Mateyu 22 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 22:1-46

Fanizo la Phwando la Ukwati

1Yesu anayankhula nawonso mʼmafanizo, nati, 2“Ufumu wakumwamba uli ngati mfumu imene inakonzera phwando mwana wake wamwamuna. 3Anatumiza antchito ake kwa amene anayitanidwa kuphwando koma anakana kubwera.

4“Kenaka anatumiza antchito ena nati, ‘Awuzeni oyitanidwa kuti phwando lakonzedwa: ndapha ngʼombe yayimuna ndi nyama zina zonenepa ndipo zonse zakonzedwa. Bwerani ku phwando laukwati.’

5“Koma iwo sanalabadire ndipo anachoka; wina anapita ku munda wake ndi wina ku malonda ake. 6Ndipo otsalawo anagwira antchito ake, nawazunza ndi kuwapha. 7Mfumu inakwiya. Inatumiza asilikali ake ndipo anawononga opha anzawowo ndi kutentha mzinda wawo.

8“Pamenepo anati kwa antchito ake, ‘Phwando laukwati lakonzedwa, koma amene ndinawayitana sanali oyenera. 9Pitani ku mphambano za misewu ndipo kayitaneni aliyense amene mukamupeze kuti abwere ku phwando.’ 10Pamenepo antchitowo anapita ku misewu nakasonkhanitsa anthu onse amene anakawapeza, abwino ndi oyipa omwe, ndipo nyumba ya madyerero inadzaza ndi oyitanidwa.

11“Koma pamene mfumu inabwera kudzaona oyitanidwawo, inaona munthu amene sanavale zovala zaukwati. 12Inamufunsa kuti, ‘Bwenzi walowa bwanji muno wopanda zovala zaukwati?’ Munthuyo anakhala chete.

13“Pamenepo mfumuyo inawuza otumikira kuti, ‘Mʼmangeni manja ndi miyendo, ndipo muponyeni kunja, ku mdima kumene kudzakhale kulira ndi kukuta mano.’

14“Popeza oyitanidwa ndi ambiri koma osankhidwa ndi ochepa.”

Za Kupereka Msonkho

15Kenaka Afarisi anatuluka nakakonza njira zomupezera zifukwa Yesu mʼmawu ake. 16Anatumiza ophunzira awo kwa Iye pamodzi ndi Aherodia. Anati, “Aphunzitsi, tidziwa kuti ndinu wangwiro ndi kuti mumaphunzitsa mawu a Mulungu monga mwa choonadi. Simutekeseka ndi anthu, popeza simusamala kuti kodi ndi ndani? 17Tiwuzeni tsono maganizo anu ndi otani, kodi nʼkololedwa kupereka msonkho kwa Kaisara kapena ayi?”

18Koma Yesu podziwa maganizo awo oyipa anati, “Inu achiphamaso, bwanji mufuna kundipezera chifukwa? 19Onetseni ndalama imene mumapereka msonkho.” Iwo anabweretsa dinari, 20ndipo anawafunsa kuti, “Kodi chithunzi ichi ndi malemba awa ndi za ndani?”

21Iwo anayankha kuti, “Ndi za Kaisara.”

Pamenepo anawawuza kuti, “Perekani kwa Kaisara zake za Kaisara, ndi kwa Mulungu zake za Mulungu.”

22Atamva izi, anadabwa, ndipo anamusiya Iye, nachoka.

Ukwati ndi za Kuuka kwa Akufa

23Tsiku lomwelo Asaduki amene amati kulibe za kuukanso, anabwera kwa Iye ndi funso. 24Iwo anati, “Aphunzitsi, Mose anatiwuza kuti munthu akamwalira wosasiya ana, mʼbale wake akuyenera kukwatira mkazi wamasiyeyo kuti amuberekere ana mʼbale wakeyo. 25Tsopano panali abale asanu ndi awiri pakati pathu. Woyambayo anakwatira ndipo anamwalira, ndipo popeza analibe ana, mʼbale wake analowa chokolo. 26Izi zinachitikiranso mʼbale wa chiwiri ndi wachitatu mpaka wachisanu ndi chiwiri. 27Pa mapeto pake mkaziyo anamwaliranso. 28Tsopano, kodi akadzaukitsidwa adzakhala mkazi wa ndani mwa asanu ndi awiriwa popeza aliyense anamukwatirapo?”

