Mika 1 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mika 1:1-16

1Yehova anayankhula ndi Mika wa ku Moreseti pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda. Awa ndi masomphenya amene iye anaona onena za Samariya ndi Yerusalemu.

2Tamverani, inu anthu a mitundu yonse,

mvetsera iwe dziko lapansi ndi okhala mʼmenemo,

pakuti Ambuye Yehova achitira umboni wokutsutsani,

Ambuye akuyankhula ali mʼnyumba yake yopatulika.

Chiweruzo cha Samariya ndi Yerusalemu

3Taonani! Yehova akubwera kuchokera ku malo ake;

Iye akutsika ndipo akuponda pa malo okwera a dziko lapansi.

4Mapiri akusungunuka pansi pake,

ndipo zigwa zikugawikana

ngati phula pa moto,

ngati madzi ochokera mʼphiri.

5Zonsezi ndi chifukwa cha cholakwa cha Yakobo,

chifukwa cha machimo a nyumba ya Israeli.

Kodi cholakwa cha Yakobo nʼchiyani?

Kodi si Samariya?

Kodi malo achipembedzo a Yuda ndi ati?

Kodi si Yerusalemu?

6“Choncho Ine ndidzasandutsa Samariya kukhala bwinja,

malo odzalamo mphesa.

Miyala yake ndidzayitaya ku chigwa

ndipo ndidzafukula maziko ake.

7Mafano ake onse ndidzawaphwanyaphwanya;

mphatso zake zonse ndidzazitentha ndi moto;

ndidzawononga zifanizo zonse za milungu yake.

Popeza analandira mphatso zake kuchokera ku malipiro a akazi achiwerewere,

mphatsozonso zidzagwiritsidwa ntchito ndi ena ngati malipiro a akazi achiwerewere.”

Kulira ndi Kumva Chisoni

8Chifukwa cha zimenezi ine ndidzalira momvetsa chisoni;

ndidzayenda wopanda nsapato ndi wamaliseche.

Ndidzafuwula ngati nkhandwe

ndi kulira ngati kadzidzi.

9Pakuti chilonda cha Samariya nʼchosachizika;

chafika ku Yuda.

Chafika pa chipata chenicheni cha anthu anga,

mpaka mu Yerusalemu mwenimwenimo.

10Musanene zimenezi ku Gati;

musalire nʼkomwe.

Mugubuduzike mu fumbi

ku Beti-Leafura.

11Inu anthu okhala ku Safiro,

muzipita ku ukapolo muli amaliseche ndi amanyazi.

Iwo amene akukhala ku Zanaani

sadzatuluka.

Beti-Ezeli akulira mwachisoni;

chitetezo chake chakuchokerani.

12Anthu amene amakhala ku Maroti akubuwula ndi ululu,

akuyembekezera thandizo,

chifukwa Yehova wabweretsa tsoka,

lafika mpaka pa chipata cha Yerusalemu.

13Inu anthu okhala ku Lakisi

mangani akavalo ku magaleta.

Inu amene munayamba kuchimwitsa

mwana wamkazi wa Ziyoni,

pakuti zolakwa za Israeli

zinapezeka pakati panu.

14Chifukwa chake perekani mphatso zolawirana

ndi a ku Moreseti Gati.

Mzinda wa Akizibu udzaonetsa kunama

kwa mafumu a Israeli.

15Ndidzabweretsa mgonjetsi kudzalimbana ndi inu

okhala mu Maresa.

Ulemerero wa Israeli udzafika

ku Adulamu.

16Metani mipala mitu yanu kuonetsa kuti mukulirira

ana anu amene mumawakonda;

mudzichititse dazi ngati dembo,

pakuti anawo adzatengedwa pakati panu kupita ku ukapolo.

