Mateyu 25 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 25:1-46

Fanizo la Anamwali Khumi

1“Nthawi imeneyo ufumu wakumwamba udzafanizidwa ndi anamwali khumi amene anatenga nyale zawo napita kukakumana ndi mkwati. 2Asanu anali opusa ndipo asanu ena anali ochenjera. 3Opusawo anatenga nyale zawo koma sanatenge mafuta; 4koma ochenjerawo anatenga mafuta awo mʼmabotolo pamodzi ndi nyale zawo. 5Mkwati anachedwa ndipo onse anayamba kusinza nagona.

6“Pakati pa usiku kunamveka kufuwula kuti, ‘Onani Mkwati! Tulukani kuti mukakumane naye!’

7“Pamenepo anamwali onse anadzuka nayatsa nyale zawo. 8Opusawo anati kwa ochenjerawo, ‘Tipatseniko mafuta anu; nyale zathu zikuzima.

9“Ochenjerawo anayankha, nati, ‘Ayi sangakwanire inu ndi ife. Pitani kwa ogulitsa mafuta ndi kukadzigulira nokha.’

10“Koma pamene ankapita kukagula mafutawo, mkwati anafika. Anamwali amene anali okonzeka aja analowa naye pamodzi mʼnyumba ya phwando la ukwati. Ndipo khomo linatsekedwa.

11“Pambuyo pake enawo anabwera nati, ‘Ambuye! Ambuye! Titsekulireni!’

12“Koma iye anayankha kuti, ‘Zoonadi, ine ndikuwuzani kuti sindikukudziwani.’

13“Choncho khalani odikira, popeza simudziwa tsiku kapena nthawi.”

Fanizo la Kagwiritsidwe Ntchito ka Ndalama

14“Komanso udzafanizidwa ndi munthu amene ankapita pa ulendo, ndipo anayitana antchito ake nawasiyira chuma chake. 15Wina anamupatsa ndalama 5,000, kwa wina 2,000 ndi kwa wina 1,000. Aliyense monga mwa nzeru zake. Pamenepo anapita pa ulendo wake. 16Munthu amene analandira ndalama 5,000 uja, anapita nthawi yomweyo nachita nazo malonda napindula 5,000 zina. 17Chimodzimodzinso amene analandira 2,000 uja anapindula 2,000 zina. 18Koma munthu amene analandira 1,000 uja, anapita nakumba dzenje nabisapo ndalama ya mbuye wake.

19“Patapita nthawi yayitali, mbuye wa antchitowo anabwera nawayitana kuti afotokoze chimene anachita ndi ndalama zija. 20Munthu amene analandira ndalama 5,000 uja anabweretsa 5,000 zina nati, ‘Ambuye munandisungitsa 5,000, taonani ndapindula 5,000 zinanso.’

21“Ambuye ake anayankha nati, ‘Wachita bwino, wantchito wabwino ndi wokhulupirika iwe! Wakhala wokhulupirika pa zinthu zochepa; ndidzakuyika iwe kukhala woyangʼanira zinthu zambiri. Bwera, udzakondwere pamodzi ndi mbuye wako!’

22“Munthu amene anali ndi ndalama 2,000 uja anabweranso nati, ‘Ambuye munandisungitsa 2,000, onani, ndapindula 2,000 zinanso.’

23“Mbuye wake anayankha nati, ‘Wachita bwino, wantchito wabwino ndi wokhulupirika! Wakhala wokhulupirika pa zinthu zochepa; ndidzakuyika kukhala woyangʼanira zinthu zambiri. Bwera, udzakondwere pamodzi ndi mbuye wako!’

24“Kenaka munthu amene analandira ndalama 1,000 uja anabwera nati, ‘Ambuye ndinadziwa kuti ndinu munthu wowuma mtima, amene mumakolola pamene simunadzale ndi kututa kumene simunafese. 25Choncho ndinachita mantha ndipo ndinapita ndi kukabisa ndalama yanuyo pa dzenje. Onani, si iyi ndalama yanu ija.’

26“Mbuye wake anayankha nati, ‘Iwe wantchito woyipa ndi waulesi! Iwe umadziwa kuti ndimakolola pamene sindinadzale, ndi kututa kumene sindinafese. 27Bwanji sunayike ndalama yanga kwa osunga ndalama kuti ine pobwera ndidzalandire ndalama yangayo pamodzi ndi chiwongoladzanja?

