Mika 1 – CCL & NAV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mika 1:1-16

1Yehova anayankhula ndi Mika wa ku Moreseti pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda. Awa ndi masomphenya amene iye anaona onena za Samariya ndi Yerusalemu.

2Tamverani, inu anthu a mitundu yonse,

mvetsera iwe dziko lapansi ndi okhala mʼmenemo,

pakuti Ambuye Yehova achitira umboni wokutsutsani,

Ambuye akuyankhula ali mʼnyumba yake yopatulika.

Chiweruzo cha Samariya ndi Yerusalemu

3Taonani! Yehova akubwera kuchokera ku malo ake;

Iye akutsika ndipo akuponda pa malo okwera a dziko lapansi.

4Mapiri akusungunuka pansi pake,

ndipo zigwa zikugawikana

ngati phula pa moto,

ngati madzi ochokera mʼphiri.

5Zonsezi ndi chifukwa cha cholakwa cha Yakobo,

chifukwa cha machimo a nyumba ya Israeli.

Kodi cholakwa cha Yakobo nʼchiyani?

Kodi si Samariya?

Kodi malo achipembedzo a Yuda ndi ati?

Kodi si Yerusalemu?

6“Choncho Ine ndidzasandutsa Samariya kukhala bwinja,

malo odzalamo mphesa.

Miyala yake ndidzayitaya ku chigwa

ndipo ndidzafukula maziko ake.

7Mafano ake onse ndidzawaphwanyaphwanya;

mphatso zake zonse ndidzazitentha ndi moto;

ndidzawononga zifanizo zonse za milungu yake.

Popeza analandira mphatso zake kuchokera ku malipiro a akazi achiwerewere,

mphatsozonso zidzagwiritsidwa ntchito ndi ena ngati malipiro a akazi achiwerewere.”

Kulira ndi Kumva Chisoni

8Chifukwa cha zimenezi ine ndidzalira momvetsa chisoni;

ndidzayenda wopanda nsapato ndi wamaliseche.

Ndidzafuwula ngati nkhandwe

ndi kulira ngati kadzidzi.

9Pakuti chilonda cha Samariya nʼchosachizika;

chafika ku Yuda.

Chafika pa chipata chenicheni cha anthu anga,

mpaka mu Yerusalemu mwenimwenimo.

10Musanene zimenezi ku Gati;

musalire nʼkomwe.

Mugubuduzike mu fumbi

ku Beti-Leafura.

11Inu anthu okhala ku Safiro,

muzipita ku ukapolo muli amaliseche ndi amanyazi.

Iwo amene akukhala ku Zanaani

sadzatuluka.

Beti-Ezeli akulira mwachisoni;

chitetezo chake chakuchokerani.

12Anthu amene amakhala ku Maroti akubuwula ndi ululu,

akuyembekezera thandizo,

chifukwa Yehova wabweretsa tsoka,

lafika mpaka pa chipata cha Yerusalemu.

13Inu anthu okhala ku Lakisi

mangani akavalo ku magaleta.

Inu amene munayamba kuchimwitsa

mwana wamkazi wa Ziyoni,

pakuti zolakwa za Israeli

zinapezeka pakati panu.

14Chifukwa chake perekani mphatso zolawirana

ndi a ku Moreseti Gati.

Mzinda wa Akizibu udzaonetsa kunama

kwa mafumu a Israeli.

15Ndidzabweretsa mgonjetsi kudzalimbana ndi inu

okhala mu Maresa.

Ulemerero wa Israeli udzafika

ku Adulamu.

16Metani mipala mitu yanu kuonetsa kuti mukulirira

ana anu amene mumawakonda;

mudzichititse dazi ngati dembo,

pakuti anawo adzatengedwa pakati panu kupita ku ukapolo.

Ketab El Hayat

ميخا 1:1-16

1هَذِهِ كَلِمَةُ الرَّبِّ الَّتِي أَوْحَى بِها إِلَى مِيخَا الْمُورَشْتِيِّ فِي أَثْنَاءِ حُكْمِ يُوثَامَ وَآحَازَ وَحَزَقِيَّا مُلُوكِ يَهُوذَا، بِشَأْنِ السَّامِرَةِ وَأُورُشَلِيمَ. 2اسْمَعُوا يَا جَمِيعَ الشُّعُوبِ، وَأَصْغِي أَيَّتُهَا الأَرْضُ وَكُلُّ مَنْ فِيهَا، وَلْيَكُنِ السَّيِّدُ الرَّبُّ مِنْ هَيْكَلِهِ الْمُقَدَّسِ شَاهِداً عَلَيْكُمْ.

