Mateyu 26 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 26:1-75

Chiwembu cha Ayuda pa Yesu

1Yesu atamaliza kuyankhula zonsezi, anati kwa ophunzira ake, 2“Monga mukudziwa, kwatsala masiku awiri kuti Paska ifike ndipo Mwana wa Munthu adzaperekedwa kuti apachikidwe.”

3Pamenepo akulu a ansembe ndi akuluakulu anasonkhana ku nyumba ya mkulu wa ansembe dzina lake Kayafa, 4ndipo anapangana kuti amugwire Yesu mobisa ndi kumupha. 5Ndipo anati, “Osati nthawi yaphwando chifukwa pangabuke chipolowe pakati pa anthu.”

Yesu Adzozedwa ku Betaniya

6Yesu ali ku Betaniya mʼnyumba Simoni Wakhate, 7mayi wina anabwera kwa Iye ndi botolo la mafuta onunkhira a mtengowapatali, amene anathira pa mutu pake Iye akudya pa tebulo.

8Ophunzira ataona izi anayipidwa nafunsa kuti, “Chifukwa chiyani akuwononga chotere? 9Mafuta amenewa akanatha kugulitsidwa pa mtengo waukulu, ndipo ndalama zake zikanaperekedwa kwa osauka.”

10Yesu podziwa izi anawawuza kuti, “Chifukwa chiyani mukumuvutitsa mayiyu? Wandichitira Ine chinthu chabwino. 11Osauka mudzakhala nawo nthawi zonse, koma simudzakhala ndi Ine nthawi zonse. 12Pamene wathira mafuta onunkhirawa pa thupi langa, wachita izi kukonzekera kuyikidwa kwanga mʼmanda. 13Zoonadi, ndikuwuzani kuti kulikonse kumene Uthenga Wabwinowu udzalalikidwa ku dziko lonse lapansi, zimene wachitazi zidzanenedwanso pomukumbukira.”

Yudasi Avomereza Kupereka Yesu

14Pamenepo mmodzi wa khumi ndi awiriwo wotchedwa Yudasi Isikarioti anapita kwa akulu a ansembe 15nafunsa kuti, “Kodi mundipatsa chiyani ngati nditamupereka Iye kwa inu?” Pamenepo anamuwerengera ndalama zokwanira masiliva makumi atatu. 16Kuyambira pamenepo Yudasi anafunafuna nthawi yabwino yoti amupereke Yesu.

Paska Womaliza ndi Mgonero wa Ambuye

17Pa tsiku loyamba laphwando la buledi wopanda yisiti, ophunzira anabwera kwa Yesu ndi kumufunsa kuti, “Kodi mukufuna tikakonze kuti malo odyera Paska?”

18Iye anayankha kuti, “Pitani mu mzinda kwa munthu wakutiwakuti ndipo kamuwuzeni kuti, ‘Aphunzitsi akuti, nthawi yanga yoyikidwa yayandikira. Ine ndidzadya phwando la Paska ndi ophunzira anga ku nyumba kwako.’ ” 19Pamenepo ophunzira ake anachita monga momwe Yesu anawawuzira ndipo anakonza Paska.

20Kutada, Yesu ndi ophunzira ake khumi ndi awiriwo anakhala pa tebulo nʼkumadya. 21Akudya, Iye anati, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti mmodzi wa inu adzandipereka.”

22Iwo anamva chisoni kwambiri ndipo anayamba kuyankhulana naye mmodzimmodzi nati, “Kodi nʼkukhala ine Ambuye?”

23Yesu anayankha nati, “Iye amene akusunsa mʼmbale pamodzi ndi Ine, yemweyo adzandipereka. 24Mwana wa Munthu adzaphedwa monga mmene kunalembedwera za Iye. Koma tsoka kwa munthu amene apereka Mwana wa Munthu! Kukanakhala bwino kwa iye akanapanda kubadwa.”

25Ndipo Yudasi amene anamupereka Iye anati, “Monga nʼkukhala ine Aphunzitsi?”

Yesu anayankha nati, “Iwe watero.”

26Pamene ankadya, Yesu anatenga buledi, nayamika ndipo anamunyema nagawira ophunzira ake nanena kuti, “Tengani, idyani; ili ndi thupi langa.”

