Mika 7 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mika 7:1-20

Chipsinjo cha Israeli

1Tsoka ine!

Ndili ngati munthu wokunkha zipatso nthawi yachilimwe,

pa nthawi yokolola mphesa;

palibe phava lamphesa loti nʼkudya,

palibe nkhuyu zoyambirira zimene ndimazilakalaka kwambiri.

2Anthu opembedza atha mʼdziko;

palibe wolungama ndi mmodzi yemwe amene watsala.

Anthu onse akubisalirana kuti aphane;

aliyense akusaka mʼbale wake ndi khoka.

3Manja awo onse ndi aluso pochita zoyipa;

wolamulira amafuna mphatso,

woweruza amalandira ziphuphu,

anthu amphamvu amalamula kuti zichitike zimene akuzifuna,

onse amagwirizana zochita.

4Munthu wabwino kwambiri pakati pawo ali ngati mtengo waminga,

munthu wolungama kwambiri pakati pawo ndi woyipa kuposa mpanda waminga.

Tsiku limene alonda ako ananena lafika,

tsiku limene Mulungu akukuchezera.

Tsopano ndi nthawi ya chisokonezo chawo.

5Usadalire mnansi;

usakhulupirire bwenzi.

Usamale zoyankhula zako

ngakhale kwa mkazi amene wamukumbatira.

6Pakuti mwana wamwamuna akunyoza abambo ake,

mwana wamkazi akuwukira amayi ake,

mtengwa akukangana ndi apongozi ake,

adani a munthu ndi amene amakhala nawo mʼbanja mwake momwe.

7Koma ine ndikudikira Yehova mwachiyembekezo,

ndikudikira Mulungu Mpulumutsi wanga;

Mulungu wanga adzamvetsera.

Kuuka kwa Israeli

8Iwe mdani wanga, usandiseke!

Ngakhale ndagwa, ndidzauka.

Ngakhale ndikukhala mu mdima,

Yehova ndiye kuwunika kwanga.

9Ndidzapirira mkwiyo wa Yehova,

chifukwa ndinamuchimwira,

mpaka ataweruza mlandu wanga

ndi kukhazikitsa chilungamo changa.

Iye adzanditulutsa ndi kundilowetsa mʼkuwunika;

ndidzaona chilungamo chake.

10Ndipo mdani wanga adzaona zimenezi

nadzagwidwa ndi manyazi,

iye amene anandifunsa kuti,

“Ali kuti Yehova Mulungu wako?”

Ndidzaona kugonjetsedwa kwake ndi maso anga;

ngakhale tsopano adzaponderezedwa

ngati matope mʼmisewu.

11Idzafika nthawi yomanganso makoma anu,

nthawi yokulitsanso malire anu.

12Nthawi imeneyo anthu adzabwera kwa inu

kuchokera ku Asiriya ndi mizinda ya ku Igupto,

ngakhale kuchokera ku Igupto mpaka ku Yufurate

ndiponso kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja inanso

kuchokera ku phiri lina mpaka ku phiri linanso.

13Dziko lapansi lidzasanduka chipululu

chifukwa cha anthu okhala mʼdzikomo, potsatira zochita za anthuwo.

Pemphero ndi Matamando

14Wetani anthu anu ndi ndodo yanu yowateteza,

nkhosa zimene ndi cholowa chanu,

zimene zili zokha mʼnkhalango,

mʼdziko la chonde.

Muzilole kuti zidye mu Basani ndi mu Giliyadi

monga masiku akale.

15“Ndidzawaonetsa zodabwitsa zanga,

ngati masiku amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto.”

16Mitundu ya anthu idzaona zimenezi ndipo idzachita manyazi,

ngakhale ali ndi mphamvu zotani.

Adzagwira pakamwa pawo

ndipo makutu awo adzagontha.

17Adzabwira fumbi ngati njoka,

ngati zolengedwa zomwe zimakwawa pansi.

Adzabwera akunjenjemera kuchokera mʼmaenje awo;

mwamantha adzatembenukira kwa Yehova Mulungu wathu

ndipo adzachita nanu mantha.

18Kodi alipo Mulungu wofanana nanu,

amene amakhululukira tchimo ndi kuyiwala zolakwa

za anthu otsala amene ndi cholowa chake?

Inu simusunga mkwiyo mpaka muyaya

koma kwanu nʼkuonetsa chikondi chosasinthika.

19Inu mudzatichitiranso chifundo;

mudzapondereza pansi machimo athu

ndi kuponyera zolakwa zathu zonse pansi pa nyanja.

20Mudzakhala wokhulupirika kwa Yakobo,

ndi kuonetsa chifundo chanu kwa Abrahamu,

monga munalonjeza molumbira kwa makolo athu

masiku amakedzana.

New International Version – UK

Micah 7:1-20

Israel’s misery

1What misery is mine!

I am like one who gathers summer fruit

at the gleaning of the vineyard;

there is no cluster of grapes to eat,

none of the early figs that I crave.

2The faithful have been swept from the land;

not one upright person remains.

Everyone lies in wait to shed blood;

they hunt each other with nets.

3Both hands are skilled in doing evil;

the ruler demands gifts,

the judge accepts bribes,

the powerful dictate what they desire –

they all conspire together.

4The best of them is like a brier,

the most upright worse than a thorn hedge.

The day God visits you has come,

the day your watchmen sound the alarm.

Now is the time of your confusion.

5Do not trust a neighbour;

put no confidence in a friend.

Even with the woman who lies in your embrace

guard the words of your lips.

6For a son dishonours his father,

a daughter rises up against her mother,

a daughter-in-law against her mother-in-law –

a man’s enemies are the members of his own household.

7But as for me, I watch in hope for the Lord,

I wait for God my Saviour;

my God will hear me.

Israel will rise

8Do not gloat over me, my enemy!

Though I have fallen, I will rise.

Though I sit in darkness,

the Lord will be my light.

9Because I have sinned against him,

I will bear the Lord’s wrath,

until he pleads my case

and upholds my cause.

He will bring me out into the light;

I will see his righteousness.

10Then my enemy will see it

and will be covered with shame,

she who said to me,

‘Where is the Lord your God?’

My eyes will see her downfall;

even now she will be trampled underfoot

like mire in the streets.

11The day for building your walls will come,

the day for extending your boundaries.

12In that day people will come to you

from Assyria and the cities of Egypt,

even from Egypt to the Euphrates

and from sea to sea

and from mountain to mountain.

13The earth will become desolate because of its inhabitants,

as the result of their deeds.

Prayer and praise

14Shepherd your people with your staff,

the flock of your inheritance,

which lives by itself in a forest,

in fertile pasture-lands.7:14 Or in the middle of Carmel

Let them feed in Bashan and Gilead

as in days long ago.

15‘As in the days when you came out of Egypt,

I will show them my wonders.’

16Nations will see and be ashamed,

deprived of all their power.

They will put their hands over their mouths

and their ears will become deaf.

17They will lick dust like a snake,

like creatures that crawl on the ground.

They will come trembling out of their dens;

they will turn in fear to the Lord our God

and will be afraid of you.

18Who is a God like you,

who pardons sin and forgives the transgression

of the remnant of his inheritance?

You do not stay angry for ever

but delight to show mercy.

19You will again have compassion on us;

you will tread our sins underfoot

and hurl all our iniquities into the depths of the sea.

20You will be faithful to Jacob,

and show love to Abraham,

as you pledged on oath to our ancestors

in days long ago.