دينونة الله على السامرة وأورشليم

3انْظُرُوا: هَا هُوَ الرَّبُّ خَارِجٌ مِنْ مَقَرِّ سُكْنَاهُ. هُوَذَا يَنْزِلُ لِيَطَأَ مَشَارِفَ الأَرْضِ، 4فَتَذُوبُ الْجِبَالُ مِنْ تَحْتِ قَدَمَيْهِ، وَتَتَصَدَّعُ الْوِدْيَانُ كَالشَّمْعِ أَمَامَ النَّارِ، كَالْمِيَاهِ الْمُنْصَبَّةِ فِي الْمُنْخَفَضَاتِ. 5مِنْ أَجْلِ آثَامِ يَعْقُوبَ وَمِنْ أَجْلِ خَطَايَا بَيْتِ إِسْرَائِيلَ. فَمَا هُوَ ذَنْبُ يَعْقُوبَ؟ أَلَيْسَ هُوَ أَصْنَامَ السَّامِرَةِ؟ وَمَا هِيَ خَطِيئَةُ يَهُوذَا؟ أَلَيْسَتْ هِيَ أَوْثَانَ أُورُشَلِيمَ؟ 6لِذَلِكَ سَأَجْعَلُ السَّامِرَةَ كَوْمَةَ حِجَارَةٍ فِي الْحَقْلِ وَمَغْرَساً لِلْكُرُومِ، وَأَقْذِفُ بِحِجَارَتِهَا إِلَى الْوَادِي، وَأُعَرِّي أَسَاسَاتِهَا. 7فَتَتَحَطَّمُ كُلُّ أَصْنَامِهَا، وَتُحْرَقُ كُلُّ تَقْدِمَاتِ زِنَاهَا بِالنَّارِ، وَأُدَمِّرُ جَمِيعَ تَمَاثِيلِهَا لأَنَّهَا جَمَعَتْهَا مِنْ أُجْرَةِ زَانِيَةٍ، وَإِلَى زَانِيَةٍ يَكُونُ مَآلُهَا.

نواح وولولة

8لِهَذَا أَنُوحُ وَأُوَلْوِلُ وَأَمْشِي حَافِياً عُرْيَاناً، وَأُعْوِلُ كَبَنَاتِ آوَى، وَأَنْتَحِبُ كَالنَّعَامِ. 9لأَنَّ جُرُوحَ السَّامِرَةِ لَنْ تَنْدَمِلَ، وَهِيَ لابُدَّ أَنْ تُصِيبَ يَهُوذَا، هَا هِيَ قَدْ بَلَغَتْ أَبْوَابَ شَعْبِي أَهْلِ أُورُشَلِيمَ.

10لَا تُخْبِرُوا فِي جَتَّ، وَلا تَبْكُوا فِي عَكَّاءَ. عَفِّرُوا أَنْفُسَكُمْ بِالتُّرَابِ فِي بَيْتِ عَفْرَةَ. 11اخْرُجُوا يَا أَهْلَ شَافِيرَ عَرَايَا مُجَلَّلِينَ بِالْعَارِ، وَلْيَمْكُثْ سُكَّانُ صَانَانَ فِي مَنَازِلِهِمْ خَجَلاً. وَعِنْدَمَا تَسْمَعُونَ عَوِيلَ أَهْلِ هَأَيْصِلَ تُدْرِكُونَ أَنَّهَا قَدْ سَقَطَتْ وَلا مَلْجَأَ لَكُمْ فِيهَا. 12لَشَدَّ مَا انْتَظَرَ أَهْلُ مَارُوثَ الْخَيْرَ، غَيْرَ أَنَّ الشَّرَّ قَدْ أَقْبَلَ عَلَى بَابِ أُورُشَلِيمَ مِنْ عِنْدِ الرَّبِّ. 13شُدُّوا الْخَيْلَ إِلَى الْمَرْكَبَاتِ يَا سُكَّانَ لاخِيشَ، لأَنَّكُمْ كُنْتُمْ أَوَّلَ مَنِ ارْتَكَبَ الْخَطِيئَةَ بَيْنَ مُدُنِ صِهْيَوْنَ، وَفِيكُمْ قَدْ وُجِدَتْ آثَامُ إِسْرَائِيلَ. 14لِهَذَا تَحْمِلُونَ هَدَايَا وَدَاعٍ إِلَى مُورَشَةِ جَتَّ، وَتُصْبِحُ مَدِينَةُ أَكْزِيبَ خِدْعَةً لِمُلُوكِ إِسْرَائِيلَ. 15وَأَبْعَثُ إِلَيْكُمْ بِقَاهِرٍ يَا أَهْلَ مَرِيشَةَ، فَيَهْرُبُ مِنْ أَمَامِهِ نُبَلاءُ إِسْرَائِيلَ إِلَى مَغَارَةِ عَدُلَّامَ. 16احْلِقُوا رُؤُوسَكُمْ وَجُزُّوا شُعُورَكُمْ مِنْ أَجْلِ أَبْنَاءِ مَسَرَّتِكُمْ. اجْعَلُوا رُؤُوسَكُمْ صَلْعَاءَ كَرَأْسِ النَّسْرِ، لأَنَّهُمْ سَيُؤْخَذُونَ مِنْكُمْ إِلَى السَّبْيِ.