29Yesu anayankha kuti, “Inu mukulakwitsa chifukwa simukudziwa malemba kapena mphamvu ya Mulungu. 30Anthu akadzaukitsidwa, sadzakwatira kapena kukwatiwa; adzakhala ngati angelo kumwamba. 31Koma za kuukitsidwa kwa akufa, kodi simunawerenge zimene Mulungu ananena kwa inu kuti, 32‘Ine ndine Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake ndi Mulungu wa Yakobo?’ Iyeyo si Mulungu wa akufa koma wa amoyo.”

33Magulu a anthu atamva zimenezi, anazizwa ndi chiphunzitso chake.

Lamulo Lalikulu Koposa

34Pakumva kuti Yesu anawakhalitsa chete Asaduki, Afarisi anasonkhana pamodzi. 35Mmodzi wa iwo, katswiri wa malamulo anamuyesa Iye ndi funso ndipo anati, 36“Aphunzitsi, kodi lamulo lalikulu koposa mu malamulo ndi liti?” 37Yesu anayankha kuti, “Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse ndi moyo wako wonse ndi nzeru zako zonse. 38Ili ndi lamulo loyamba ndi loposa onse. 39Ndipo lachiwiri ndi lofanana nalo: ‘Konda mnansi wako monga iwe mwini.’ 40Malamulo onse ndi aneneri zakhazikika pa malamulo awiriwa.”

Kodi Khristu ndi Mwana wa Ndani?

41Afarisi atasonkhana pamodzi, Yesu anawafunsa kuti, 42“Kodi mukuganiza bwanji za Khristu? Ndi Mwana wa ndani?”

Iwo anayankha kuti, “Mwana wa Davide.”

43Iye anawawuza kuti, “Nanga zikutheka bwanji kuti Davide poyankhula mwa Mzimu Woyera amatchula Iye ‘Ambuye?’ Pakuti akuti,

44“Ambuye anati kwa Ambuye wanga:

‘Khala pa dzanja langa lamanja

mpaka ndiyike adani ako

pansi pa mapazi ako.’

45Ngati tsono Davide amamutchula ‘Ambuye,’ zingatheke bwanji kukhala mwana wake?” 46Panalibe wina anatha kuyankha, ndipo kuchokera pamenepo, panalibe wina anayerekeza kumufunsa funso.

Священное Писание

Матай 22:1-46

Притча о свадебном пире

(Лк. 14:16-24)

1Иса продолжал учить народ в притчах, говоря:

2– Царство Всевышнего можно сравнить со свадебным пиром, который один царь приготовил для своего сына. 3Он разослал к приглашённым своих рабов, чтобы позвать их на свадьбу, но приглашённые не хотели прийти. 4Тогда царь послал других рабов, наказав им: «Пойдите и скажите им, что мой пир уже готов, зарезаны быки и другой откормленный скот, всё угощение готово, пусть приходят на свадебный пир». 5Приглашённые, однако, не обратили на это никакого внимания и разошлись. Один пошёл на своё поле, другой торговать, 6а некоторые даже схватили посланных рабов, унизили и убили их. 7Царь был разгневан. Он послал своё войско, уничтожил тех убийц и сжёг их город.

8Потом он сказал своим рабам: «Свадебный пир готов, но те, кого я пригласил, не заслужили чести быть на нём. 9Пойдите теперь на перекрёстки дорог и приглашайте на пир всех, кого вы встретите». 10Рабы пошли по улицам и стали созывать всех, кого встречали, злых и добрых, и пиршественный зал наполнился гостями, которые возлежали за столами. 11Когда же царь пришёл посмотреть на возлежащих, он заметил человека, на котором не было свадебной одежды. 12«Друг, – спросил царь, – как это ты вошёл сюда без свадебной одежды?» Человеку нечего было сказать. 13Тогда царь приказал слугам: «Свяжите его по рукам и ногам и выбросьте вон, во тьму, где будет плач и скрежет зубов». 14Ведь приглашённых много, но избранных мало.

