Mateyu 19 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 19:1-30

Za Kuthetsa Ukwati

1Yesu atatsiriza kunena zinthu zimenezi, anachoka ku Galileya ndi kupita ku chigawo cha Yudeya mbali ina ya mtsinje wa Yorodani. 2Magulu akulu a anthu anamutsatira Iye, ndipo iwo anachiritsidwa pomwepo.

3Afarisi ena anabwera kwa Iye kudzamuyesa. Anamufunsa Iye nati, “Kodi ndikololedwa kuti mwamuna amuleke mkazi wake pa chifukwa china chilichonse?”

4Iye anayankha kuti, “Kodi simunawerenge kuti pachiyambi Mulungu analenga iwo, ‘mwamuna ndi mkazi?’ 5Ndipo anati, ‘Pa chifukwa ichi mwamuna adzasiya abambo ake ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake, ndipo awiriwo adzakhala thupi limodzi.’ 6Motero salinso awiri ayi koma mmodzi. Nʼchifukwa chake chimene Mulungu wachimanga pamodzi munthu wina asachilekanitse.”

7Ndipo iwo anamufunsa nati, “Nanga nʼchifukwa chiyani Mose analamula kuti mwamuna azipatsa mkazi wake kalata ya chisudzulo ndi kumuchotsa?”

8Yesu anayankha kuti, “Mose anakulolezani kuti muzisudzula akazi anu chifukwa cha kuwuma mitima kwanu. Koma sizinali chotere kuyambira pachiyambi. 9Ine ndikuwuzani kuti aliyense amene asudzula mkazi wake, osati chifukwa cha chiwerewere nakakwatira mkazi wina, achita chigololo.”

10Ophunzira ake anati kwa Iye, “Ngati umu ndi mmene zilili pa mwamuna ndi mkazi, kuli bwino kusakwatira.”

11Yesu anayankha kuti, “Si aliyense amene angavomere chiphunzitso ichi, koma kwa okhawo amene achimvetsetsa. 12Pakuti ena ndi akuti sangakwatire chifukwa anabadwa motero, ena ali motero chifukwa chofulidwa ndi anthu ndipo ena anawukana ukwati chifukwa cha ufumu wakumwamba. Iye amene angalandire ichi alandire.”

Yesu Adalitsa Ana

13Pamenepo anabwera nawo ana kwa Yesu kuti awasanjike manja ndi kuwapempherera. Koma ophunzira ake anadzudzula amene anabweretsa anawo.

14Yesu anati, “Lolani ana abwere kwa Ine, ndipo musawaletse pakuti ufumu wakumwamba ndi wa iwo onga anawa.” 15Atasanjika manja ake pa anawo, anachokapo.

Mnyamata Wolemera ndi Ufumu wa Mulungu

16Taonani mnyamata wina anabwera kwa Yesu namufunsa kuti, “Aphunzitsi, ndi chinthu chiti chabwino chimene ndiyenera kuchita kuti ndipeze moyo wosatha?”

17Yesu anayankha kuti, “Ukundifunsiranji Ine za chinthu chimene ndi chabwino? Pali mmodzi yekha amene ndi wabwino. Ngati ukufuna kulowa mʼmoyo wosatha mvera malamulo.”

18Mnyamatayo anamufunsa kuti, “Ndi ati?”

Yesu anayankha kuti, “Usaphe, usachite chigololo, usabe, usapereke umboni onama, 19lemekeza abambo ako ndi amayi ako ndipo konda mnansi wako monga iwe mwini.”

20Mnyamatayo anati, “Zonsezi ndimazisunga, nanga chatsala ndi chiyani?”

21Yesu anayankha kuti, “Ngati ukufuna kukhala wangwiro, pita kagulitse katundu wako ndi kupereka kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Ukakachita zimenezi, ukabwere udzanditsate Ine.”

22Mnyamatayo atamva zimenezi, anachoka mokhumudwa, chifukwa anali ndi chuma chambiri.

23Pamenepo Yesu anati kwa ophunzira ake, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti nʼkovuta kuti olemera akalowe mu ufumu wakumwamba. 24Komanso ndikuwuzani kuti, nʼkwapafupi kuti ngamira idzere pa kabowo ka zingano kusiyana ndi kuti wolemera akalowe mu ufumu wa Mulungu.”

25Ophunzira atamva zimenezi, anadabwa kwambiri ndipo anamufunsa kuti, “Nanga angapulumuke ndani?”

26Yesu anawayangʼana iwo nati, “Ndi anthu, izi nʼzosatheka, koma ndi Mulungu zinthu zonse zimatheka.”

27Petro anamuyankha Iye kuti, “Ife tinasiya zonse ndi kukutsatirani Inu! Nanga tsono ife tidzalandira chiyani?”

28Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti pa nthawi yokonzanso zinthu zonse, pamene Mwana wa Munthu adzakhala pa mpando wake waufumu mu ulemerero wake kumwamba, inu amene mwanditsata Ine mudzakhalanso pa mipando khumi ndi iwiri yaufumu, kuweruza mafuko khumi ndi awiri a Israeli. 29Ndipo aliyense amene wasiya nyumba, kapena abale, kapena alongo, kapena bambo kapena mayi kapena mkazi, kapena ana, kapena minda chifukwa cha Ine adzalandira madalitso ochuluka ndi kulandiranso moyo wosatha. 30Koma ambiri amene ali oyambirira adzakhala omalizira, ndipo ambiri amene ndi omalizira adzakhala oyambirira.”