27Kenaka anatenga chikho, nayamika nachipereka kwa iwo nati, “Imwani nonsenu. 28Awa ndi magazi anga a pangano amene akhetsedwa chifukwa cha ambiri kuti akhululukidwe machimo. 29Ndikuwuzani kuti sindidzamwanso kuchokera ku chipatso cha mtengo wa mpesa kuyambira lero mpaka tsiku ilo pamene ndidzamwenso mwatsopano ndi inu mu ufumu wa Atate anga.”

30Atayimba nyimbo, anatuluka kupita ku phiri la Olivi.

Yesu Aneneratu kuti Petro Adzamukana

31Pamenepo Yesu anawawuza kuti, “Usiku omwe uno inu nonse mudzandithawa, pakuti kwalembedwa:

“ ‘Kantha mʼbusa,

ndipo nkhosa zidzabalalika.’

32Koma ndikadzauka, ndidzatsogola kupita ku Galileya.”

33Petro anayankha nati, “Ngakhale onsewa atakuthawani, ine ndekha ayi.”

34Yesu anayankha nati, “Zoonadi, ndikukuwuza kuti usiku omwe uno, asanalire tambala, udzandikana Ine katatu.”

35Koma Petro ananenetsa nati, “Ngakhale kutakhala kufa nanu pamodzi, sindidzakukanani.” Ndipo ophunzira onse ananena chimodzimodzi.

Yesu mu Getsemani

36Kenaka Yesu anapita ku malo otchedwa Getsemani, ndipo anawawuza kuti, “Khalani pano pamene Ine ndikukapemphera apo.” 37Anatenga Petro ndi ana awiri a Zebedayo, ndipo anayamba kumva chisoni ndi kuvutika mu mtima. 38Pamenepo anawawuza kuti, “Moyo wanga uli ndi chisoni chofa nacho. Khalani pano ndipo dikirani pamodzi ndi Ine.”

39Atapita patsogolo pangʼono, anagwa pansi chafufumimba napemphera kuti, “Atate anga, ngati ndikotheka, chikho ichi chichotsedwe kwa Ine. Koma osati monga mmene ndifunira, koma monga mufunira Inu.”

40Kenaka anabwera kwa ophunzira ake nawapeza ali mtulo. Iye anafunsa Petro kuti, “Kodi anthu inu, simukanakhala maso pamodzi ndi Ine kwa ora limodzi lokha? 41Khalani maso ndi kupemphera kuti musagwe mʼmayesero. Mzimu ukufuna koma thupi ndi lofowoka.”

42Anachokanso nakapemphera kachiwiri kuti, “Atate anga, ngati chikhochi sichingandichoke, mpaka nditamwa, kufuna kwanu kuchitike.”

43Atabweranso anawapeza ali mtulo chifukwa zikope zawo zinalemedwa ndi tulo. 44Choncho anawasiya napitanso kukapemphera kachitatu nanenanso chimodzimodzi.

45Kenaka anabwera kwa ophunzira ake nati kwa iwo, “Kodi mukanagonabe ndi kupumula? Taonani, ora layandikira ndipo Mwana wa Munthu akuperekedwa mʼmanja mwa ochimwa. 46Imirirani, tiyeni tizipita! Wondipereka Ine wafika!”

Amugwira Yesu

47Akuyankhula choncho, Yudasi mmodzi mwa khumi ndi awiriwo anafika. Pamodzi ndi iye panali gulu lalikulu la anthu ali ndi mikondo ndi zibonga otumidwa ndi akulu a ansembe ndi akuluakulu. 48Womuperekayo anawawuziratu chizindikiro anthuwo kuti, “Amene ndidzapsompsona ndi iyeyo; mugwireni.” 49Pamenepo Yudasi anapita kwa Yesu nati, “Moni, Aphunzitsi!” Ndipo anapsompsona Iye.

50Yesu anayankha kuti, “Bwenzi langa, chita chimene wabwerera.”