Вопрос об уплате налогов

(Мк. 12:13-17; Лк. 20:20-26)

15После этого блюстители Закона стали советоваться, как бы им поймать Ису на слове. 16Они подослали к Нему своих учеников вместе со сторонниками правителя Ирода.

– Учитель, – спросили они, – мы знаем, что Ты Человек честный и истинно учишь пути Всевышнего. Ты беспристрастен и не стремишься никому угодить. 17Скажи нам, как Ты считаешь, следует ли платить налог римскому императору или нет?

18Иса, зная их коварные намерения, сказал:

– Лицемеры, вы хотите поймать Меня на слове? 19Покажите Мне монету, которой платится дань.

Они принесли Ему серебряную монету22:19 Букв.: «динарий».. 20Иса спросил их:

– Кто на ней изображён и чьё на ней имя?

21– Императора, – ответили они.

Тогда Иса сказал им:

– Так и отдавайте императору то, что принадлежит императору, а Всевышнему – то, что принадлежит Всевышнему.

22Такой ответ их озадачил, и, оставив Ису, они ушли.

Вопрос о воскресении мёртвых

(Мк. 12:18-27; Лк. 20:27-40)

23В тот же день саддукеи, которые утверждают, что нет воскресения мёртвых, подошли к Исе. Они спросили Его:

24– Учитель, Муса сказал, что если кто-либо умрёт, не оставив детей, то его брат должен жениться на вдове и восстановить род своему брату22:24 См. Втор. 25:5-6.. 25Так вот, у нас тут было семеро братьев. Первый женился и умер бездетным, и вдова стала женой его брата. 26То же самое произошло и со вторым, и с третьим, и со всеми семью братьями. 27После всех умерла и женщина. 28Итак, после воскресения, которому из семи братьев она будет женой? Ведь все были её мужьями.

29Иса ответил им:

– Вы заблуждаетесь, потому что не знаете ни Писания, ни силы Всевышнего. 30Воскреснув, люди не будут ни жениться, ни выходить замуж, а будут как ангелы на небесах. 31Что же касается воскресения мёртвых, то разве вы не читали, что сказал вам Всевышний: 32«Я – Бог Ибрахима, Бог Исхака и Бог Якуба»?22:32 Исх. 3:6. Он Бог не мёртвых, а живых.

33Люди слушали и удивлялись Его учению.

Самое важное повеление

(Мк. 12:28-31; Лк. 10:25-28)

34Блюстители же Закона, услышав, как Иса заставил замолчать саддукеев, собрались вокруг Него. 35Один из них, учитель Таурата, чтобы поймать Ису на слове, спросил:

36– Учитель, какое повеление в Законе самое важное?

37Иса ответил:

– «Люби Вечного, Бога твоего, всем сердцем, всей душой и всем разумом своим»22:37 Втор. 6:5.. 38Это первое и самое важное повеление. 39Второе, не менее важное повеление: «Люби ближнего твоего, как самого себя»22:39 Лев. 19:18.. 40Всё учение Таурата и Книги Пророков основано на этих двух повелениях.

Масих – Повелитель Давуда

(Мк. 12:35-37; Лк. 20:41-44)

41Когда блюстители Закона собрались вместе, Иса спросил их:

42– Что вы думаете о Масихе? Чей Он сын?

– Сын Давуда, – ответили Ему.

43Иса говорит им:

– Почему же тогда Давуд, под водительством Духа, называет Масиха Повелителем? Ведь он говорит:

44«Вечный сказал моему Повелителю:

сядь по правую руку от Меня,

пока Я не повергну всех врагов Твоих

к ногам Твоим»22:44 Заб. 109:1..

45Итак, если Давуд называет Масиха Повелителем, то как же в таком случае Он может быть всего лишь его сыном?

46В ответ никто не мог сказать ни слова, и с этого дня они больше не решались задавать Ему вопросы.