Mateyu 6 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 6:1-34

Zopereka Zachifundo

1“Samalani kuti musachite ntchito zanu zolungama pamaso pa anthu kuti akuoneni. Popeza ngati mutero simudzalandira mphotho yochokera kwa Atate anu akumwamba.

2“Pamene mupereka zachifundo, musachite modzionetsera monga amachita achiphamaso mʼmasunagoge ndi pa misewu kuti atamidwe ndi anthu. Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti iwowo alandiriratu mphotho yawo yonse. 3Koma pamene mupereka zachifundo, dzanja lanu lamanzere lisadziwe chimene dzanja lanu lamanja likuchita, 4kotero kuti kupereka kwanu kukhale mwachinsinsi. Ndipo Atate anu amene amaona zochitika mwachinsinsi, adzakupatsani mphotho.

Za Kupemphera

5“Pamene mupemphera, musakhale ngati achiphamaso, chifukwa iwo amakonda kupemphera choyimirira mʼmasunagoge ndi pa mphambano za mʼmisewu kuti anthu awaone. Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti iwo alandiriratu mphotho yawo yonse. 6Koma pamene mupemphera, lowani mʼchipinda chanu chamʼkati, ndi kutseka chitseko ndipo mupemphere kwa Atate anu amene saoneka. Ndipo Atate anu, amene amaona zochitika mseri, adzakupatsani mphotho. 7Ndipo pamene mukupemphera, musamabwerezabwereza monga akunja, pakuti iwo amaganiza kuti adzamveka chifukwa chochulutsa mawu. 8Musakhale ngati iwo chifukwa Atate anu amadziwa zimene musowa musanapemphe.

9“Chifukwa chake pempherani motere:

“ ‘Atate athu akumwamba,

dzina lanu lilemekezedwe,

10Ufumu wanu ubwere,

chifuniro chanu chichitike

pansi pano monga kumwamba.

11Mutipatse chakudya chathu chalero.

12Mutikhululukire mangawa athu,

monga ifenso tawakhululukira amangawa athu.

13Ndipo musatitengere kokatiyesa;

koma mutipulumutse kwa woyipayo.’

14Ngati inu mukhululukira anthu pamene akuchimwirani, Atate anu akumwamba adzakukhululukirani. 15Koma ngati inu simukhululukira anthu zolakwa zawo, Atate anunso sadzakukhululukirani machimo anu.

Kusala Kudya

16“Pamene mukusala kudya, musaonetse nkhope yachisoni monga achita achiphamaso, pakuti iwo amasintha nkhope zawo kuonetsa anthu kuti akusala kudya. Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti iwo alandiriratu mphotho yawo yonse. 17Koma pamene ukusala kudya, samba mʼmaso nudzole mafuta kumutu, 18kuti usaonekere kwa anthu kuti ukusala kudya koma kwa Atate ako ali mseri; ndipo Atate ako amene amaona za mseri adzakupatsa mphotho.

Za Chuma cha Kumwamba

19“Musadziwunjikire chuma pa dziko lapansi, pamene njenjete ndi dzimbiri zimawononga ndi pamene mbala zimathyola ndi kuba. 20Koma mudziwunjikire chuma kumwamba kumene njenjete ndi dzimbiri siziwononga ndipo mbala sizithyola ndi kuba. 21Pakuti kumene kuli chuma chako, mtima wako udzakhala komweko.

Diso Nyale ya Thupi

22“Diso ndi nyale ya thupi. Ngati maso ako ali bwino, thupi lako lonse lidzakhala mʼkuwala. 23Koma ngati maso ako sali bwino, thupi lako lonse lidzakhala mu mdima. Koma ngati kuwala kuli mwa iwe ndi mdima, ndiye kuti mdimawo ndi waukulu bwanji!

24“Palibe munthu angathe kukhala kapolo wa ambuye awiri. Pakuti pena adzamuda mmodzi ndi kukonda winayo kapena adzagwira ntchito mokhulupirika kwa mmodzi, nadzanyoza winayo. Simungathe kukhala kapolo wa Mulungu ndi wa chuma pa nthawi imodzi.

Musade Nkhawa

25“Nʼchifukwa chake ndikuwuzani kuti musadere nkhawa za moyo wanu kuti mudzadya chiyani kapena mudzamwa chiyani; kapenanso za thupi lanu kuti mudzavala chiyani. Kodi moyo suposa chakudya? Kodi thupi siliposa zovala? 26Onani mbalame zamlengalenga sizifesa kapena kukolola kapena kusunga mʼnkhokwe komabe Atate anu akumwamba amazidyetsa. Kodi inu simuziposa kwambiri? 27Kodi ndani wa inu podandaula angathe kuwonjeza ora limodzi pa moyo wake?

