Mateyu 23 – CCL & HHH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 23:1-39

Yesu Adzudzula Aphunzitsi Amalamulo ndi Afarisi

1Pamenepo Yesu anati kwa magulu a anthu ndi ophunzira ake: 2“Aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi amakhala pa mpando wa Mose. 3Choncho muziwamvera ndi kuchita chilichonse chimene akuwuzani. Koma musachite zimene amachita, popeza sachita zimene amaphunzitsa. 4Amamanga akatundu olemera nawayika pa mapewa a anthu, koma iwo eni safuna kuwanyamula.

5“Ntchito zawo amachita ndi cholinga chakuti anthu awaone. Amadzimangirira timaphukusi tikulutikulu ta Mawu a Mulungu pa mphumi ndi pa mkono komanso amatalikitsa mphonje za mikanjo yawo. 6Amakonda malo aulemu pa maphwando ndi malo ofunika kwambiri mʼmasunagoge. 7Amakondwera ndi kupatsidwa moni mʼmisika ndi kutchulidwa kuti ‘Aphunzitsi.’

8“Koma inu simuyenera kutchulidwa ‘Aphunzitsi,’ popeza muli naye Mbuye mmodzi ndipo inu nonse ndinu abale. 9Ndipo musamatchule wina aliyense pansi pano kuti ‘Atate,’ pakuti muli ndi Atate mmodzi, ndipo ali kumwamba. 10Komanso musamatchedwenso ‘Mtsogoleri,’ pakuti muli naye Mtsogoleri mmodzi amene ndi Khristu. 11Wamkulu pakati panu adzakhala wokutumikirani. 12Pakuti aliyense amene adzikuza adzachepetsedwa, ndipo aliyense amene adzichepetsa adzakuzidwa.

Tsoka kwa Aphunzitsi Amalamulo ndi Afarisi

13“Tsoka kwa inu aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi achiphamaso! Mumatseka pa khomo la kumwamba kuti anthu asalowemo. Eni akenu simulowamo komanso simulola kuti ena amene akufuna kulowa kuti alowe. 14Muli ndi tsoka, inu aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, anthu achiphamaso! Mumawadyera akazi amasiye chuma chawo, kwinaku nʼkumanamizira kunena mapemphero ataliatali. Chifukwa cha zimenezi Mulungu adzakulangani koposa.

15“Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Mumayenda maulendo ambiri pa mtunda ndi pa nyanja kuti mutembenuze munthu mmodzi, ndipo akatembenuka, mumamusandutsa kukhala mwana wa gehena kawiri kuposa inu.

16“Tsoka kwa inu, atsogoleri akhungu! Mumati, ‘Ngati wina alumbira kutchula Nyumba ya Mulungu, zilibe kanthu; koma ngati wina alumbira kutchula ndalama zagolide za mʼNyumbayo, wotere ayenera kusunga lumbiro lake.’ 17Inu akhungu opusa! Chopambana nʼchiyani: ndalama zagolide, kapena Nyumba imene imayeretsa golideyo? 18Ndiponso mumati, ‘Ngati wina alumbira kutchula guwa lansembe, sizitanthauza kanthu; koma ngati wina alumbira kutchula mphatso ya paguwa lansembe, wotere ayenera kusunga lumbiro lake.’ 19Inu anthu akhungu! Chopambana nʼchiyani: mphatso, kapena guwa limene limayeretsa mphatsoyo? 20Chifukwa chake, iye amene alumbira kutchula guwa alumbira pa ilo ndi pa chilichonse chili pamenepo. 21Ndipo iye wolumbira potchula Nyumba ya Mulungu alumbira pa Nyumbayo ndi pa Iye amene amakhala mʼmenemo. 22Ndipo iye wolumbira kutchula kumwamba alumbira kutchula mpando waufumu wa Mulungu ndi pa Iye wokhalapo.

23“Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Mumapereka chakhumi cha timbewu tonunkhira ndi cha timbewu tokometsera chakudya. Koma mwasiya zofunikira kwambiri za mʼmalamulo monga chilungamo, chifundo ndi kukhulupirika. Muyenera kuchita zomalizirazi komanso osasiya zoyambazo. 24Atsogoleri akhungu inu! Mumachotsa kantchentche mu chakumwa chanu koma mumameza ngamira.

