Mika 7 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mika 7:1-20

Chipsinjo cha Israeli

1Tsoka ine!

Ndili ngati munthu wokunkha zipatso nthawi yachilimwe,

pa nthawi yokolola mphesa;

palibe phava lamphesa loti nʼkudya,

palibe nkhuyu zoyambirira zimene ndimazilakalaka kwambiri.

2Anthu opembedza atha mʼdziko;

palibe wolungama ndi mmodzi yemwe amene watsala.

Anthu onse akubisalirana kuti aphane;

aliyense akusaka mʼbale wake ndi khoka.

3Manja awo onse ndi aluso pochita zoyipa;

wolamulira amafuna mphatso,

woweruza amalandira ziphuphu,

anthu amphamvu amalamula kuti zichitike zimene akuzifuna,

onse amagwirizana zochita.

4Munthu wabwino kwambiri pakati pawo ali ngati mtengo waminga,

munthu wolungama kwambiri pakati pawo ndi woyipa kuposa mpanda waminga.

Tsiku limene alonda ako ananena lafika,

tsiku limene Mulungu akukuchezera.

Tsopano ndi nthawi ya chisokonezo chawo.

5Usadalire mnansi;

usakhulupirire bwenzi.

Usamale zoyankhula zako

ngakhale kwa mkazi amene wamukumbatira.

6Pakuti mwana wamwamuna akunyoza abambo ake,

mwana wamkazi akuwukira amayi ake,

mtengwa akukangana ndi apongozi ake,

adani a munthu ndi amene amakhala nawo mʼbanja mwake momwe.

7Koma ine ndikudikira Yehova mwachiyembekezo,

ndikudikira Mulungu Mpulumutsi wanga;

Mulungu wanga adzamvetsera.

Kuuka kwa Israeli

8Iwe mdani wanga, usandiseke!

Ngakhale ndagwa, ndidzauka.

Ngakhale ndikukhala mu mdima,

Yehova ndiye kuwunika kwanga.

9Ndidzapirira mkwiyo wa Yehova,

chifukwa ndinamuchimwira,

mpaka ataweruza mlandu wanga

ndi kukhazikitsa chilungamo changa.

Iye adzanditulutsa ndi kundilowetsa mʼkuwunika;

ndidzaona chilungamo chake.

10Ndipo mdani wanga adzaona zimenezi

nadzagwidwa ndi manyazi,

iye amene anandifunsa kuti,

“Ali kuti Yehova Mulungu wako?”

Ndidzaona kugonjetsedwa kwake ndi maso anga;

ngakhale tsopano adzaponderezedwa

ngati matope mʼmisewu.

11Idzafika nthawi yomanganso makoma anu,

nthawi yokulitsanso malire anu.

12Nthawi imeneyo anthu adzabwera kwa inu

kuchokera ku Asiriya ndi mizinda ya ku Igupto,

ngakhale kuchokera ku Igupto mpaka ku Yufurate

ndiponso kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja inanso

kuchokera ku phiri lina mpaka ku phiri linanso.

13Dziko lapansi lidzasanduka chipululu

chifukwa cha anthu okhala mʼdzikomo, potsatira zochita za anthuwo.

Pemphero ndi Matamando

14Wetani anthu anu ndi ndodo yanu yowateteza,

nkhosa zimene ndi cholowa chanu,

zimene zili zokha mʼnkhalango,

mʼdziko la chonde.

Muzilole kuti zidye mu Basani ndi mu Giliyadi

monga masiku akale.

15“Ndidzawaonetsa zodabwitsa zanga,

ngati masiku amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto.”

16Mitundu ya anthu idzaona zimenezi ndipo idzachita manyazi,

ngakhale ali ndi mphamvu zotani.

Adzagwira pakamwa pawo

ndipo makutu awo adzagontha.

17Adzabwira fumbi ngati njoka,

ngati zolengedwa zomwe zimakwawa pansi.

Adzabwera akunjenjemera kuchokera mʼmaenje awo;

mwamantha adzatembenukira kwa Yehova Mulungu wathu

ndipo adzachita nanu mantha.

18Kodi alipo Mulungu wofanana nanu,

amene amakhululukira tchimo ndi kuyiwala zolakwa

za anthu otsala amene ndi cholowa chake?

Inu simusunga mkwiyo mpaka muyaya

koma kwanu nʼkuonetsa chikondi chosasinthika.

19Inu mudzatichitiranso chifundo;

mudzapondereza pansi machimo athu

ndi kuponyera zolakwa zathu zonse pansi pa nyanja.

20Mudzakhala wokhulupirika kwa Yakobo,

ndi kuonetsa chifundo chanu kwa Abrahamu,

monga munalonjeza molumbira kwa makolo athu

masiku amakedzana.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

彌迦書 7:1-20

以色列的敗壞

1我真悲慘!

就像夏天的果子已被收盡,

葡萄已被摘淨,

找不到一串可吃的,

尋不見我心中渴望的初熟無花果。

2虔敬人已從大地上滅絕,

世間再沒有正直人。

人人伺機殺人流血,

用網羅獵取自己的弟兄。

3他們善於作惡。

領袖和審判官索要賄賂,

顯貴袒露心中的惡慾,朋比為奸。

4他們當中最好的不過是蒺藜,

最正直的也不過是荊棘籬笆。

你們的守望者所說的日子,

就是你們受懲罰的日子已經來到。

你們必驚慌失措。

5不要相信鄰居,

不要信賴朋友,

即使對你懷中的妻子也要守口如瓶。

6因為兒子藐視父親,

女兒與母親作對,

媳婦與婆婆作對;

家人之間反目成仇。

7至於我,

我要仰望耶和華,

等候拯救我的上帝;

我的上帝必垂聽我的祈求。

8我的仇敵啊,

你們不要對我幸災樂禍!

我雖跌倒,但必再爬起來;

我雖坐在黑暗裡,

但耶和華必做我的光。

9我得罪了耶和華,

所以要忍受祂的懲罰,

直到祂為我辯護,替我伸冤。

祂必領我進入光明,

我必親睹祂的公義。

10從前嘲笑我說「你的上帝耶和華在哪裡」的仇敵看見這事,

都必滿面羞愧。

我必親眼看見他們遭到報應,

他們要像街上的泥土一樣被人踐踏。

11以色列啊,

終有一日你會重建自己的城牆。

到那日,你必擴張自己的疆域。

12那日,從亞述埃及的各城,

埃及幼發拉底河,

從天涯到海角7·12 從天涯到海角」希伯來文是「從海到海,從山到山」。

人們都要到你這裡來。

13然而,大地要因地上居民的罪惡而荒涼。

14耶和華啊,

求你用你的杖牧放屬於你的羊群,

就是你的子民。

他們獨自居住在叢林中,

住在肥沃的田園間。

願他們像從前一樣在巴珊基列吃草。

15耶和華說:

「我要向他們顯出神蹟奇事,

就像他們離開埃及時一樣。」

16列國看見這一切,

都必因自己勢力衰微而羞愧,

都必用手捂口,耳朵變聾。

17他們要像蛇一樣舔土,

又如地上的爬蟲,

戰戰兢兢地走出營寨;

他們必畏懼我們的上帝耶和華,

他們必對你充滿恐懼。

18有何神明像你一樣赦免罪惡,

饒恕你倖存子民的過犯?

你不會永遠發怒,

因為你樂於施恩。

19你必再憐憫我們,

將我們的罪惡踐踏在腳下,

把我們的一切過犯拋進深海。

20你必按古時給我們列祖的誓言,

以信實待雅各

以慈愛待亞伯拉罕