Mika 5 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mika 5:1-15

Wolamulira Wochokera ku Betelehemu

1Iwe mzinda wa anthu ankhondo, sonkhanitsa anthu ako ankhondo,

pakuti anthu atizungulira kuti alimbane nafe.

Adzakantha ndi ndodo pa chibwano

cha wolamulira wa Israeli.

2“Koma iwe Betelehemu Efurata,

ngakhale uli wonyozeka pakati pa mafuko a Yuda,

mwa iwe mudzatuluka

munthu amene adzalamulira Israeli,

amene chiyambi chake nʼchakalekale,

nʼchamasiku amakedzana.”

3Nʼchifukwa chake Israeli adzasiyidwa

mpaka pa nthawi imene mayi amene ali woyembekezera adzachire.

Ndipo abale ake onse otsalira adzabwerera

kudzakhala pamodzi ndi Aisraeli.

4Iye adzalimbika, ndipo adzaweta nkhosa zake

mwa mphamvu ya Yehova,

mu ulemerero wa dzina la Yehova Mulungu wake.

Ndipo iwo adzakhala mu mtendere,

pakuti ukulu wake udzakhala ponseponse pa dziko lapansi.

5Ndipo Iye adzakhala mtendere wawo.

Chipulumutso ndi Chiwonongeko

Asiriya akadzalowa mʼdziko lathu

ndi kuyamba kuthira nkhondo malo athu otetezedwa,

tidzawadzutsira abusa asanu ndi awiri,

ngakhalenso atsogoleri asanu ndi atatu.

6Iwo adzagonjetsa dziko la Asiriya ndi lupanga,

dziko la Nimurodi adzalilamulira mwankhondo.

Adzatipulumutsa kwa Asiriya

akadzafika mʼmalire a mʼdziko lathu

kudzatithira nkhondo.

7Otsalira a Yakobo adzakhala

pakati pa mitundu yambiri ya anthu

ngati mame ochokera kwa Yehova,

ngati mvumbi pa udzu,

omwe sulamulidwa ndi munthu

kapena kudikira lamulo la anthu.

8Otsala a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu ya anthu,

mʼgulu la anthu a mitundu yambiri,

ngati mkango pakati pa nyama za mʼnkhalango.

Ngati mwana wa mkango pakati pa gulu la nkhosa,

amene pozidutsa amazidya ndi kuzikhadzula,

ndipo palibe angathe kuzilanditsa.

9Mudzagonjetsa adani anu,

ndipo adani anu onse adzawonongeka.

10Yehova akuti,

“Tsiku limenelo ndidzawononga akavalo anu onse

ndi kuphwasula magaleta anu.

11Ndidzawononga mizinda ya mʼdziko mwanu

ndi kugwetsa malinga anu onse.

12Ndidzawononga ufiti wanu

ndipo sikudzakhalanso anthu owombeza mawula.

13Ndidzawononga mafano anu osema

pamodzi ndi miyala yanu yopatulika imene ili pakati panu;

simudzagwadiranso zinthu zopanga

ndi manja anu.

14Ndidzazula mitengo ya mafano a Asera imene ili pakati panu,

ndipo ndidzawononga mizinda yanu.

15Ndidzayilanga mwaukali ndi mokwiya

mitundu imene sinandimvere Ine.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

弥迦书 5:1-15

耶和华的应许

1耶路撒冷的居民5:1 耶路撒冷的居民”希伯来文是“被围攻的女子”。啊,

现在你们要调集军队!

敌人正四面围攻我们,

要用杖击打以色列首领的脸颊。

2以法他伯利恒啊,

你在犹大各城中毫不起眼,

但将有一位从你那里出来,

为我统治以色列

祂的根源自亘古,来自太初。

3耶和华要将以色列人交给他们的敌人,

直到那临盆的妇人生下儿子。

那时,祂流亡的弟兄将重返他们的以色列同胞那里。

4祂要挺身而起,

倚靠耶和华的能力,

奉祂上帝耶和华的威名牧养祂的群羊。

他们将安然居住,

因为那时祂必受尊崇,直达地极。

5祂必给他们带来平安!

亚述人侵略我们的国土、践踏我们的宫殿时,

我们将选立七位牧者和八位首领抗击他们。

6他们要用刀剑统治亚述,统治宁录地区。

亚述人侵入我们国境、践踏我们疆土时,

祂必拯救我们。

7雅各余剩的子孙将在万民中像从耶和华那里降下的雨露,

又像洒在草上的甘霖。

他们不依靠人,

不冀望于世人。

8在各国各民中,

雅各余剩的子孙犹如林间百兽中的狮子,

又像闯入羊群的猛狮,

将猎物扑倒撕碎,

无人能搭救。

9愿你们伸手战胜仇敌!

愿你们的仇敌都被铲除!

10耶和华说:

“到那日,

我要消灭你们的战马,

毁坏你们的战车。

11我要摧毁你们境内的城邑,

拆除你们所有的堡垒。

12我要除掉你们手中的巫术,

使你们那里不再有占卜的。

13我要从你们中间除去雕刻的神像和神柱,

使你们不再跪拜自己所造的。

14我要从你们中间铲除亚舍拉神像,

毁灭你们的偶像。

15我要在烈怒中报应那些不听从我的国家。”