликовца мале је вредности.

21Многе хране уста праведника,

а безумни гину због безумља.

22Господњи благослов обогаћује

и тегобу са собом не носи.

23Злобнику је злоба ко забава,

а мудрост је за промишљеног.

24Зликовца стиже оно чега се боји,

а праведном се жеља испуњава.

25Као кад прохуји вихор ветар, тако ни зликовца нема,

а праведникови темељи су вечни.

26Као сирће зубима и дим очима,

такав је ленштина ономе ко га упосли.

27Богобојазност умножава дане,

а године зликоваца ће се скратити.

28Праведни се радују у нади,

а нада ће злобних да исхлапи.

29Пут Господњи је тврђава честитоме,

а пропаст за злотворе.

30Праведника неће довека пољуљати,

а злотвори неће населити земљу.

31Мудрошћу рађају уста праведника,

а језик ће развратника ишчупан да буде.

32Уживање није страно праведним уснама,

а ни разврат устима зликовца.