Mika 3 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mika 3:1-12

Atsogoleri ndi Aneneri Adzudzulidwa

1Ndipo ine ndinati,

“Tamverani, inu atsogoleri a Yakobo,

inu olamulira nyumba ya Israeli.

Kodi sindinu oyenera kudziwa kuweruza molungama,

2inu amene mumadana ndi zabwino ndi kukonda zoyipa;

inu amene mumasenda khungu la anthu anga,

ndipo mumakungunula mnofu pa mafupa awo;

3inu amene mumadya anthu anga,

mumasenda khungu lawo

ndi kuphwanya mafupa awo;

inu amene mumawadula nthulinthuli

ngati nyama yokaphika?”

4Pamenepo adzalira kwa Yehova,

koma Iye sadzawayankha.

Nthawi imeneyo Iye adzawabisira nkhope yake

chifukwa cha zoyipa zimene anazichita.

5Yehova akuti,

“Aneneri amene

amasocheretsa anthu anga,

ngati munthu wina awapatsa chakudya

amamufunira ‘mtendere;’

ngati munthu wina sawapatsa zakudya

amamulosera zoyipa.

6Nʼchifukwa chake kudzakuderani,

simudzaonanso masomphenya,

mdima udzakugwerani ndipo simudzawombezanso.

Dzuwa lidzawalowera aneneriwo, ndipo mdima udzawagwera.

7Alosi adzachita manyazi

ndipo owombeza mawula adzanyazitsidwa.

Onse adzaphimba nkhope zawo

chifukwa Mulungu sakuwayankha.”

8Koma kunena za ine, ndadzazidwa ndi mphamvu,

ndi Mzimu wa Yehova,

ndi kulungama, ndi kulimba mtima,

kuti ndilalikire za kugalukira kwa Yakobo,

kwa Israeli za tchimo lake.

9Imvani izi, inu atsogoleri a nyumba ya Yakobo,

inu olamulira nyumba ya Israeli,

inu amene mumadana ndi kuweruza kolungama;

ndipo mumakhotetsa zinthu zonse zolondola;

10inu amene mukumanga Ziyoni pokhetsa magazi,

ndi Yerusalemu ndi kuyipa kwanu.

11Atsogoleri ake amalandira chiphuphu kuti aweruze,

ansembe ake amalandira malipiro kuti alalikire,

ndipo aneneri ake amanenera kuti alandire ndalama.

Komatu amatsamira pa Yehova nʼkumanena kuti,

“Kodi Yehova sali pakati pathu?

Palibe tsoka limene lidzatigwere.”

12Choncho chifukwa cha inu,

Ziyoni adzatipulidwa ngati munda,

Yerusalemu adzasanduka bwinja,

ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.

King James Version

Micah 3:1-12

1And I said, Hear, I pray you, O heads of Jacob, and ye princes of the house of Israel; Is it not for you to know judgment? 2Who hate the good, and love the evil; who pluck off their skin from off them, and their flesh from off their bones; 3Who also eat the flesh of my people, and flay their skin from off them; and they break their bones, and chop them in pieces, as for the pot, and as flesh within the caldron. 4Then shall they cry unto the LORD, but he will not hear them: he will even hide his face from them at that time, as they have behaved themselves ill in their doings.

5¶ Thus saith the LORD concerning the prophets that make my people err, that bite with their teeth, and cry, Peace; and he that putteth not into their mouths, they even prepare war against him. 6Therefore night shall be unto you, that ye shall not have a vision; and it shall be dark unto you, that ye shall not divine; and the sun shall go down over the prophets, and the day shall be dark over them.3.6 that…: vision: Heb. from a vision3.6 that…: divine: Heb. from divining 7Then shall the seers be ashamed, and the diviners confounded: yea, they shall all cover their lips; for there is no answer of God.3.7 lips: Heb. upper lip

8¶ But truly I am full of power by the spirit of the LORD, and of judgment, and of might, to declare unto Jacob his transgression, and to Israel his sin. 9Hear this, I pray you, ye heads of the house of Jacob, and princes of the house of Israel, that abhor judgment, and pervert all equity. 10They build up Zion with blood, and Jerusalem with iniquity.3.10 blood: Heb. bloods 11The heads thereof judge for reward, and the priests thereof teach for hire, and the prophets thereof divine for money: yet will they lean upon the LORD, and say, Is not the LORD among us? none evil can come upon us.3.11 and say: Heb. saying 12Therefore shall Zion for your sake be plowed as a field, and Jerusalem shall become heaps, and the mountain of the house as the high places of the forest.