28“Ndipo bwanji inu mudera nkhawa za zovala? Onani makulidwe a maluwa akutchire. Sagwira ntchito kapena kuwomba nsalu. 29Ndikukuwuzani kuti angakhale Solomoni mu ulemerero wake sanavale mofanana ndi limodzi la maluwa amenewa. 30Ngati umu ndi mmene Mulungu avekera udzu wa kutchire umene ulipo lero ndipo mawa uponyedwa ku moto, kodi sadzakuvekani koposa? Aa! Inu a chikhulupiriro chochepa! 31Chifukwa chake musadere nkhawa ndi kuti, ‘Tidzadya chiyani?’ kapena ‘Tidzamwa chiyani?’ kapena ‘Tidzavala chiyani?’ 32Pakuti anthu akunja amazifuna zinthu zonsezi ndipo Atate anu akumwamba adziwa kuti musowa zimenezi. 33Koma muyambe mwafuna ufumu wake ndi chilungamo chake ndipo zinthu zonsezi zidzapatsidwa kwa inu. 34Chifukwa chake musadere nkhawa ndi za mawa, popeza tsiku lililonse lili ndi zovuta zake zokwanira.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

馬太福音 6:1-34

論賙濟窮人

1「你們要小心,行善的時候不可張揚,故意叫人看見,否則就不能得你們天父的賞賜了。

2「因此,賙濟窮人的時候,不要大吹大擂,像那些偽君子在會堂和街市上所行的一樣,以博取人們的讚賞。我實在告訴你們,他們得到的賞賜僅此而已。 3你們賙濟窮人的時候,右手所做的別叫左手知道, 4要不聲不響地去做。這樣,鑒察隱祕事的天父必賞賜你們。

論禱告

5「你們禱告時,不要像偽君子那樣。他們喜歡站在會堂裡和十字路口上公開禱告,故意讓人看見。我實在告訴你們,他們得到的賞賜不過是人的讚賞。 6你們禱告的時候,要進入內室,關上門,向你們肉眼看不見的父祈禱,鑒察隱祕事的父必賞賜你們。

7「你們禱告時不可像外族人那樣喋喋不休,他們以為長篇大論,就必蒙上帝垂聽。 8不可像他們那樣,因為在你們禱告以前,你們的父已經知道你們的需要了。

9「你們應當這樣禱告,

『我們天上的父,

願人們都尊崇你的聖名,

10願你的國度降臨,

願你的旨意在地上成就,就像在天上成就一樣。

11求你今天賜給我們日用的飲食。

12饒恕我們的罪,

就像我們饒恕了得罪我們的人。

13不要讓我們遇見誘惑,

救我們脫離那惡者。

因為國度、權柄、榮耀都是你的,直到永遠。阿們!』

14「如果你們饒恕別人的過犯,你們的天父也必饒恕你們的過犯。 15如果你們不饒恕別人的過犯,你們的天父也不會饒恕你們的過犯。

論禁食

16「你們禁食的時候,不要像偽君子那樣愁眉苦臉,因為他們故意蓬頭垢面,好讓別人知道他們在禁食。我實在告訴你們,他們得到的賞賜不過是人的讚賞。 17你禁食的時候要梳頭洗臉, 18不叫人們看出你在禁食,只讓你肉眼看不見的父知道,鑒察隱祕事的父必賞賜你。

論積財

19「不要為自己在世上積攢財寶,世上有蟲子咬,會生銹,又有賊闖進來偷。 20你們要把財寶積攢在天上,天上沒有蟲子咬,不會生銹,也沒有賊闖進來偷。 21要知道,你的財寶在哪裡,你的心也在哪裡。

22「眼睛是身上的燈。如果你的眼睛明亮,全身都光明; 23要是你的眼睛昏花6·23 昏花」或作「邪惡」。,全身就黑暗。如果你裡面的光黑暗了,那黑暗是多麼大啊!

24「一個人不能服侍兩位主人,因為他不是恨這位、愛那位,就是重這位、輕那位。你們不能又事奉上帝,又崇拜金錢。

不要憂慮衣食

25「所以我告訴你們,不要為生活憂慮,如吃什麼、喝什麼,也不要為身體憂慮,如穿什麼。難道生命不比飲食重要嗎?身體不比穿著重要嗎?

26「你們看天上的飛鳥,牠們不種,不收,也不在倉裡積存糧食,你們的天父尚且養活牠們,難道你們還不如飛鳥貴重嗎? 27你們誰能用憂慮使自己多活片刻呢?

28「何必為穿著憂慮呢?你們看看野地的百合花是如何生長的,它們既不勞苦,也不紡織。 29但我告訴你們,就連所羅門王最顯赫時的穿戴還不如一朵百合花! 30你們的信心太小了!野地裡的草今天還在,明天就丟在爐中化為灰燼,上帝還這樣裝扮它們,何況你們呢? 31所以,你們不要憂慮『吃什麼?喝什麼?穿什麼?』 32因為這些都是外族人的追求,你們的天父知道你們的需要。

33「你們要先尋求上帝的國和祂的義,這一切都會賜給你們。 34所以,不要為明天憂慮,因為明天自有明天的憂慮,一天的難處一天擔就夠了。