Anzeru a Kummawa
1Atabadwa Yesu mʼBetelehemu wa ku Yudeya, mʼnthawi ya mfumu Herode, Anzeru a kummawa anabwera ku Yerusalemu 2nafunsa kuti, “Ali kuti amene wabadwa kukhala mfumu ya Ayuda? Chifukwa tinaona nyenyezi yake kummawa ndipo tabwera kudzamupembedza.”
3Mfumu Herode atamva zimenezi, anavutika mu mtima kwambiri pamodzi ndi anthu onse a mu Yerusalemu. 4Ndipo anayitanitsa anthu onse, akulu ansembe ndi aphunzitsi amalamulo nawafunsa kuti, “Kodi Khristu adzabadwira kuti?” 5Ndipo anamuyankha kuti, “Ku Betelehemu wa ku Yudeya chifukwa izi ndi zimene mneneri analemba kuti,
6“ ‘Koma iwe Betelehemu, chigawo cha Yudeya,
sindiwe wamngʼonongʼono mwa olamulira a Yudeya;
pakuti otsogolera adzachokera mwa iwe,
amene adzaweta anthu anga Aisraeli.’ ”
7Pomwepo Herode anawayitanira mseri Anzeruwo nawafunsitsa nthawi yeniyeni yomwe nyenyeziyo inaoneka. 8Ndipo anawatumiza ku Betelehemu nawawuza kuti, “Pitani mukafufuze za mwanayo mosamalitsa. Ndipo mukamupeza mudzandiwuze kuti inenso ndikamupembedze.”
9Atamva mawu a mfumu, ananyamuka ulendo wawo, ndipo taonani nyenyezi anayiona kummawa ija, inawatsogolera mpaka inayima pamwamba pa nyumba yomwe munali mwanayo. 10Pamene iwo anaona nyenyeziyo, anasangalala kwambiri. 11Pofika ku nyumbayo, anaona mwanayo pamodzi ndi amayi ake Mariya, ndipo anagwada namulambira Iye. Pomwepo anamasula chuma chawo ndi kupereka mphatso zawo za ndalama zagolide, lubani ndi mure. 12Ndipo atachenjezedwa mʼmaloto kuti asapitenso kwa Herode, anabwerera ku dziko la kwawo podzera njira ina.
Athawira ku Igupto
13Atachoka, taonani mngelo wa Ambuye anaonekera kwa Yosefe mʼmaloto nati, “Tadzuka, tenga mwanayo pamodzi ndi amayi ake ndipo muthawire ku Igupto. Mukakhale kumeneko mpaka nditakuwuza pakuti Herode adzafunafuna mwanayo kuti amuphe.” 14Atadzuka, Yosefe anatenga mwanayo ndi amayi ake usiku omwewo napita ku Igupto, 15nakhala kumeneko mpaka Herode atamwalira. Ndipo zinakwaniritsidwa zomwe ananena Ambuye mwa mneneri kuti, “Ndinayitana mwana wanga kuti atuluke mu Igupto.”
Kuphedwa kwa Ana mʼBetelehemu
16Herode atazindikira kuti Anzeruwo anamupusitsa, anakwiya kwambiri. Ndipo anatumiza anthu kukapha ana onse aamuna a mʼBetelehemu ndi midzi yozungulira amene anali a zaka ziwiri kapena zocheperapo, molingana ndi nthawi imene Anzeruwo anamuwuza. 17Pamenepo, zimene ananena mneneri Yeremiya zinakwaniritsidwa:
18“Kulira kukumveka ku Rama,
kubuma ndi kulira kwakukulu,
Rakele akulirira ana ake;
sakutonthozeka,
chifukwa ana akewo palibe.”
Abwerera ku Nazareti
19Atamwalira Herode, mngelo wa Ambuye anaonekera kwa Yosefe mʼmaloto ku Igupto 20nanena kuti, “Nyamuka, tenga mwanayo ndi amayi ake ndipo mupite ku dziko la Israeli, popeza amene anafuna moyo wa mwanayo anamwalira.”
