Mika 7 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mika 7:1-20

Chipsinjo cha Israeli

1Tsoka ine!

Ndili ngati munthu wokunkha zipatso nthawi yachilimwe,

pa nthawi yokolola mphesa;

palibe phava lamphesa loti nʼkudya,

palibe nkhuyu zoyambirira zimene ndimazilakalaka kwambiri.

2Anthu opembedza atha mʼdziko;

palibe wolungama ndi mmodzi yemwe amene watsala.

Anthu onse akubisalirana kuti aphane;

aliyense akusaka mʼbale wake ndi khoka.

3Manja awo onse ndi aluso pochita zoyipa;

wolamulira amafuna mphatso,

woweruza amalandira ziphuphu,

anthu amphamvu amalamula kuti zichitike zimene akuzifuna,

onse amagwirizana zochita.

4Munthu wabwino kwambiri pakati pawo ali ngati mtengo waminga,

munthu wolungama kwambiri pakati pawo ndi woyipa kuposa mpanda waminga.

Tsiku limene alonda ako ananena lafika,

tsiku limene Mulungu akukuchezera.

Tsopano ndi nthawi ya chisokonezo chawo.

5Usadalire mnansi;

usakhulupirire bwenzi.

Usamale zoyankhula zako

ngakhale kwa mkazi amene wamukumbatira.

6Pakuti mwana wamwamuna akunyoza abambo ake,

mwana wamkazi akuwukira amayi ake,

mtengwa akukangana ndi apongozi ake,

adani a munthu ndi amene amakhala nawo mʼbanja mwake momwe.

7Koma ine ndikudikira Yehova mwachiyembekezo,

ndikudikira Mulungu Mpulumutsi wanga;

Mulungu wanga adzamvetsera.

Kuuka kwa Israeli

8Iwe mdani wanga, usandiseke!

Ngakhale ndagwa, ndidzauka.

Ngakhale ndikukhala mu mdima,

Yehova ndiye kuwunika kwanga.

9Ndidzapirira mkwiyo wa Yehova,

chifukwa ndinamuchimwira,

mpaka ataweruza mlandu wanga

ndi kukhazikitsa chilungamo changa.

Iye adzanditulutsa ndi kundilowetsa mʼkuwunika;

ndidzaona chilungamo chake.

10Ndipo mdani wanga adzaona zimenezi

nadzagwidwa ndi manyazi,

iye amene anandifunsa kuti,

“Ali kuti Yehova Mulungu wako?”

Ndidzaona kugonjetsedwa kwake ndi maso anga;

ngakhale tsopano adzaponderezedwa

ngati matope mʼmisewu.

11Idzafika nthawi yomanganso makoma anu,

nthawi yokulitsanso malire anu.

12Nthawi imeneyo anthu adzabwera kwa inu

kuchokera ku Asiriya ndi mizinda ya ku Igupto,

ngakhale kuchokera ku Igupto mpaka ku Yufurate

ndiponso kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja inanso

kuchokera ku phiri lina mpaka ku phiri linanso.

13Dziko lapansi lidzasanduka chipululu

chifukwa cha anthu okhala mʼdzikomo, potsatira zochita za anthuwo.

Pemphero ndi Matamando

14Wetani anthu anu ndi ndodo yanu yowateteza,

nkhosa zimene ndi cholowa chanu,

zimene zili zokha mʼnkhalango,

mʼdziko la chonde.

Muzilole kuti zidye mu Basani ndi mu Giliyadi

monga masiku akale.

15“Ndidzawaonetsa zodabwitsa zanga,

ngati masiku amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto.”

16Mitundu ya anthu idzaona zimenezi ndipo idzachita manyazi,

ngakhale ali ndi mphamvu zotani.

Adzagwira pakamwa pawo

ndipo makutu awo adzagontha.

17Adzabwira fumbi ngati njoka,

ngati zolengedwa zomwe zimakwawa pansi.

Adzabwera akunjenjemera kuchokera mʼmaenje awo;

mwamantha adzatembenukira kwa Yehova Mulungu wathu

ndipo adzachita nanu mantha.