Hoffnung für Alle

Micha 1:1-16

Eine Gerichtsbotschaft für Israel und Juda

(Kapitel 1–3)

Samarias Untergang

1In diesem Buch sind die Botschaften aufgeschrieben, die Micha aus Moreschet vom Herrn empfing. Während der Regierungszeit der judäischen Könige Jotam, Ahas und Hiskia offenbarte ihm Gott, was mit Samaria und Jerusalem geschehen würde:

2Hört zu, all ihr Völker! Gebt acht, ihr Bewohner der Erde! Gott, der Herr, tritt als Zeuge gegen Israel1,2 Wörtlich: gegen euch. – Vom Zusammenhang her sind hier wahrscheinlich die Israeliten angesprochen. auf, er kommt aus seinem heiligen Tempel. 3Seht! Von seiner Wohnung im Himmel steigt er herab und schreitet über die Gipfel der Erde. 4Unter seinen Schritten schmelzen die Berge wie Wachs im Feuer, sie fließen in die Ebene, wie Wasser den Abhang hinabschießt. In den Tälern brechen tiefe Spalten auf.

5Dies geschieht, weil die Israeliten, die Nachkommen von Jakob, gegen den Herrn gesündigt und ihm den Rücken gekehrt haben. Wer ist verantwortlich für Israels Schuld? Seine Hauptstadt Samaria! Und wer hat Juda zum Götzendienst an den Opferstätten verführt? Seine Hauptstadt Jerusalem!

6Darum sagt der Herr: »Ich werde Samaria bis auf die Grundmauern niederreißen und die Trümmer ins Tal hinunterwerfen. Ich mache die Stadt dem Erdboden gleich; dort, wo sie lag, wird man dann Weinberge anlegen! 7Alle Götzenstatuen von Samaria lasse ich in Stücke hauen, die geschnitzten Bilder werden ein Raub der Flammen. Mit den kostbaren Gegenständen, die man vom Lohn der Tempelhuren angeschafft hat, bezahlen die Plünderer dann wiederum ihre Huren.«

Micha trauert über das Schicksal seines Volkes

8Darum klage und weine ich, voller Trauer gehe ich barfuß und ohne Obergewand umher. Ich heule wie ein Schakal, schreie wie ein Strauß. 9Denn Samarias Wunden sind unheilbar, und auch Juda wird nicht verschont. Ja, selbst Jerusalem, die Hauptstadt meines Volkes, ist dem Untergang nah!

10Erzählt den Philistern in Gat nichts davon, zeigt ihnen nicht eure Tränen! Wälzt euch vor Verzweiflung im Staub von Bet-Leafra!1,10 Die Verse 10‒15 enthalten im hebräischen Text zahlreiche Wortspiele im Zusammenhang mit den Ortsnamen. Zum Beispiel klingt das hebräische Wort für »erzählen« im Namen Gat an und »Staub« in Bet-Leafra. 11Flieht nackt in Schimpf und Schande, ihr Einwohner von Schafir! Ihr von Zaanan, ihr werdet es nicht einmal mehr wagen, eure Stadt zu verlassen! Bet-Ezel bietet euch keinen Schutz mehr, man hört dort nur noch lautes Klagen. 12Die Einwohner von Marot zittern vor Angst und hoffen, noch einmal davonzukommen,1,12 Oder: Die Einwohner von Marot bangen um ihr Hab und Gut. denn der Herr lässt die Feinde schon bis vor die Tore von Jerusalem heranrücken.

13Spannt die Pferde an und flieht, ihr Leute von Lachisch! Ihr habt die Menschen in Zion zur Sünde verführt, ihr seid genauso gottlos wie das Nordreich Israel! 14Darum müsst ihr auch Moreschet im Gebiet von Gat hergeben. Auf die Stadt Achsib hatten die Könige von Israel ihre Hoffnung gesetzt. Doch sie werden enttäuscht wie von einem Bach, dessen Wasser im Sommer versiegt.

15Ihr Einwohner von Marescha, eure Stadt wird ebenfalls dem Eroberer zum Opfer fallen, den Gott euch schickt! Dann werden sich Israels vornehme Männer in der Adullamhöhle verstecken müssen.1,15 Wörtlich: Die Herrlichkeit Israels wird bis Adullam kommen. 16Schneide dir in Trauer die Haare ab, Juda, bis du kahl bist wie ein Geier! Denn deine Bewohner, deine geliebten Kinder, werden in ein fremdes Land verschleppt!