28“ ‘Mulandeni ndalamayo, ndipo patsani iye amene ali ndi ndalama 10,000. 29Pakuti aliyense amene ali nazo adzapatsidwa zambiri, ndipo adzakhala nazo zochuluka. Aliyense amene alibe adzalandidwa ngakhale chimene ali nacho. 30Ndipo muponyeni wantchito wopanda phinduyu kunja, ku mdima kumene kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.’ ”

Nkhosa ndi Mbuzi

31“Pamene Mwana wa Munthu adzabwera mu ulemerero wake, pamodzi ndi angelo ake onse, adzakhala pa mpando waufumu mu ulemerero wakumwamba. 32Mitundu yonse ya anthu idzasonkhanitsidwa pamaso pake, ndipo adzawalekanitsa iwo wina ndi mnzake monga mʼbusa amalekanitsa nkhosa ndi mbuzi. 33Adzayika nkhosa ku dzanja lake lamanja ndi mbuzi ku lamanzere.

34“Pamenepo mfumu idzati kwa a ku dzanja lamanja, ‘Bwerani inu odalitsika ndi Atate anga; landirani ufumu umene unakonzedwa chifukwa cha inu kuyambira pachiyambi cha dziko. 35Pakuti ndinali ndi njala ndipo munandipatsa chakudya, ndinali ndi ludzu ndipo munandipatsa madzi akumwa, ndinali mlendo ndipo munandilandira, 36ndinali wausiwa ndipo munandiveka, ndinali wodwala ndipo munandisamalira, ndinali ku ndende ndipo inu munandiyendera.’

37“Ndipo olungamawo adzamuyankha kuti, ‘Ambuye ndi liti tinakuonani muli ndi njala ndipo tinakudyetsani, kapena ludzu ndipo tinakupatsani madzi akumwa? 38Ndi liti tinakuonani muli mlendo ndipo tinakulandirani, kapena wa usiwa ndipo tinakuvekani? 39Ndi liti tinakuonani mutadwala kapena ku ndende ndipo tinakuyenderani?’

40“Mfumu idzayankha kuti, ‘Zoonadi, ndikuwuzani kuti chilichonse chimene munachitira mmodzi wa abale anga onyozekawa munandichitira Ine.’

41“Pamenepo adzanena kwa akumanzere kwake kuti, ‘Chokani kwa Ine, inu otembereredwa, pitani ku moto wosatha wokonzedwera mdierekezi ndi angelo ake. 42Pakuti ndinali ndi njala ndipo simunandipatse chakudya, ndinali ndi ludzu ndipo simunandipatse madzi akumwa, 43ndinali mlendo koma inu simunandilandire, ndinali wa usiwa koma simunandiveke, ndinali wodwala komanso ku ndende simunandisamalire.’

44“Iwo adzayankha kuti, ‘Ambuye ndi liti tinakuonani muli ndi njala kapena ludzu kapena mlendo kapena wausiwa kapena wodwala kapena mʼndende, ndipo kuti sitinakuthandizeni?’

45“Iye adzayankha kuti, ‘Zoonadi, ndikuwuzani kuti chilichonse chimene simunachitire mmodzi wa abale anga onyozekawa simunandichitire Ine.’

46“Amenewa adzapita ku chilango chosatha pamene olungama ku moyo wosatha.”

New Russian Translation

Матфея 25:1-46

Притча о десяти девушках

1Тогда Небесное Царство будет подобно десяти девушкам, которые, взяв свои лампы, вышли встречать жениха. 2Пять из них были глупыми, а другие пять умными. 3Глупые девушки взяли лампы, но не взяли для них масла. 4А умные вместе с лампами взяли и масло в кувшинах. 5Жених задержался, и они все стали дремать и заснули. 6Около полуночи раздался крик: «Жених идет! Выходите встречать его!» 7Девушки проснулись и стали поправлять свои лампы. 8Глупые сказали умным: «Дайте нам немного масла, наши лампы гаснут». 9«Нет, – ответили те, – если мы поделимся с вами маслом, то не хватит ни вам, ни нам. Пойдите лучше к торговцам и купите». 10Только они ушли за маслом, пришел жених. Девушки с зажженными лампами вошли с ним на свадебный пир, и дверь за ними закрылась. 11Позже вернулись и остальные девушки и стали просить: «Господин! Господин! Открой нам!» 12Но жених ответил: «Говорю вам истину: я не знаю вас». 13Поэтому бодрствуйте: ведь вы не знаете ни дня, ни часа, в который придет Сын Человеческий25:13 В древнейших рукописях отсутствуют слова: «в который придет Сын Человеческий»..

