Mateyu 28 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 28:1-20

Yesu Auka kwa Akufa

1Litapita tsiku la Sabata, mmawa wa tsiku loyamba la Sabata, Mariya wa ku Magadala ndi Mariya wina anapita kukaona manda.

2Kunachitika chivomerezi chachikulu, pakuti mngelo wa Ambuye anabwera kuchokera kumwamba ndipo anapita ku manda, nakagubuduza mwala nawukhalira. 3Maonekedwe ake anali ngati mphenzi ndipo zovala zake zinali mbuu ngati matalala. 4Alondawo anachita naye mantha kwambiri kotero kuti ananjenjemera ndi kuwuma ngati akufa.

5Mngelo anati kwa amayiwo, “Musachite mantha popeza ndikudziwa kuti mukufuna Yesu amene anapachikidwa. 6Iye muno mulibe, wauka monga mmene ananenera. Bwerani, dzaoneni malo amene anagona. 7Ndipo pitani msanga kawuzeni ophunzira ake kuti, ‘Wauka kwa akufa ndipo watsogola kupita ku Galileya. Mukamuona Iye kumeneko.’ Taonani ndakuwuzani.”

8Pamenepo amayiwo anachoka mofulumira ku mandako ali ndi mantha komabe atadzaza ndi chimwemwe, ndipo anathamanga kukawuza ophunzira ake. 9Mwadzidzidzi Yesu anakumana nawo nati, “Moni.” Iwo anabwera kwa Iye, nagwira mapazi ake namulambira. 10Ndipo Yesu anawawuza kuti, “Musachite mantha, pitani kawuzeni abale anga kuti apite ku Galileya ndipo kumeneko akandiona Ine.”

Uthenga wa Alonda

11Amayi aja akupita, ena mwa alonda aja anapita ku mzinda nafotokozera akulu a ansembe zonse zimene zinachitika. 12Akulu a ansembe atakumana ndi akuluakulu anapangana zochita. Anapatsa alonda aja ndalama zambiri, 13nawawuza kuti, “Muzinena kuti, ‘Ophunzira ake anabwera usiku ndipo amuba ife tili mtulo.’ 14Ngati nkhani iyi imupeze bwanamkubwa, ife tidzamukhazika mtima pansi ndipo simudzakhala mʼmavuto.” 15Pamenepo alondawo anatenga ndalamazo nachita monga mmene anawuzidwira. Ndipo mbiri iyi inawanda pakati pa Ayuda mpaka lero lino.

Yesu Atuma Ophunzira Ake

16Ndipo ophunzira khumi ndi mmodzi aja anapita ku Galileya, ku phiri limene Yesu anawawuza kuti apite. 17Atamuona Iye, anamulambira; koma ena anakayika. 18Kenaka Yesu anabwera kwa iwo nati, “Ulamuliro wonse kumwamba ndi dziko lapansi wapatsidwa kwa Ine. 19Chifukwa chake, pitani kaphunzitseni anthu a mitundu yonse, ndi kuwabatiza mʼdzina la Atate ndi la Mwana ndi la Mzimu Woyera, 20ndi kuwaphunzitsa amvere zonse zimene ndinakulamulirani. Ndipo onani, Ine ndidzakhala pamodzi ndi inu kufikira kutha kwa dziko lapansi pano.”

Słowo Życia

Mateusza 28:1-20

Zmartwychwstanie

1Po szabacie, pierwszego dnia tygodnia, wczesnym rankiem Maria z Magdali i druga Maria poszły obejrzeć grobowiec. 2Nagle gwałtownie zatrzęsła się ziemia. Anioł Pana zstąpił z nieba, odsunął kamień od grobowca i usiadł na nim. 3Wyglądał jak błyskawica, a jego szata—jak śnieg. 4Na jego widok strażnicy zadrżeli ze strachu i padli na ziemię jak martwi. 5Wtedy anioł odezwał się do kobiet:

—Nie bójcie się! Wiem, że szukacie Jezusa, którego ukrzyżowano. 6Nie ma Go tutaj! Powstał z martwych, jak zapowiedział. Wejdźcie i zobaczcie miejsce, gdzie był złożony! 7Teraz zaś szybko wracajcie do Jego uczniów i powiedzcie im: „On zmartwychwstał i oczekuje was w Galilei. Tam właśnie was spotka”. To miałem wam przekazać.

8Przestraszone, ale pełne radości, kobiety odeszły od grobowca i pobiegły powiedzieć o tym uczniom. 9Nagle na ich drodze stanął Jezus.

—Witajcie!—powiedział.

One zaś podeszły, padły Mu do nóg i oddały pokłon. 10Wtedy rzekł do nich:

—Nie bójcie się! Idźcie i powiedzcie moim braciom, aby udali się do Galilei. Tam się zobaczymy.

Raport straży

11Gdy były jeszcze w drodze, niektórzy strażnicy pilnujący grobowca udali się do miasta i opowiedzieli najwyższym kapłanom o wszystkim, co zaszło. 12Ci, po naradzie ze starszymi, dali strażnikom sporą łapówkę.

13—Rozpowiadajcie tak: Nocą, gdy spaliśmy, jego uczniowie przyszli i wykradli ciało—powiedzieli. 14—A gdyby gubernator usłyszał, że spaliście na służbie, obronimy was i uwolnimy od kłopotów.

15Strażnicy wzięli pieniądze i zrobili tak, jak im powiedziano. W ten sposób ta plotka rozeszła się wśród wszystkich mieszkańców Judei i trwa po dziś dzień.

Wielki nakaz misyjny

16Natomiast jedenastu uczniów, zgodnie z poleceniem Jezusa, udało się do Galilei, na górę. 17Gdy Go zobaczyli, oddali Mu pokłon, ale niektórzy z nich wciąż jeszcze wątpili. 18Jezus zbliżył się do nich i powiedział:

—Otrzymałem wszelką władzę w niebie i na ziemi. 19Idźcie więc i pozyskujcie uczniów ze wszystkich narodów, chrzcząc ich w imię Ojca i Syna, i Ducha Świętego. 20Uczcie ich przestrzegać wszystkiego, co wam poleciłem. Ja zaś będę z wami przez wszystkie dni—aż do końca czasów.