Mateyu 28 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 28:1-20

Yesu Auka kwa Akufa

1Litapita tsiku la Sabata, mmawa wa tsiku loyamba la Sabata, Mariya wa ku Magadala ndi Mariya wina anapita kukaona manda.

2Kunachitika chivomerezi chachikulu, pakuti mngelo wa Ambuye anabwera kuchokera kumwamba ndipo anapita ku manda, nakagubuduza mwala nawukhalira. 3Maonekedwe ake anali ngati mphenzi ndipo zovala zake zinali mbuu ngati matalala. 4Alondawo anachita naye mantha kwambiri kotero kuti ananjenjemera ndi kuwuma ngati akufa.

5Mngelo anati kwa amayiwo, “Musachite mantha popeza ndikudziwa kuti mukufuna Yesu amene anapachikidwa. 6Iye muno mulibe, wauka monga mmene ananenera. Bwerani, dzaoneni malo amene anagona. 7Ndipo pitani msanga kawuzeni ophunzira ake kuti, ‘Wauka kwa akufa ndipo watsogola kupita ku Galileya. Mukamuona Iye kumeneko.’ Taonani ndakuwuzani.”

8Pamenepo amayiwo anachoka mofulumira ku mandako ali ndi mantha komabe atadzaza ndi chimwemwe, ndipo anathamanga kukawuza ophunzira ake. 9Mwadzidzidzi Yesu anakumana nawo nati, “Moni.” Iwo anabwera kwa Iye, nagwira mapazi ake namulambira. 10Ndipo Yesu anawawuza kuti, “Musachite mantha, pitani kawuzeni abale anga kuti apite ku Galileya ndipo kumeneko akandiona Ine.”

Uthenga wa Alonda

11Amayi aja akupita, ena mwa alonda aja anapita ku mzinda nafotokozera akulu a ansembe zonse zimene zinachitika. 12Akulu a ansembe atakumana ndi akuluakulu anapangana zochita. Anapatsa alonda aja ndalama zambiri, 13nawawuza kuti, “Muzinena kuti, ‘Ophunzira ake anabwera usiku ndipo amuba ife tili mtulo.’ 14Ngati nkhani iyi imupeze bwanamkubwa, ife tidzamukhazika mtima pansi ndipo simudzakhala mʼmavuto.” 15Pamenepo alondawo anatenga ndalamazo nachita monga mmene anawuzidwira. Ndipo mbiri iyi inawanda pakati pa Ayuda mpaka lero lino.

Yesu Atuma Ophunzira Ake

16Ndipo ophunzira khumi ndi mmodzi aja anapita ku Galileya, ku phiri limene Yesu anawawuza kuti apite. 17Atamuona Iye, anamulambira; koma ena anakayika. 18Kenaka Yesu anabwera kwa iwo nati, “Ulamuliro wonse kumwamba ndi dziko lapansi wapatsidwa kwa Ine. 19Chifukwa chake, pitani kaphunzitseni anthu a mitundu yonse, ndi kuwabatiza mʼdzina la Atate ndi la Mwana ndi la Mzimu Woyera, 20ndi kuwaphunzitsa amvere zonse zimene ndinakulamulirani. Ndipo onani, Ine ndidzakhala pamodzi ndi inu kufikira kutha kwa dziko lapansi pano.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

馬太福音 28:1-20

耶穌復活

1安息日剛過,週日黎明時分,抹大拉瑪麗亞和另一位瑪麗亞一同到墳墓去察看。

2突然,大地劇烈地震動,上帝的天使從天而降,推開堵著墓穴的石頭,坐在上面。 3他的容貌如閃電,衣裳潔白如雪。 4看守墓穴的衛兵嚇得要死,渾身發抖。

5天使對那兩個女人說:「不要怕,我知道你們是在找那位被釘十字架的耶穌。 6祂不在這裡,正如祂所說的,祂已經復活了。你們來看,這是安放祂的地方。 7現在你們快回去,把這消息告訴祂的門徒,祂已經從死裡復活,先你們一步去了加利利,你們將在那裡見到祂。記住,我已經告訴你們了。」

8她們聽了又驚又喜,連忙離開墳墓,跑去告訴門徒。 9忽然,耶穌迎面而來,對她們說:「願你們平安!」她們就上前抱住祂的腳敬拜祂。

10耶穌對她們說:「不要害怕。去告訴我的弟兄,叫他們到加利利去,他們將在那裡見到我。」

行賄造謠

11她們還在趕路的時候,有些守墓的衛兵已經進城把整件事告訴祭司長。 12祭司長和長老聚集商議,決定用重金買通守墓的衛兵,又吩咐他們: 13「你們就說,『半夜裡我們熟睡的時候,耶穌的門徒把祂的屍體偷走了。』 14如果這件事傳到總督那裡,我們一定會替你們出面,保你們無事。」 15守衛收下錢,便依照吩咐去做。於是,這說法在猶太人中一直流傳到今天。

大使命

16十一個門徒趕到加利利,到了耶穌和他們約定的山上, 17看到耶穌就敬拜祂,但有些人仍然心存疑惑。 18耶穌上前對門徒說:

「天上地下所有的權柄都交給我了。 19所以,你們要去使萬民作我的門徒,奉父、子、聖靈的名給他們施洗, 20教導他們遵守我吩咐你們的一切。記住,我必常與你們同在,一直到世界的末了。」