Mika 2 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mika 2:1-13

Zokonzekera za Munthu ndi Zokonzekera za Mulungu

1Tsoka kwa amene amakonzekera chiwembu,

kwa amene amakonzekera kuchita zoyipa usiku pa mabedi awo!

Kukacha mmawa amakachitadi

chifukwa ali ndi mphamvu zochitira zimenezo.

2Amasirira minda ndi kuyilanda,

amasirira nyumba ndi kuzilanda.

Amatenga nyumba ya munthu mwachinyengo,

munthu mnzawo kumulanda cholowa chake.

3Nʼchifukwa chake Yehova akuti,

“Ine ndikukonzekera kubweretsa tsoka pa anthu awa,

tsoka limene simudzatha kudzipulumutsa nokha.

Inu simudzayendanso monyada,

pakuti idzakhala nthawi ya masautso.

4Tsiku limenelo anthu adzakuchitani chipongwe;

adzakunyogodolani ndi nyimbo iyi yamaliro:

‘Tawonongeka kotheratu;

dziko la anthu anga lagawidwa.

Iye wandilanda!

Wapereka minda yathu kwa anthu otiwukira.’ ”

5Nʼchifukwa chake simudzakhala ndi munthu mu msonkhano wa Yehova

kuti agawe dziko pochita maere.

Aneneri Onyenga

6Aneneri awo amanena kuti, “Usanenere!

Usanenere ndi pangʼono pomwe zimenezi;

ife sitidzachititsidwa manyazi.”

7Inu nyumba ya Yakobo, monga zimenezi ndi zoyenera kuzinena:

“Kodi Mzimu wa Yehova wakwiya?

Kodi Iye amachita zinthu zotere?”

“Kodi mawu ake sabweretsa zabwino

kwa amene amayenda molungama?

8Posachedwapa anthu anga andiwukira

ngati mdani.

Mumawavula mkanjo wamtengowapatali

anthu amene amadutsa mosaopa kanthu,

monga anthu amene akubwera ku nkhondo.

9Mumatulutsa akazi a anthu anga

mʼnyumba zawo zabwino.

Mumalanda ana awo madalitso anga

kosatha.

10Nyamukani, chokani!

Pakuti ano si malo anu opumulirapo,

chifukwa ayipitsidwa,

awonongedwa, sangatheke kuwakonzanso.

11Ngati munthu wabodza ndi wachinyengo abwera nʼkunena kuti,

‘Ine ndidzanenera ndipo mudzakhala ndi vinyo ndi mowa wambiri,

woteroyo adzakhala mneneri amene anthu awa angamukonde!’

Alonjeza Chipulumutso

12“Inu banja la Yakobo, ndidzakusonkhanitsani nonse;

ndidzawasonkhanitsa pamodzi otsala a ku Israeli.

Ndidzawabweretsa pamodzi ngati nkhosa mʼkhola,

ngati ziweto pa msipu wake;

malowo adzadzaza ndi chinamtindi cha anthu.

13Amene adzawapulumutse adzayenda patsogolo pawo;

iwo adzathyola chipata ndipo adzatuluka.

Mfumu yawo idzawatsogolera,

Yehova adzakhala patsogolo pawo.”

O Livro

Miqueias 2:1-13

Os planos de Deus e do homem

1Ai de ti que tens prazer em te levantares de noite, para tecer conspirações de maldade! Sais de madrugada para dar cumprimento aos esquemas que ardilaste; tens a oportunidade de o fazer e fazes mesmo. 2Pretendes um determinado pedaço de terra ou a casa de uma pessoa qualquer, ainda que seja tudo o que ela possui, e consegues obter o que queres, à força de falsidade e violência.

3Mas o Senhor diz-te: “Receberás maldade em recompensa da tua maldade; nada me poderá deter. Nunca mais tornarás a ser orgulhoso e altivo, pensando que eu estou do teu lado. 4Os teus adversários rir-se-ão de ti e zombarão do teu desespero. Vocês dirão: ‘Estamos perdidos, arruinados! Deus confiscou-nos a terra e mandou-nos para o fim do mundo, o que era nosso, deu-o a outros!’ ”

5Sim, com efeito serão outros que delimitarão as vossas fronteiras. O povo do Senhor passará a viver onde os outros quiserem.

Profetas falsos

6“Não digas essas coisas!”, clama o povo. “Não insistas com coisas semelhantes! É desagradável, uma conversa dessas! Nunca semelhantes males nos poderiam acontecer!”

7Será essa a resposta que se espera de vocês, ó descendência de Jacob? Terá o Espírito do Senhor perdido a paciência? É assim que ele procede?

“Não! Eis que as minhas palavras fazem bem àquele que anda corretamente! 8Mesmo agora o meu povo levanta-se contra mim, porque roubam descaradamente daqueles que confiam em vocês, que caminham em paz. 9Expulsaram as mulheres do meu povo das suas casas; roubaram aos seus meninos os direitos que eu lhes dava.

10Levantem-se! Vão-se embora! Aqui já não é mais o vosso lar! Encheram isto tudo de corrupção!

11‘Eu vos pregarei as alegrias do vinho, as alegrias da bebida!’ É essa a espécie de profecias que gostariam de ouvir dos vossos profetas beberrões e mentirosos!

A libertação é prometida

12Mas há de vir o tempo, ó Israel, em que juntarei aqueles que restam, vos juntarei como cordeiros num rebanho, como um rebanho nas pastagens; será uma multidão barulhenta e feliz. 13Alguém irá adiante, abrindo o caminho, e seguirá atrás dele todo o rebanho, saindo pela porta da cidade. E o seu Rei, o Senhor, os conduzirá.”