Mika 1 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mika 1:1-16

1Yehova anayankhula ndi Mika wa ku Moreseti pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda. Awa ndi masomphenya amene iye anaona onena za Samariya ndi Yerusalemu.

2Tamverani, inu anthu a mitundu yonse,

mvetsera iwe dziko lapansi ndi okhala mʼmenemo,

pakuti Ambuye Yehova achitira umboni wokutsutsani,

Ambuye akuyankhula ali mʼnyumba yake yopatulika.

Chiweruzo cha Samariya ndi Yerusalemu

3Taonani! Yehova akubwera kuchokera ku malo ake;

Iye akutsika ndipo akuponda pa malo okwera a dziko lapansi.

4Mapiri akusungunuka pansi pake,

ndipo zigwa zikugawikana

ngati phula pa moto,

ngati madzi ochokera mʼphiri.

5Zonsezi ndi chifukwa cha cholakwa cha Yakobo,

chifukwa cha machimo a nyumba ya Israeli.

Kodi cholakwa cha Yakobo nʼchiyani?

Kodi si Samariya?

Kodi malo achipembedzo a Yuda ndi ati?

Kodi si Yerusalemu?

6“Choncho Ine ndidzasandutsa Samariya kukhala bwinja,

malo odzalamo mphesa.

Miyala yake ndidzayitaya ku chigwa

ndipo ndidzafukula maziko ake.

7Mafano ake onse ndidzawaphwanyaphwanya;

mphatso zake zonse ndidzazitentha ndi moto;

ndidzawononga zifanizo zonse za milungu yake.

Popeza analandira mphatso zake kuchokera ku malipiro a akazi achiwerewere,

mphatsozonso zidzagwiritsidwa ntchito ndi ena ngati malipiro a akazi achiwerewere.”

Kulira ndi Kumva Chisoni

8Chifukwa cha zimenezi ine ndidzalira momvetsa chisoni;

ndidzayenda wopanda nsapato ndi wamaliseche.

Ndidzafuwula ngati nkhandwe

ndi kulira ngati kadzidzi.

9Pakuti chilonda cha Samariya nʼchosachizika;

chafika ku Yuda.

Chafika pa chipata chenicheni cha anthu anga,

mpaka mu Yerusalemu mwenimwenimo.

10Musanene zimenezi ku Gati;

musalire nʼkomwe.

Mugubuduzike mu fumbi

ku Beti-Leafura.

11Inu anthu okhala ku Safiro,

muzipita ku ukapolo muli amaliseche ndi amanyazi.

Iwo amene akukhala ku Zanaani

sadzatuluka.

Beti-Ezeli akulira mwachisoni;

chitetezo chake chakuchokerani.

12Anthu amene amakhala ku Maroti akubuwula ndi ululu,

akuyembekezera thandizo,

chifukwa Yehova wabweretsa tsoka,

lafika mpaka pa chipata cha Yerusalemu.

13Inu anthu okhala ku Lakisi

mangani akavalo ku magaleta.

Inu amene munayamba kuchimwitsa

mwana wamkazi wa Ziyoni,

pakuti zolakwa za Israeli

zinapezeka pakati panu.

14Chifukwa chake perekani mphatso zolawirana

ndi a ku Moreseti Gati.

Mzinda wa Akizibu udzaonetsa kunama

kwa mafumu a Israeli.

15Ndidzabweretsa mgonjetsi kudzalimbana ndi inu

okhala mu Maresa.

Ulemerero wa Israeli udzafika

ku Adulamu.

16Metani mipala mitu yanu kuonetsa kuti mukulirira

ana anu amene mumawakonda;

mudzichititse dazi ngati dembo,

pakuti anawo adzatengedwa pakati panu kupita ku ukapolo.

Священное Писание

Михей 1:1-16

Пролог

1Слово Вечного1:1 Вечный – на языке оригинала: «Яхве». Под этим именем Всевышний открылся Мусе и народу Исраила (см. Исх. 3:13-15). См. пояснительный словарь., которое было к Михею из Морешета в дни правления Иотама, Ахаза и Езекии, царей Иудеи1:1 Иотам, Ахаз и Езекия правили Иудеей в период с 752 по 686 гг. до н. э. Об их правлении см. 4 Цар. 15:32–20:21; 2 Лет. 27–32., – видение, которое было ему о Самарии и Иерусалиме.

2Слушайте, все народы,

внимай, земля, и всё, что на ней!

Пусть Владыка Вечный будет свидетелем против вас,

Владыка – из святого храма Своего.

Суд над Самарией и Иерусалимом

3Смотрите, Вечный выходит из Своего жилища;

Он нисходит и ступает по высотам земли.

4Плавятся горы под Ним,

как воск от огня,

раскалываются долины,

как вода, что льётся со склона.

5Всё это – за отступничество Якуба,

за грехи Исраила.

Кто ввёл Якуба в грех?

Разве не сама столица Самария?

Кто склонил Иудею к идолопоклонству?

Разве не сама столица Иерусалим?

6– За это Я сделаю Самарию грудой развалин,

среди которых разобьют виноградники.

Я низвергну её камни в долину

и обнажу её основания.

7Все её истуканы будут расколоты,

сожжены все храмовые дары;

Я уничтожу всех её идолов.

В уплату за блуд получала она эти дары,

и платой блудницам опять они станут.

Плач и горе

8Об этом я буду плакать и горевать,

буду скитаться босым и нагим.

Как шакал, буду выть,

и причитать – как сова,

9потому что рана Самарии неисцелима;

она дошла до Иудеи,

до ворот моего народа –

до самого Иерусалима.

10Не объявляйте об этом нашим врагам в Гате1:10 В стихах с 10 по 15 пророк прибегает к тонкой игре слов. Гат – на языке оригинала созвучно с глаголом «объявлять».,

не плачьте вовсе1:10 Или: «Не плачьте в Акко». На языке оригинала слова «в Акко» и «плакать» созвучны..

В Бет-Офре1:10 Бет-Офра – переводится как «дом пыли».

в знак скорби валяйтесь в пыли.

11Вы уйдёте в изгнание, горожане Шафира1:11 Шафир – переводится как «приятный».,

нагими и опозоренными.

Не смогут выйти из города

жители Цаанана1:11 Цаанан – на языке оригинала созвучно с глаголом «выйти»..

Плачет Бет-Ецель1:11 Бет-Ецель – переводится как «ближайший дом».

не дождётесь от него помощи.

12Ждут тревожно добрых вестей

горожане Марота1:12 Марот – переводится как «горечь».,

ведь Вечный ниспослал бедствия

к воротам Иерусалима.

13Запрягайте скакунов в колесницы,

обитатели Лахиша1:13 Лахиш – можно перевести как «упряжка (лошадей)»..

Вы были началом греха

для дочери Сиона1:13 Дочь Сиона – олицетворение Иерусалима; также в 4:8, 10 и 13.,

потому что с вас начались

преступления Исраила.

14Теперь пошлите прощальные подарки

Морешет-Гату.

Жители Ахзива1:14 Ахзив – переводится как «обман». окажутся обманом

для царей Исраила.

15Я опять приведу владельца к вам,

обитатели Мареши1:15 Мареша – на языке оригинала созвучно со словом «владелец»..

Вожди1:15 Букв.: «Слава». Исраила будут прятаться

в пещерах Адуллама.

16Обрейте головы в знак печали

о ваших милых сыновьях;

станьте лысыми, подобно грифу,

потому что в плен уводят их от вас.