Pamenepo anthuwo anabwera patsogolo namugwira Yesu ndi kumumanga. 51Pa chifukwa ichi, mmodzi wa anzake a Yesu anagwira lupanga lake, nalisolola ndi kutema wantchito wa mkulu wa ansembe, nadula khutu lake.

52Yesu anati kwa iye, “Bwezera lupanga lako mʼchimake, chifukwa onse amene amapha ndi lupanga adzafa ndi lupanga. 53Kodi mukuganiza kuti sindingathe kupempha Atate anga ndipo nthawi yomweyo nʼkundipatsa magulu a angelo oposa khumi ndi awiri? 54Koma nanga malemba akwaniritsidwa bwanji amene akuti ziyenera kuchitika motere?”

55Pa nthawi yomweyo Yesu anati kwa gululo, “Kodi ndine mtsogoleri wa anthu owukira kuti mwabwera ndi malupanga ndi zibonga kudzandigwira? Tsiku ndi tsiku ndimakhala mʼNyumba ya Mulungu kuphunzitsa, koma simunandigwire. 56Koma zonsezi zachitika kuti zolembedwa ndi aneneri zikwaniritsidwe.” Pamenepo ophunzira anamusiya nathawa.

Yesu ku Bwalo la Akulu Ayuda

57Iwo amene anamugwira Yesu anamutengera kwa Kayafa, mkulu wa ansembe, kumene aphunzitsi amalamulo ndi akuluakulu anasonkhana. 58Koma Petro anamutsatira Iye patali, mpaka ku bwalo la mkulu wa ansembe. Analowa nakhala pansi pamodzi ndi alonda kuti aone zotsatira.

59Akulu a ansembe ndi akulu olamulira Ayuda amafunafuna umboni wonama wofuna kuphera Yesu. 60Koma sanathe kupeza uliwonse, angakhale kuti mboni zambiri zabodza zinapezeka.

Pomalizira mboni ziwiri zinabwera patsogolo. 61Ndipo zinati, “Munthu uyu anati, ‘Ndikhoza kupasula Nyumba ya Mulungu ndi kuyimanganso mʼmasiku atatu.’ ”

62Pamenepo mkulu wa ansembe anayimirira nati kwa Yesu, “Kodi suyankha? Kodi umboni umenewu ndi otani umene anthu awa akupereka kukutsutsa Iwe?” 63Koma Yesu anakhalabe chete.

Mkulu wa ansembe anati kwa Iye, “Ndikulamulira Iwe ndi lumbiro pamaso pa Mulungu wa Moyo: utiwuze ife ngati ndiwe Khristu Mwana wa Mulungu.”

64Yesu anayankha nati, “Mwanena ndinu. Koma ndikunena kwa inu nonse: mʼtsogolomo mudzaona Mwana wa Munthu atakhala kudzanja lamanja la Wamphamvuzonse ndipo akubwera ndi mitambo ya kumwamba.”

65Pamenepo mkulu wa ansembe anangʼamba zovala zake nati, “Wanyoza Mulungu! Tifuniranji mboni zina? Taonani, tsopano mwamva mwano wake. 66Mukuganiza bwanji?”

Iwo anayankha kuti, “Ayenera kuphedwa!”

67Kenaka anamulavulira kumaso namumenya ndi zibakera. Ena anamumenya makofi. 68Ndipo anati, “Tanenera kwa ife, Khristu. Wakumenya ndani?”

Petro Amukana Yesu

69Tsopano Petro anakhala ku bwalo la nyumbayo, ndipo mtsikana wantchito anabwera kwa iye nati, “Iwenso unali ndi Yesu wa ku Galileya.”

70Koma iye anakana pamaso pawo nati, “Sindikudziwa chimene ukunena.”

71Kenaka anachoka kupita ku khomo la mpanda, kumene mtsikana wina anamuonanso nawuza anthu nati, “Munthu uyu anali ndi Yesu wa ku Nazareti.”

72Iye anakananso molumbira kuti, “Sindimudziwa munthuyu!”

73Patapita kanthawi pangʼono, amene anayimirira pamenepo anapita kwa Petro nati, “Zoonadi, ndiwe mmodzi wa iwo, popeza mayankhulidwe ako akukuwulula.”