18Kodi alipo Mulungu wofanana nanu,

amene amakhululukira tchimo ndi kuyiwala zolakwa

za anthu otsala amene ndi cholowa chake?

Inu simusunga mkwiyo mpaka muyaya

koma kwanu nʼkuonetsa chikondi chosasinthika.

19Inu mudzatichitiranso chifundo;

mudzapondereza pansi machimo athu

ndi kuponyera zolakwa zathu zonse pansi pa nyanja.

20Mudzakhala wokhulupirika kwa Yakobo,

ndi kuonetsa chifundo chanu kwa Abrahamu,

monga munalonjeza molumbira kwa makolo athu

masiku amakedzana.

New International Reader’s Version

Micah 7:1-20

Israel’s Sin Brings Suffering

1I’m suffering very much!

I’m like someone who gathers summer fruit in a vineyard

after the good fruit has already been picked.

No grapes are left to eat.

None of the early figs I long for remain.

2Faithful people have disappeared from the land.

Those who are honest are gone.

Everyone hides and waits

to spill the blood of others.

They use nets to try and trap one another.

3They are very good at doing what is evil.

Rulers require gifts.

Judges accept money from people

who want special favors.

Those who are powerful

always get what they want.

All of them make evil plans together.

4The best of these people are as harmful as thorns.

The most honest of them are even worse.

God has come to punish you.

The time your prophets warned you about has come.

Panic has taken hold of you.

5Don’t trust your neighbors.

Don’t put your faith in your friends.

Be careful what you say

even to your own wife.

6Sons don’t honor their fathers.

Daughters refuse to obey their mothers.

Daughters-in-law are against their mothers-in-law.

A man’s enemies are the members of his own family.

7But I will look to the Lord.

I’ll put my trust in God my Savior.

He will hear me.

Jerusalem Will Be Rebuilt

8The people of Jerusalem say,

“Don’t laugh when we suffer,

you enemies of ours!

We have fallen.

But we’ll get up.

Even though we sit in the dark,

the Lord will give us light.

9We’ve sinned against the Lord.

So he is angry with us.

His anger will continue until he takes up our case.

Then he’ll do what is right for us.

He’ll bring us out into the light.

Then we’ll see him save us.

10Our enemies will see it too.

And they will be put to shame.

After all, they said to us,

‘Where is the Lord your God?’

But we will see them destroyed.

Soon they will be stomped on

like mud in the streets.”

11People of Jerusalem, the time will come

when your walls will be rebuilt.

Land will be added to your territory.

12At that time your people will come back to you.

They’ll return from Assyria

and the cities of Egypt.

They’ll come from the countries

between Egypt and the Euphrates River.

They’ll return from the lands

between the seas.

They’ll come back from the countries

between the mountains.

13But the rest of the earth will be deserted.

The people who live in it

have done many evil things.

Prayer and Praise

14Lord, be like a shepherd to your people.

Take good care of them.

They are your flock.

They live by themselves

in the safety of a forest.

Rich grasslands are all around them.

Let them eat grass in Bashan and Gilead

just as they did long ago.

15The Lord says to his people,

“I showed you my wonders

when you came out of Egypt long ago.

In the same way, I will show them to you again.”

16When the nations see those wonders,

they will be put to shame.

All their power will be taken away from them.

They will be so amazed

that they won’t be able to speak or hear.

17They’ll be forced to eat dust like a snake.

They’ll be like creatures

that have to crawl on the ground.

They’ll come out of their dens

trembling with fear.

They’ll show respect for the Lord our God.

They will also have respect for his people.

18Lord, who is a God like you?

You forgive sin.

You forgive your people

when they do what is wrong.

You don’t stay angry forever.

Instead, you take delight in showing

your faithful love to them.

19Once again you will show loving concern for us.

You will completely wipe out

the evil things we’ve done.

You will throw all our sins

into the bottom of the sea.

20You will be faithful to Jacob’s people.

You will show your love

to Abraham’s children.

You will do what you promised to do for our people.

You made that promise long ago.