Bibelen på hverdagsdansk

Mattæusevangeliet 19:1-30

Om ægteskab og skilsmisse

Mark. 10,1-12; Luk. 16,18

1Efter at Jesus havde undervist sine disciple om tilgivelse, tog de af sted fra Galilæa og vandrede gennem det jødiske område på den østlige side af Jordanfloden. 2Mange mennesker fulgte ham, og han helbredte dem, der var syge.

3Nogle farisæere prøvede at stille en fælde for Jesus og spurgte: „Har en mand lov til at skille sig fra sin kone uanset af hvilken grund?” 4-5Jesus svarede: „Har I ikke læst, at Gud fra begyndelsen skabte mennesket som mand og kvinde og sagde, at manden skal forlade sin far og mor og knytte sig til sin kone, og de to skal blive ét?19,4-5 1.Mos. 2,24. 6Altså er de ikke længere to, men en enhed. Det, som Gud på den måde har sammenføjet, må intet menneske splitte ad.”

7„Hvordan kan det så være, at Moses har sagt, at en mand godt må skille sig fra sin kone, når bare han giver hende et skilsmissebrev?”19,7 5.Mos. 24,1. fortsatte farisæerne.

8„Den indrømmelse gav Moses på grund af menneskers uforsonlige holdning, men det var ikke Guds mening fra begyndelsen,” svarede Jesus. 9„Det siger jeg jer: Hvis en mand skiller sig fra sin kone af nogen anden grund end utroskab fra hendes side og derefter gifter sig med en anden, så er han skyldig i ægteskabsbrud over for den første.”

10„Så er det nok bedre aldrig at gifte sig!” udbrød disciplene. 11„Det er ikke enhver, som kan forstå og tage til sig, hvad jeg siger, kun hvem det er givet,” svarede Jesus. 12„Der er nogle, som forbliver ugifte, fordi de fra fødslen af er ude af stand til at fuldbyrde et ægteskab, og andre, fordi mennesker har gjort dem ude af stand til det. Endelig er der nogle, der afstår fra ægteskab for Guds riges skyld. Den, som kan forstå det, kan tage det til sig.”

Hvordan man får adgang til Guds rige

Mark. 10,13-16; Luk. 18,15-17

13Derefter bragte nogle forældre deres børn hen til Jesus, for at han skulle lægge hænderne på dem og velsigne dem. Men disciplene ville jage dem bort. 14„Lad børnene være i fred,” sagde Jesus. „I må ikke hindre dem i at komme til mig, for det er sådan nogle som dem, der får adgang til Guds rige.” 15Så lagde han hænderne på dem og velsignede dem. Derefter brød de alle op og gik videre.

Hvordan man får det evige liv

Mark. 10,17-27; Luk. 18,18-27

16Så kom der en mand og spurgte: „Mester, sig mig: Hvad godt skal jeg gøre for at få del i det kommende liv?”

17„Hvorfor spørger du mig om det gode?” svarede Jesus. „Der er jo kun én, der er god, nemlig Gud selv. Men hvis du ønsker at gå ind til livet, så hold Guds bud.”

18„Hvilke bud tænker du på?” spurgte manden.

„Du må ikke begå drab, du må ikke bryde ægteskabet, du må ikke stjæle, du må ikke anklage nogen på falsk grundlag, 19du skal ære din far og din mor—og du skal elske din næste som dig selv.”

20„Dem har jeg overholdt alle sammen,” svarede den unge mand. „Er der mere, jeg skal gøre?”

21„Hvis du virkelig vil opnå det fuldkomne liv, så gå hen og sælg alt, hvad du ejer, og giv pengene til de fattige. Så skal du få del i Himlens rigdom—og kom så og følg mig!”

22Da den unge mand hørte det svar, gik han bedrøvet sin vej. Han var nemlig meget rig.

23Så sagde Jesus til disciplene: „Det siger jeg jer: Det er ikke let at komme ind i Guds rige, når man er bundet af sin rigdom. 24Ja, faktisk er det lettere for en kamel at gå gennem et nåleøje, end det er for en rig at gå ind i Guds rige.”

25Disciplene var dybt rystede. „Hvem kan så få det evige liv?” spurgte de. 26Jesus så på dem og sagde: „Det kan intet menneske opnå af sig selv, men Gud kan gøre alt.”

Lønnen for at følge Jesus

Mark. 10,28-31; Luk. 18,28-30; 22,28-30

27„Men vi har forladt alt for at følge dig. Hvad får vi så ud af det?” spurgte Peter.

28Jesus svarede: „Det siger jeg jer: Når Menneskesønnen sidder på sin herlighedstrone i den kommende verden, så skal I, mine disciple, sidde på 12 troner og regere over Israels 12 stammer. 29Alle, som har forladt deres hjem, brødre, søstre, far, mor, børn eller deres job for at følge mig, skal få det 100 gange igen—og de skal få det evige liv! 30Men mange, der her på jorden regnes blandt de store, vil i Guds rige være de mindste. Og mange af dem, der her er blandt de mindste, vil dér være de største.”