74Pamenepo anayamba kudzitemberera ndipo analumbira kwa iwo nati, “Sindimudziwa munthu ameneyo!”

Nthawi yomweyo tambala analira. 75Ndipo Petro anakumbukira mawu amene Yesu anayankhula kuti, “Tambala asanalire, udzandikana Ine katatu.” Ndipo anatuluka panja nakalira kwambiri.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Матто 26:1-75

Религиозные вожди замышляют убить Исо Масеха

(Мк. 14:1-2; Лк. 22:1-2; Ин. 11:45-53)

1Закончив говорить это, Исо сказал ученикам:

2– Вы знаете, что через два дня будет праздник Освобождения26:2 Праздник Освобождения – этот праздник отмечался в память об избавлении иудейского народа под руководством пророка Мусо из Египетского рабства (см. Исх. 12; 13:17-22; 14; Втор. 16:1-8)., и Ниспосланного как Человек отдадут на распятие.

3А во дворце верховного священнослужителя Каиафы26:3 Каиафа был верховным священнослужителем с 18 по 36 гг. в это время собрались главные священнослужители и старейшины народа. 4Они решили хитростью схватить Исо и убить.

5– Только не во время праздника, – говорили они, – иначе народ может взбунтоваться.

Помазание Исо Масеха дорогим ароматическим маслом

(Мк. 14:3-9; Лк. 7:37-38; Ин. 12:1-8)

6Исо находился в Вифании, в доме Шимона прокажённого26:6 Скорее всего, Шимон когда-то страдал от кожного заболевания и исцелился (ср. Лев. 13:45-46; Чис. 5:2), но прозвище «прокажённый» за ним осталось.. 7И когда Он возлежал за столом, к Нему подошла женщина с алебастровым кувшином, в котором было очень дорогое ароматическое масло, и возлила это масло Ему на голову. 8Увидев это, ученики рассердились:

– Зачем такая трата? 9Ведь это ароматическое масло можно было продать за большую сумму, а деньги раздать нищим.

10Но Исо, зная, что они говорят, сказал им:

– Что вы упрекаете женщину? Ведь она сделала для Меня доброе дело. 11Потому что нищие всегда с вами, а Я не всегда буду с вами. 12Вылив на Меня это масло, она тем самым приготовила Меня к погребению. 13Говорю вам истину: во всём мире, везде, где будет возвещена эта Радостная Весть, будут вспоминать об этой женщине и о том, что она сделала.

Иуда Искариот решает предать Исо Масеха

(Мк. 14:10-11; Лк. 22:3-6)

14Затем Иуда Искариот, один из двенадцати учеников, пошёл к главным священнослужителям 15с предложением.

– Что вы мне дадите, если я предам вам Исо? – спросил он их. Те отсчитали ему тридцать серебряных монет26:15 См. Зак. 11:12. Здесь, по всей вероятности, говорится о тетрадрахмах – древнегреческих монетах, каждая из которых равнялась заработку 4 дней наёмного работника.. 16И с того момента Иуда стал искать удобного случая, чтобы предать Исо.

Приготовление учеников к празднику Освобождения

(Мк. 14:12-16; Лк. 22:7-13)

17В первый день праздника Пресных хлебов26:17 Праздник Пресных хлебов – в этот праздник, длившийся семь дней, предписывалось есть только пресный хлеб (см. Исх. 12:15-20; 13:3-10; Лев. 23:6-8; Чис. 28:17-25). Часто, когда говорили о празднике Пресных хлебов, имели в виду и сам этот праздник, и предшествующий ему праздник Освобождения (и наоборот). ученики спросили Исо:

– Где нам приготовить Тебе праздничный ужин?

18Исо ответил:

– Идите в город к такому-то и скажите ему: «Учитель говорит, что Его время уже подошло, и Он хочет в твоём доме отметить праздник Освобождения со Своими учениками».

19Ученики сделали всё, как им велел Исо, и приготовили праздничный ужин.

Последний ужин с учениками

(Мк. 14:17-25; Лк. 22:17-23; 1 Кор. 11:23-25)

20Вечером Исо со Своими двенадцатью учениками возлёг у стола. 21Когда они ели, Исо сказал:

– Говорю вам истину: один из вас предаст Меня.

