Mika 6 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mika 6:1-16

Mlandu wa Yehova ndi Israeli

1Tamverani zimene Yehova akunena:

“Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri;

zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.

2Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri;

tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi.

Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake;

Iye akutsutsa Aisraeli.

3“Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani?

Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.

4Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto

ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo.

Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni,

pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.

5Anthu anga, kumbukirani

zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani

ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha.

Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala,

kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”

6Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova

ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba?

Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza,

ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?

7Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000,

kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta?

Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga?

Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?

8Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino.

Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe?

Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo

ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.

Kulakwa kwa Israeli ndi Chilango chake

9Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda

ndi nzeru kuopa dzina lanu.

“Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.

10Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala

chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo,

ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?

11Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo,

ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?

12Anthu ake olemera amachita zachiwawa;

anthu ake ndi abodza

ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.

13Choncho, ndayamba kukuwonongani,

kukusakazani chifukwa cha machimo anu.

14Mudzadya, koma simudzakhuta;

mudzakhalabe ndi njala.

Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika,

chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.

15Mudzadzala, koma simudzakolola.

Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito.

Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.

16Inu mwatsatira malangizo a Omuri

ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu,

ndi khalidwe lawo lonse.

Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe

ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu;

mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”

King James Version

Micah 6:1-16

1Hear ye now what the LORD saith; Arise, contend thou before the mountains, and let the hills hear thy voice.6.1 before: or, with 2Hear ye, O mountains, the LORD’s controversy, and ye strong foundations of the earth: for the LORD hath a controversy with his people, and he will plead with Israel. 3O my people, what have I done unto thee? and wherein have I wearied thee? testify against me. 4For I brought thee up out of the land of Egypt, and redeemed thee out of the house of servants; and I sent before thee Moses, Aaron, and Miriam. 5O my people, remember now what Balak king of Moab consulted, and what Balaam the son of Beor answered him from Shittim unto Gilgal; that ye may know the righteousness of the LORD.

6¶ Wherewith shall I come before the LORD, and bow myself before the high God? shall I come before him with burnt offerings, with calves of a year old?6.6 of a…: Heb. sons of a year? 7Will the LORD be pleased with thousands of rams, or with ten thousands of rivers of oil? shall I give my firstborn for my transgression, the fruit of my body for the sin of my soul?6.7 body: Heb. belly 8He hath shewed thee, O man, what is good; and what doth the LORD require of thee, but to do justly, and to love mercy, and to walk humbly with thy God?6.8 walk…: Heb. humble thyself to walk

9The LORD’s voice crieth unto the city, and the man of wisdom shall see thy name: hear ye the rod, and who hath appointed it.6.9 the man…: or, thy name shall see that which is

10¶ Are there yet the treasures of wickedness in the house of the wicked, and the scant measure that is abominable?6.10 Are…: or, Is there yet unto every man an house of the, etc6.10 scant…: Heb. measure of leanness 11Shall I count them pure with the wicked balances, and with the bag of deceitful weights?6.11 count…: or, be pure with, etc 12For the rich men thereof are full of violence, and the inhabitants thereof have spoken lies, and their tongue is deceitful in their mouth. 13Therefore also will I make thee sick in smiting thee, in making thee desolate because of thy sins. 14Thou shalt eat, but not be satisfied; and thy casting down shall be in the midst of thee; and thou shalt take hold, but shalt not deliver; and that which thou deliverest will I give up to the sword. 15Thou shalt sow, but thou shalt not reap; thou shalt tread the olives, but thou shalt not anoint thee with oil; and sweet wine, but shalt not drink wine.

16¶ For the statutes of Omri are kept, and all the works of the house of Ahab, and ye walk in their counsels; that I should make thee a desolation, and the inhabitants thereof an hissing: therefore ye shall bear the reproach of my people.6.16 For the…: or, For he doth much keep the, etc6.16 desolation: or, astonishment