Mika 6 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mika 6:1-16

Mlandu wa Yehova ndi Israeli

1Tamverani zimene Yehova akunena:

“Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri;

zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.

2Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri;

tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi.

Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake;

Iye akutsutsa Aisraeli.

3“Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani?

Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.

4Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto

ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo.

Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni,

pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.

5Anthu anga, kumbukirani

zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani

ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha.

Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala,

kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”

6Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova

ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba?

Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza,

ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?

7Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000,

kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta?

Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga?

Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?

8Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino.

Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe?

Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo

ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.

Kulakwa kwa Israeli ndi Chilango chake

9Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda

ndi nzeru kuopa dzina lanu.

“Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.

10Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala

chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo,

ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?

11Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo,

ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?

12Anthu ake olemera amachita zachiwawa;

anthu ake ndi abodza

ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.

13Choncho, ndayamba kukuwonongani,

kukusakazani chifukwa cha machimo anu.

14Mudzadya, koma simudzakhuta;

mudzakhalabe ndi njala.

Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika,

chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.

15Mudzadzala, koma simudzakolola.

Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito.

Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.

16Inu mwatsatira malangizo a Omuri

ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu,

ndi khalidwe lawo lonse.

Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe

ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu;

mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”

Nueva Versión Internacional

Miqueas 6:1-16

Querella de Dios contra su pueblo

1Escuchen lo que dice el Señor:

«Levántate, presenta tu pleito ante las montañas;

deja que las colinas oigan tu voz».

2Montañas, escuchen el pleito del Señor;

presten atención, firmes cimientos de la tierra.

Porque el Señor tiene un pleito contra su pueblo,

presenta una acusación contra Israel:

3«Pueblo mío, ¿qué te he hecho?

¿En qué te he ofendido? ¡Respóndeme!

4Yo fui quien te sacó de Egipto,

quien te libró de esa tierra de esclavitud.

Yo envié a Moisés, Aarón y Miriam

para que te dirigieran.

5Recuerda, pueblo mío,

lo que pidió Balac, rey de Moab,

y lo que le respondió Balán, hijo de Beor.

Recuerda tu paso desde Sitín hasta Guilgal,

y reconoce que el Señor actuó con justicia».

6¿Con qué me presentaré ante el Señor

y me postraré ante el Dios Altísimo?

¿Podré presentarme con holocaustos

o con becerros de un año?

7¿Se complacerá el Señor con miles de carneros

o con diez mil arroyos de aceite?

¿Ofreceré a mi primogénito por mi delito,

al fruto de mis entrañas por mi pecado?

8¡Él te ha mostrado, oh mortal, lo que es bueno!

¿Y qué es lo que espera de ti el Señor?:

Practicar la justicia,

amar la misericordia

y caminar humildemente ante tu Dios.

Castigo por delitos económicos y sociales

9La voz del Señor clama a la ciudad

y es de sabios temer a su nombre:

«¡Escuchen, pueblo de Judá y asamblea de la ciudad!6:9 Versículo de difícil traducción.

10¡Malvados!

¿Debo tolerar sus tesoros mal habidos

y sus odiosas medidas adulteradas?

11¿Debo tener por justas la balanza falsa

y la bolsa de pesas alteradas?

12Los ricos de la ciudad son gente violenta;

sus habitantes son gente mentirosa;

y sus lenguas hablan con engaño.

13Por lo que a mí toca, te demoleré a golpes,

te destruiré por tus pecados.

14Comerás, pero no te saciarás,

sino que seguirás padeciendo hambre.6:14 seguirás padeciendo hambre. Texto de difícil traducción.

Almacenarás, pero no salvarás nada,

porque lo que salves lo daré a la espada.

15Sembrarás, pero no cosecharás;

prensarás las aceitunas, pero no usarás el aceite;

pisarás las uvas, pero no beberás el vino.

16Tú sigues fielmente los decretos de Omrí

y todas las prácticas de la dinastía de Acab;

te conduces según sus consejos.

Por eso voy a entregarte a la destrucción

y a poner en ridículo a tus habitantes.

¡Tendrás que soportar el insulto de los pueblos!».6:16 los pueblos (LXX); mi pueblo (TM).