22Ученики сильно опечалились и один за другим стали спрашивать Его:

– Но ведь это же не я, Повелитель?

23А Исо сказал:

– Меня предаст тот, кто опустил руку в блюдо вместе со Мной. 24Да, Ниспосланный как Человек уходит так, как о Нём сказано в Писании, но горе тому человеку, который предаёт Его! Лучше бы ему вообще не родиться.

25Тогда Иуда, предатель, тоже спросил:

– Но ведь это же не я, Учитель?

– Это ты так говоришь, – ответил Исо.

26Когда они ели, Исо взял хлеб и, благословив, разломил его, дал Своим ученикам и сказал:

– Возьмите и ешьте, это Моё тело.

27Затем Он взял чашу, поблагодарил за неё Всевышнего и подал им со словами:

– Пейте из неё все. 28Это Моя кровь священного соглашения26:28 Ср. Исх. 24:8; Евр. 9:18-20., проливаемая за многих людей для прощения грехов. 29Говорю вам, что Я уже не буду пить от плода виноградного до того дня, когда Я буду пить с вами новое26:29 Или: «снова». вино в Царстве Моего Отца.

Предсказание об отречении Петруса

(Мк. 14:26-31; Лк. 22:33-34; Ин. 13:37-38)

30Они спели песни из Забура26:30 Традиционно на этом празднике иудеи пели песни из Забура со 112 по 117 и 135. и пошли на Оливковую гору.

31Тогда Исо сказал им:

– В эту ночь вы все отступитесь от Меня, ведь написано:

«Я поражу пастуха,

и разбегутся овцы стада»26:31 Зак. 13:7..

32Но когда Я воскресну, то пойду в Галилею и буду ждать вас там.

33Петрус ответил:

– Даже если все Тебя оставят, я этого никогда не сделаю.

34– Говорю тебе истину, – сказал ему Исо, – в эту ночь, прежде чем пропоёт петух, ты трижды отречёшься от Меня.

35Но Петрус уверял:

– Даже если мне придётся умереть с Тобой, я никогда не откажусь от Тебя.

То же самое говорили и все ученики.

Молитва в Гефсиманском саду

(Мк. 14:32-42; Лк. 22:39-46)

36Исо пришёл с ними на место, называемое Гефсимания, и сказал ученикам:

– Посидите здесь, а Я пойду и помолюсь.

37Он взял с Собой Петруса и двух сыновей Завдая. Его охватили тоска и тревога. 38Тогда Он сказал им:

– Душа Моя объята смертельной печалью. Побудьте здесь и бодрствуйте со Мной.

39Отойдя немного, Он пал на лицо Своё и молился:

– Отец Мой, если возможно, то пусть минует Меня эта чаша страданий, но да будет всё не как Я хочу, а как Ты хочешь.

40Затем Он возвратился к ученикам и нашёл их спящими.

– Неужели вы даже часу не могли пободрствовать вместе со Мной? – спросил Он Петруса. – 41Бодрствуйте и молитесь, чтобы вам не поддаться искушению. Дух бодр, но тело слабо.

42И во второй раз Он снова ушёл и молился:

– Отец Мой, если невозможно, чтобы эта чаша страданий миновала Меня и чтобы Мне не пить из неё, то пусть всё будет по Твоей воле.

43Когда Он вернулся, ученики опять спали, потому что их веки отяжелели. 44И оставив их, Исо отошёл и стал молиться в третий раз теми же словами. 45Затем Исо возвратился к ученикам и сказал им:

– Вы всё спите и отдыхаете? Вот время настало, и Ниспосланный как Человек предаётся в руки грешников. 46Вставайте, идём. Вот уже и Мой предатель приблизился.

Исо Масех предан и арестован

(Мк. 14:43-50; Лк. 22:47-53; Ин. 18:3-11)

47Он ещё говорил, как подошёл Иуда, один из двенадцати учеников, и с ним большая толпа, вооружённая мечами и кольями. Их послали главные священнослужители и старейшины народа. 48Предатель так условился с ними:

– Хватайте Того, Кого я поцелую.

49Иуда сразу же подошёл к Исо и сказал:

– Здравствуй, Учитель! – и поцеловал Его.