21Tsono Yosefe atadzuka anatenga mwanayo ndi amayi ake kupita ku dziko la Israeli. 22Koma atamva kuti Arikelao akulamulira mu Yudeya mʼmalo mwa abambo ake, Herode, anaopa kupitako. Atachenjezedwa mʼmaloto, anapita ku Galileya, 23ndipo anakakhazikika mu mzinda wa Nazareti. Pamenepo zinakwaniritsidwa zonenedwa ndi aneneri kuti, “Adzatchedwa Mnazareti.”
Dar zvjezdoznanaca
1Isus se rodio u gradu Betlehemu u Judeji za vladavine kralja Heroda. U to vrijeme neki mudraci s Istoka stignu u Jeruzalem 2i stanu se raspitivati: “Gdje je taj novorođeni kralj Židova? Vidjeli smo njegovu zvijezdu na istoku pa smo mu se došli pokloniti.”
3To veoma uznemiri kralja Heroda, a i sav Jeruzalem. 4Kralj sazove svećeničke poglavare i pismoznance da se raspita gdje se Krist treba roditi. 5“U Betlehemu u Judeji”, odgovore mu, “jer je prorok napisao:
6‘Betleheme, ti nisi samo nevažno judejsko selo,
jer će iz tebe poteći vladar
koji će voditi moj narod, Izrael.’”2:6 Mihej 5:2; 2 Samuelova 5:2.
7Tada Herod potajno pošalje po mudrace da od njih dozna vrijeme pojavka zvijezde. 8Zatim ih pošalje u Betlehem: “Pođite i pomnjivo se raspitajte za dijete. Kad ga pronađete, vratite se i javite mi da mu se i ja pođem pokloniti.”
9Poslušali su kralja i pošli. I gle! Zvijezda koju su vidjeli da izlazi išla je pred njima sve dok se nije zaustavila iznad mjesta gdje se nalazilo dijete. 10Kad su ju ugledali, silno su se razveselili. 11Uđu u kuću i ugledaju dijete s njegovom majkom Marijom te padnu ničice i poklone mu se. Zatim otvore škrinje s blagom i daruju mu zlato, tamjan i smirnu. 12Poslije toga su u snu dobili upute da se ne vraćaju k Herodu, te su se u svoju zemlju vratili drugim putem.
Bijeg u Egipat
13Kad su otišli, anđeo se Gospodnji ukaže u snu Josipu. “Ustani i bježi u Egipat s djetetom i s njegovom majkom”, reče anđeo, “i ostani ondje sve dok ti ne kažem da se vratiš jer će kralj Herod tražiti dijete da ga ubije.”
14Josip ustane i još se iste noći zaputi u Egipat s Marijom i djetetom. 15Ostao je ondje sve do Herodove smrti. Time se ispunilo što je Gospodin rekao preko proroka: “Pozvao sam svojega sina iz Egipta.”2:15 Hošea 11:1.
16Kad uvidi da su ga mudraci izigrali, Herod se silno razgnjevi i pošalje vojnike da u Betlehemu i po svoj okolici pobiju sve dječake od dvije godine i mlađe, prema vremenu izlaska zvijezde za koje se raspitao u mudraca. 17Tada se ispunilo ono što je rekao prorok Jeremija:
18“U Rami se čuje glas,
zapomaganje i gorak plač;
to Rahela oplakuje svoju djecu
i ne dade se utješiti jer ih više nema.”
Povratak iz Egipta
19Kad je Herod umro, u Egiptu se anđeo Gospodnji ukaže Josipu u snu 20i reče mu: “Ustani i povedi dijete i njegovu majku natrag u izraelsku zemlju, jer su oni koji su ga pokušavali ubiti mrtvi.” 21On ustane, uzme dijete i majku i vrati se u Izrael. 22Putem dozna da je novim kraljem postao Arhelaj, Herodov sin, pa se prestraši. Tada i u snu dobije upozorenje da ne ide u Judeju, te umjesto toga ode u Galileju 23i nastani se u Nazaretu. Time se ispunilo što su o Mesiji napisali proroci: “Zvat će se Nazarećanin.”