25“Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi achiphamaso! Mumayeretsa kunja kwa chikho ndi mbale, koma mʼkatimo mwadzaza ndi dyera ndi kusadziretsa. 26Afarisi akhungu! Poyamba tsukani mʼkati mwa chikho ndi mbale, ndipo kunja kwake kudzakhalanso koyera.

27“Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Muli ngati ziliza pa manda zowala kunja zimene zimaoneka zokongola koma mʼkatimo mwadzaza mafupa a anthu akufa ndi zonyansa zina zonse. 28Chimodzimodzinso, kunja mumaoneka kwa anthu kuti ndinu olungama koma mʼkatimo ndinu odzaza ndi chinyengo ndi zoyipa zina.

29“Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Mumamanga ziliza za aneneri ndi kukongoletsa manda a olungama. 30Ndipo mumati, ‘Ngati tikanakhala mʼmasiku a makolo athu sitikanakhetsa nawo magazi a aneneri.’ 31Potero mukutsimikiza kuti muli ana a iwo amene anapha aneneri. 32Dzazani inu muyeso wa uchimo wa makolo anu!

33“Njoka inu! Ana amamba! Mudzachithawa bwanji chilango cha gehena? 34Choncho ndi kutumizirani aneneri ndi anthu anzeru ndi aphunzitsi. Ena a iwo mudzawapha ndi kuwapachika; ena mudzawakwapula mʼmasunagoge anu ndi kuwafunafuna kuchokera mudzi wina kufikira wina. 35Ndipo magazi onse a olungama amene anakhetsedwa pansi pano, kuyambira magazi a Abele, olungama kufikira Zakariya mwana wa Barakiya, amene munamupha pakati pa Nyumba ya Mulungu ndi guwa lansembe, adzakhala pa inu. 36Zoonadi, ndikuwuzani kuti zonsezi zidzafika pa mʼbado uno.

37“Haa! Yerusalemu, Yerusalemu, iwe amene umapha aneneri ndi kugenda miyala amene atumidwa kwa iwe, kawirikawiri ndimafuna kusonkhanitsa ana ako, monga nkhuku imasonkhanitsira ana ake pansi pa mapiko ake, koma iwe sunafune. 38Taona, nyumba yako yasiyidwa ya bwinja. 39Chifukwa chake ndikuwuza kuti simudzandionanso kufikira pamene mudzati, ‘Wodala Iye amene akudza mʼdzina la Ambuye.’ ”

Habrit Hakhadasha/Haderekh

הבשורה על-פי מתי 23:1-39

1ישוע פנה אל הקהל ואל תלמידיו ואמר: 2”הסופרים והפרושים יושבים על כסא משה. 3לכן טוב שתשמעו בקולם ותעשו את מה שהם אומרים, אבל בשום אופן אל תעשו את מה שהם עושים! כי הם עצמם אינם עושים את מה שהם דורשים מכם לעשות. 4הם מכבידים עליכם בדרישות שונות, בעוד שבעצמם לא מוכנים להרים אצבע.

5”הם עושים את כל מעשיהם בשביל שיראו אותם. הם מעמידים פני צדיקים, מניחים תפילין בציבור ומאריכים את הציציות שלהם. 6במסיבות הם אוהבים לשבת בראש השולחן, ובבית הכנסת – במקומות השמורים. 7הם אוהבים שנותנים להם כבוד ברחובות ושקוראים להם ’רבי‘. 8אל תרשו לאיש לקרוא לכם כך, כי ה׳ לבדו הוא רבכם, וכולכם שווים כאחים. 9כמו כן אל תפנו לאיש בתואר ’אבי‘, כי רק לאלוהים שבשמים עליכם לקרוא ’אבי‘. 10אל תרשו שיקראו לכם ’מורי ורבי‘, כי יש לכם מורה ורב אחד בלבד, והוא המשיח.

11”ככל שתרבו לשרת את הזולת בענווה, כך תגדלו בעצמכם. כדי להיות גדולים ביותר – היו עבדים! 12מי שמכבד את עצמו יושפל ומי שמשפיל את עצמו יכובד.