50Исо же сказал ему:

– Друг, делай то, для чего пришёл.

Тут подошли люди и, схватив Исо, взяли Его под стражу. 51Тогда один из тех, кто был с Исо, вытащил меч, ударил раба главного священнослужителя и отсёк ему ухо.

52– Верни свой меч на место, – сказал ему Исо. – Все, кто берётся за меч, от меча и погибнут. 53Неужели ты думаешь, что Я не мог бы упросить Моего Отца немедленно прислать Мне более двенадцати ангельских воинств?26:53 Букв.: «более двенадцати легионов». Легион – воинское соединение в римской армии численностью до 6 000 солдат. 54Но как же тогда исполнится Писание, что всё это должно произойти?

55Затем Исо обратился к толпе:

– Что Я, разбойник, что вы пришли с мечами и кольями, чтобы арестовать Меня? Каждый день Я сидел и учил в храме, и вы не арестовывали Меня. 56Но всё произошло именно так, чтобы исполнились писания пророков.

Тогда все ученики оставили Его и убежали.

На допросе у верховного священнослужителя Каиафы

(Мк. 14:53-65; Лк. 22:54-55, 63-71; Ин. 18:12-13, 19-24)

57Арестовавшие Исо привели Его к верховному священнослужителю Каиафе, у которого уже собрались учители Таврота и старейшины. 58Петрус следовал за Исо на некотором расстоянии до двора верховного священнослужителя. Войдя внутрь, он сел со стражниками, чтобы увидеть, чем всё кончится. 59Главные священнослужители и весь Высший Совет26:59 Высший Совет (букв.: «синедрион») – высший политический, религиозный и судебный орган иудеев. В состав Совета входил семьдесят один человек. искали ложных показаний против Исо, чтобы приговорить Его к смерти. 60Но они ничего не могли найти, хотя и пришло много лжесвидетелей. Наконец вышли два человека 61и заявили:

– Этот Человек говорил: «Я могу разрушить храм Всевышнего и восстановить его за три дня».

62Тогда верховный священнослужитель встал и спросил Исо:

– Тебе нечего ответить на эти свидетельства против Тебя?

63Исо молчал. Верховный священнослужитель сказал Ему:

– Я заклинаю Тебя живым Богом, если Ты обещанный Масех, Сын Всевышнего, то скажи нам.

64– Ты сам так сказал, – ответил Исо, – но говорю вам, что отныне вы увидите Ниспосланного как Человек сидящим по правую руку от могучего Бога и идущим на облаках небесных!26:64 См. Заб. 109:1; Дон. 7:13.

65Тогда верховный священнослужитель в негодовании разорвал на себе одежду и сказал:

– Он кощунствует! Какие нам ещё нужны свидетели?! Вы теперь сами слышали Его кощунство! 66Каково ваше решение?

Они ответили:

– Он виновен и заслуживает смерти.

67Тогда Исо стали плевать в лицо и бить Его кулаками, некоторые же били Его по щекам и 68спрашивали:

– Эй Ты, Масех! Если Ты пророк, то скажи нам, кто Тебя ударил?

Отречение Петруса

(Мк. 14:66-72; Лк. 22:54-62; Ин. 18:16-18, 25-27)

69Петрус же сидел снаружи, во дворе, когда к нему подошла служанка.

– Ты тоже был с Исо Галилеянином, – сказала она.

70Но Петрус отрицал перед всеми:

– Я не знаю, о чём ты говоришь.

71Когда он отошёл к воротам, его увидела другая служанка. Она сказала стоявшим рядом:

– Этот человек был с Исо Назарянином.

72Петрус снова всё отрицал, поклявшись, что он не знает Этого Человека. 73Но спустя немного времени стоявшие там люди подошли и сказали ему:

– Точно, ты тоже один из них, тебя и говор твой выдаёт.

74Тогда Петрус начал клясться, призывая на себя проклятия:

– Я не знаю Этого Человека!

И тотчас пропел петух. 75И тогда Петрус вспомнил слова Исо: «Прежде чем пропоёт петух, ты трижды отречёшься от Меня».

И выйдя наружу, он горько заплакал.