Miyambo 10 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 10:1-32

Miyambo ya Solomoni

1Miyambo ya Solomoni:

Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake,

koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.

2Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa,

koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.

3Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala;

koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.

4Wochita zinthu mwaulesi amasauka,

koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.

5Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru,

koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.

6Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama,

koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.

7Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso,

koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.

8Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo,

koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.

9Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka;

koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.

10Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto,

koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.

11Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo,

koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.

12Udani umawutsa mikangano,

koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.

13Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu,

koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.

14Anzeru amasunga chidziwitso

koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.

15Chuma cha munthu wolemera

ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.

16Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama,

koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.

17Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo,

koma wonyoza chidzudzulo amasochera.

18Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama,

ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.

19Mawu akachuluka zolakwa sizisowa,

koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.

20Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri,

koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.

21Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri;

koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.

22Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma,

ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.

23Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa,

koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.

24Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira;

chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.

25Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa,

koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.

26Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso,

ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.

27Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo;

koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.

28Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe,

koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.

29Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino,

koma wochita zoyipa adzawonongeka.

30Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake

koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.

31Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru,

koma lilime lokhota lidzadulidwa.

32Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula,

koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.

King James Version

Proverbs 10:1-32

1The proverbs of Solomon. A wise son maketh a glad father: but a foolish son is the heaviness of his mother.

2Treasures of wickedness profit nothing: but righteousness delivereth from death. 3The LORD will not suffer the soul of the righteous to famish: but he casteth away the substance of the wicked.10.3 the substance…: or, the wicked for their wickedness 4He becometh poor that dealeth with a slack hand: but the hand of the diligent maketh rich. 5He that gathereth in summer is a wise son: but he that sleepeth in harvest is a son that causeth shame. 6Blessings are upon the head of the just: but violence covereth the mouth of the wicked. 7The memory of the just is blessed: but the name of the wicked shall rot. 8The wise in heart will receive commandments: but a prating fool shall fall.10.8 a prating…: Heb. a fool of lips10.8 fall: Heb. be beaten 9He that walketh uprightly walketh surely: but he that perverteth his ways shall be known. 10He that winketh with the eye causeth sorrow: but a prating fool shall fall.10.10 fall: Heb. be beaten 11The mouth of a righteous man is a well of life: but violence covereth the mouth of the wicked. 12Hatred stirreth up strifes: but love covereth all sins. 13In the lips of him that hath understanding wisdom is found: but a rod is for the back of him that is void of understanding.10.13 of understanding: Heb. of heart 14Wise men lay up knowledge: but the mouth of the foolish is near destruction. 15The rich man’s wealth is his strong city: the destruction of the poor is their poverty. 16The labour of the righteous tendeth to life: the fruit of the wicked to sin. 17He is in the way of life that keepeth instruction: but he that refuseth reproof erreth.10.17 erreth: or, causeth to err 18He that hideth hatred with lying lips, and he that uttereth a slander, is a fool. 19In the multitude of words there wanteth not sin: but he that refraineth his lips is wise.

20The tongue of the just is as choice silver: the heart of the wicked is little worth. 21The lips of the righteous feed many: but fools die for want of wisdom.10.21 of wisdom: Heb. of heart 22The blessing of the LORD, it maketh rich, and he addeth no sorrow with it. 23It is as sport to a fool to do mischief: but a man of understanding hath wisdom.

24The fear of the wicked, it shall come upon him: but the desire of the righteous shall be granted. 25As the whirlwind passeth, so is the wicked no more: but the righteous is an everlasting foundation. 26As vinegar to the teeth, and as smoke to the eyes, so is the sluggard to them that send him.

27The fear of the LORD prolongeth days: but the years of the wicked shall be shortened.10.27 prolongeth: Heb. addeth 28The hope of the righteous shall be gladness: but the expectation of the wicked shall perish.

29The way of the LORD is strength to the upright: but destruction shall be to the workers of iniquity. 30The righteous shall never be removed: but the wicked shall not inhabit the earth.

31The mouth of the just bringeth forth wisdom: but the froward tongue shall be cut out. 32The lips of the righteous know what is acceptable: but the mouth of the wicked speaketh frowardness.10.32 frowardness: Heb. frowardnesses