Mika 6 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mika 6:1-16

Mlandu wa Yehova ndi Israeli

1Tamverani zimene Yehova akunena:

“Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri;

zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.

2Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri;

tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi.

Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake;

Iye akutsutsa Aisraeli.

3“Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani?

Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.

4Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto

ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo.

Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni,

pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.

5Anthu anga, kumbukirani

zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani

ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha.

Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala,

kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”

6Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova

ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba?

Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza,

ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?

7Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000,

kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta?

Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga?

Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?

8Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino.

Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe?

Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo

ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.

Kulakwa kwa Israeli ndi Chilango chake

9Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda

ndi nzeru kuopa dzina lanu.

“Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.

10Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala

chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo,

ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?

11Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo,

ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?

12Anthu ake olemera amachita zachiwawa;

anthu ake ndi abodza

ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.

13Choncho, ndayamba kukuwonongani,

kukusakazani chifukwa cha machimo anu.

14Mudzadya, koma simudzakhuta;

mudzakhalabe ndi njala.

Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika,

chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.

15Mudzadzala, koma simudzakolola.

Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito.

Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.

16Inu mwatsatira malangizo a Omuri

ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu,

ndi khalidwe lawo lonse.

Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe

ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu;

mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”

Священное Писание

Михей 6:1-16

Всевышний обвиняет Исраил

1Послушайте, что говорит Вечный:

– Поднимись, изложи своё дело перед горами;

пусть слышат холмы то, что ты говоришь.

2Слушайте, горы, тяжбу Вечного,

и вы, прочные основания земли!

У Вечного тяжба с Его народом,

Он будет состязаться с Исраилом.

3Народ Мой, что Я сделал тебе?

Чем измучил тебя? Ответь Мне.

4Я вывел тебя из Египта,

выкупил из края неволи.

Я послал Мусу, Харуна и Марьям,

чтобы вести тебя.

5Вспомни, народ Мой,

что задумал Валак, царь Моава,

и что ответил ему Валаам, сын Беора6:5 Валак и Валаам – см. Чис. 22–24.,

и что случилось по пути из Шиттима в Гилгал6:5 См. Иеш. 3–4.;

вспомни, чтобы постичь праведные дела Вечного.

6С чем мне предстать перед Вечным,

с чем мне склониться перед Богом небесным?

Предстать ли со всесожжениями,

с телятами годовалыми?

7Можно ли Вечному угодить тысячами баранов,

нескончаемыми реками масла?

Отдам ли первенца в жертву за грех мой,

плод тела – за грех моей души?

8О человек, Вечный сказал тебе, что есть добро

и чего Он требует от тебя:

действовать справедливо, любить милосердие

и смиренно жить перед твоим Богом.

Вина и наказание Исраила

9Голос Вечного взывает к городу

(и мудрость – бояться Его имени):

– Внимайте жезлу и Тому,

Кто его поставил.

10Забуду ли, о дом злодеев, злодейством нажитое богатство

и меру уменьшенную, которая Мне ненавистна?

11Потерплю ли неправильные весы

и обманные гири?

12Богачи твои кровожадны,

твои обитатели лгут,

обман у них на устах.

13За это Я начал губить тебя,

разорять дотла за твои грехи.

14Будешь есть, но не наешься;

желудок твой останется пустым.

Будешь копить, но не сбережёшь,

а то, что сбережёшь, Я предам мечу.

15Будешь сеять, а жать не будешь;

будешь давить оливки, но не будешь умащаться маслом;

будешь топтать виноград, но вина пить не будешь.

16Ты соблюдал злые уставы царя Омри

и сохранил все нечестивые обычаи дома царя Ахава6:16 Омри и Ахав – см. 3 Цар. 16:21-34. Об этих царях говорится, что они делали больше зла, чем все их предшественники.;

всем их традициям следовал.

За это предам тебя разорению,

а твоих обитателей – позору;

ты будешь сносить глумление народов6:16 Или: «поругание Моего народа»..