13‏-14”אוי לכם, הפרושים והסופרים, צבועים אתם! לא די שאינכם נכנסים בעצמכם למלכות השמים, אתם גם מונעים מאחרים להיכנס! אתם מעמידים פני צדיקים ומתפללים באריכות באמצע הרחוב, וכל זאת בזמן שאתם מגרשים אלמנות מבתיהן. צבועים שכמוכם! 15כן, אוי לכם, צבועים! אתם נוסעים למרחקים כדי לגייר אדם אחד, ולאחר שהתגייר אתם הופכים אותו לבן־גיהינום עוד יותר מכם!

16”אוי לכם, מנהיגים עיוורים! הכלל שלכם הוא: ’אם נשבעת במקדש ה׳ מותר לך להפר את שבועתך, אולם אם נשבעת בזהב של בית־המקדש אסור לך להפר את שבועתך‘. 17עיוורים טיפשים! מה חשוב יותר, הזהב או המקדש שמקדש את הזהב?

18”כמו כן אתם אומרים: ’שבועה במזבח אינה מחייבת ומותר להפר אותה, אך שבועה בקורבן שעל המזבח – מחייבת‘. 19עיוורים! מה גדול וחשוב יותר, הקורבן שעל המזבח או המזבח עצמו המקדש את הקורבן? 20הרי אם אתם נשבעים ’במזבח‘, אתם נשבעים למעשה בו ובכל אשר עליו. 21כאשר אתם נשבעים ’במקדש‘, אתם נשבעים למעשה בו ובאלוהים השוכן בו. 22ואם אתם נשבעים ’בשמים‘, אתם נשבעים בכסא אלוהים ובאלוהים עצמו.

23”כן, אוי לכם פרושים וסופרים צבועים! אתם מקפידים על הלכות דקדקניות כמו לתת מעשר על עלי נענע בגינה, אולם אתם מתעלמים מהדברים החשובים באמת כמו צדק, רחמים ואמונה! אתם אמנם חייבים לתת מעשר, אולם אסור לכם להזניח את הדברים החשובים יותר. 24מנהיגים עיוורים! אתם מסננים את היתוש ובולעים את הגמל!

25”אוי לכם, סופרים ופרושים צבועים שכמוכם! אתם מקפידים כל־כך על צחצוח הכוס מבחוץ, אולם תוכה מצחין מריקבון! 26פרושים עיוורים, טהרו תחילה את פנים הכלי ואז כולו יהיה נקי!

27”אוי לכם, סופרים ופרושים! אתם דומים לקברים הנראים יפים ומפוארים מבחוץ, אך בתוכם הם מלאים עצמות מתים, ריקבון וטומאה. 28אתם משתדלים להיראות קדושים, אולם בפנים לבכם מלא צביעות וטומאה. 29‏-30כן, אוי לכם פרושים, ואוי לכם סופרים – צבועים שכמוכם! אתם בונים מצבות לנביאים שאבותיכם הרגו, ומניחים פרחים על קברי אנשי־האלוהים שאבותיכם רצחו, ואתם אומרים: ’אנחנו, כמובן, לא היינו מעזים לנהוג כפי שנהגו אבותינו!‘

31”בדבריכם אלה אתם מעידים על עצמכם שהנכם בני רשעים. 32אתם הולכים בעקבות אבותיכם וממלאים את מכסת עוונותיהם. 33נחשים בני נחשים! כיצד תימלטו מעונש הגיהינום?

34”אני שולח אליכם נביאים, חכמים וסופרים; אחדים מהם תהרגו בצליבה, ואחרים תלקו בשוטים בבתי הכנסת שלכם, ותרדפו אחריהם מעיר לעיר! 35וכך תישאו באשמת הריגתם של כל אנשי האלוהים – החל בהבל הצדיק וכלה בזכריה בן־ברכיה, שאותו רצחתם בבית־המקדש בין ההיכל למזבח. 36ובכן, כל זה יבוא על הדור הזה.

37”ירושלים, ירושלים, ההורגת את הנביאים ורוגמת באבנים את שליחי אלוהים! פעמים רבות חפצתי לאסוף את בנייך, כתרנגולת האוספת את אפרוחיה תחת כנפיה, אולם לא רציתם. 38ועתה אלוהים נוטש את ביתכם, 39ואני אומר לכם שמעתה ואילך לא תראו אותי יותר, עד אשר תאמרו: ’ברוך הבא בשם ה׳!‘ “