Притча о порученных деньгах

(Лк. 19:12-27)

14Тогда будет, как у того человека, который, отправляясь в далекое путешествие, созвал своих слуг и поручил им свое имущество. 15Одному он дал пять талантов, другому – два, третьему один, каждому по его способностям, а сам уехал. 16Получивший пять талантов сразу пошел, вложил деньги в дело и приобрел еще пять. 17Получивший два таланта тоже приобрел еще два. 18А тот, который получил один талант, пошел, вырыл яму и закопал деньги, которые ему доверил хозяин.

19Прошло много времени, и вот хозяин этих слуг вернулся и потребовал у них отчета. 20Человек, которому было доверено пять талантов, принес и другие пять: «Смотри, – сказал он хозяину, – ты доверил мне пять талантов, и я выручил еще пять!» 21Хозяин сказал: «Молодец! Ты хороший и верный слуга! Ты был верен в малом, и я поручу тебе более важное дело. Заходи и веселись со своим хозяином!»

22Пришел и человек с двумя талантами. «Хозяин, – сказал он, – ты доверил мне два таланта, смотри, я выручил еще два!» 23Хозяин сказал: «Молодец! Ты хороший и верный слуга! Ты был верен мне в малом, и я смогу поручить тебе более важное дело. Заходи и веселись со своим хозяином!»

24Затем пришел и тот, кому был доверен один талант. «Господин, – говорит он, – я знал, что ты человек суровый, жнешь там, где не сеял, и собираешь там, где не рассыпал. 25Я очень боялся и поэтому пошел и спрятал твой талант в землю. Вот то, что тебе принадлежит». 26Хозяин же ответил: «Злой и ленивый слуга! Значит, ты знал, что я жну, где не сеял, и собираю, где не рассыпал? 27В таком случае ты должен был пустить мои деньги в оборот, чтобы, когда я вернусь, ты мог отдать их мне с прибылью. 28Заберите у него этот талант и отдайте тому, у кого десять талантов. 29Потому что каждому, у кого есть, будет дано еще, и у него будет избыток. А у кого нет, будет отнято и то, что он имеет. 30Выбросьте этого негодного слугу вон, во тьму, где будет плач и скрежет зубов».

Козлы и овцы

31Когда Сын Человеческий придет в Своей славе и с Ним все ангелы, тогда Он сядет на престоле Своей славы. 32Перед Ним будут собраны все народы, и Он отделит одних людей от других, как пастух отделяет овец от козлов. 33Овец Он соберет по правую сторону от Себя, а козлов – по левую.

34Тогда Царь скажет тем, кто по правую сторону: «Придите ко Мне, благословенные Моим Отцом, получите ваше наследство – Царство, приготовленное вам еще от создания мира. 35Потому что Я был голоден, и вы накормили Меня; Я хотел пить, и вы напоили Меня; Я был странником, и вы приютили Меня. 36Я был наг, и вы одели Меня; Я был болен, и вы ухаживали за Мной; Я был в темнице, и вы пришли навестить Меня». 37Тогда праведные скажут: «Господи, когда это мы видели Тебя голодным и накормили Тебя? Когда Ты хотел пить, и мы дали Тебе напиться? 38Когда мы видели Тебя странником и приютили Тебя, или видели нагим и одели? 39Когда мы видели Тебя больным или в темнице и навестили Тебя?» 40Царь им ответит: «Говорю вам истину: то, что вы сделали одному из наименьших Моих братьев, вы сделали Мне».

41Тогда Он скажет и тем, кто будет по левую сторону: «Идите от Меня, проклятые, в вечный огонь, приготовленный для дьявола и его ангелов. 42Потому что Я был голоден, и вы не накормили Меня; Я хотел пить, и вы не напоили Меня; 43Я был странником, и вы не приютили Меня; Я был наг, и вы не одели Меня; Я был болен и в темнице, и вы не навестили Меня». 44Они тоже спросят: «Господи, когда это мы видели Тебя голодным, или когда Ты хотел пить, или был странником, или нуждался в одежде, или был болен, или в темнице, и мы не помогли Тебе?» 45Он им ответит: «Говорю вам истину: все, чего вы не сделали для одного из наименьших, вы не сделали Мне».

46И они пойдут в вечное наказание, а праведники – в вечную жизнь.