Mateyu 16 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 16:1-28

Afarisi ndi Asaduki Afuna Chizindikiro

1Afarisi ndi Asaduki anabwera kwa Yesu ndi kumuyesa pomufunsa kuti awaonetse chizindikiro chochokera kumwamba.

2Iye anayankha kuti, “Kunja kukamada, inu mumati, kudzakhala nyengo yabwino popeza thambo ndi lofiira. 3Ndipo mmawa mumati, ‘Lero kudzakhala mvula yamphepo popeza thambo ndi lofiira ndi mitambo ya mvula.’ Inu mumadziwa kutanthauzira maonekedwe a thambo koma simungathe kutanthauzira zizindikiro za nthawi. 4Mʼbado woyipa ndi wachigololo umafuna chizindikiro chodabwitsa koma palibe ngakhale chimodzi chidzapatsidwa kupatula chizindikiro cha Yona.” Pamenepo Yesu anawasiya nachoka.

Yisiti wa Afarisi ndi Asaduki

5Koma atawoloka nyanja, ophunzira anayiwala kutenga buledi. 6Yesu anawawuza kuti, “Chenjerani, khalani tcheru ndi yisiti wa Afarisi ndi Asaduki.”

7Iwo anakambirana pakati pawo za izi ndipo anati, “Ichi nʼchifukwa chakuti sitinatenge buledi aliyense.”

8Yesu atadziwa zokambirana zawo, anawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukukambirana zakuti, ‘mulibe buledi?’ Inu achikhulupiriro chochepa. 9Kodi inu simukumvetsetsabe? Kodi simukukumbukira za buledi musanu amene anadya anthu 5,000 ndi madengu amene munadzaza? 10Kapena buledi musanu ndi muwiri amene anadya anthu 4,000, nanga ndi madengu angati amene munadzaza? 11Zitheka bwanji kuti inu simukumvetsetsa kuti Ine sindinkayankhula nanu za buledi? Koma inu chenjerani ndi yisiti wa Afarisi ndi Asaduki.” 12Kenaka iwo anazindikira kuti Iye samawawuza kuti achenjere ndi yisiti wa buledi koma ndi chiphunzitso cha Afarisi ndi Asaduki.

Petro Avomereza za Yesu

13Yesu atafika ku chigawo cha Kaisareya Filipo, Iye anafunsa ophunzira ake kuti, “Kodi anthu amati Mwana wa Munthu ndi ndani?”

14Iwo anayankha kuti, “Ena amati ndi Yohane Mʼbatizi; ena amati ndi Eliya; komanso ena amati Yeremiya kapena mmodzi wa aneneri.”

15Iye anafunsa kuti, “Nanga inuyo mumati ndine yani?”

16Simoni Petro anayankha kuti, “Inu ndinu Khristu, Mwana wa Mulungu wamoyo.”

17Yesu anati kwa iye, “Ndiwe wodala Simoni mwana wa Yona, popeza si munthu amene anakuwululira izi koma Atate anga akumwamba. 18Ndipo Ine ndikuwuza iwe kuti ndiwe Petro ndipo pa thanthwe ili Ine ndidzamangapo mpingo wanga ndipo makomo a ku gehena sadzawugonjetsa. 19Ine ndidzakupatsa makiyi a Ufumu wakumwamba, ndipo chilichonse chimene iwe udzachimanga pansi pano chidzamangidwanso kumwamba.” 20Pamenepo Iye anachenjeza ophunzira ake kuti asawuze wina aliyense kuti ndi Khristu.

Yesu Aneneratu za Imfa Yake

21Kuyambira nthawi imeneyo Yesu anayamba kuwafotokozera ophunzira ake kuti Iye ayenera kupita ku Yerusalemu ndi kukazunzidwa kwambiri mʼmanja mwa akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo kuti ayenera kuphedwa, ndi kuti tsiku lachitatu adzaukitsidwa.

22Petro anamutengera Iye pambali nayamba kumudzudzula kuti, “Dzichitireni chifundo Ambuye, sizingachitike kwa Inu ayi.”

23Yesu anatembenuka nati kwa Petro, “Choka pamaso panga Satana! Iwe ndi chokhumudwitsa kwa Ine; iwe suganizira zinthu za Mulungu koma zinthu za anthu.”

Za Kusenza Mtanda

24Pamenepo Yesu anati kwa ophunzira ake, “Ngati wina aliyense abwera pambuyo panga ayenera kudzikana ndi kutenga mtanda wake ndi kunditsata Ine. 25Pakuti aliyense amene afuna kupulumutsa moyo wake adzawutaya koma aliyense amene ataya moyo wake chifukwa cha Ine adzawupeza. 26Kodi munthu adzapindula chiyani ngati atapeza zonse za dziko lapansi nataya moyo wake? Kapena munthu angapereke chiyani chosinthana ndi moyo wake? 27Pakuti Mwana wa Munthu adzabwera mu ulemerero wa Atate ake ndi angelo ake ndipo pamenepo Iye adzapereka mphotho kwa munthu mofanana ndi zimene anachita.

28“Ine ndikuwuzani inu choonadi, ena amene akuyimirira pano sadzalawa imfa asanaone Mwana wa Munthu akudza mu ufumu.”

New Russian Translation

Матфея 16:1-28

Религиозные вожди требуют знамения с неба

(Мк. 8:11-13; Лк. 12:54-56)

1Там Иисуса обступили фарисеи и саддукеи, которые, желая испытать Его, просили, чтобы Он показал им знамение с неба. 2Иисус ответил:

– На закате, увидев, что небо красное, вы говорите: «Будет хорошая погода», 3а на рассвете, если небо заволокло багровыми тучами, вы говорите: «Будет буря». Вы знаете, что означают приметы неба, а истолковать знаков времени не можете. 4Злое и развратное поколение ищет знамения, но ему не будет дано никакого знамения, кроме знамения Ионы16:4 Знамение Ионы: см. 12:40..

И, оставив их, Иисус ушел.

Иисус предостерегает от ложных учений

(Мк. 8:14-21)

5Переправляясь на другую сторону озера, ученики забыли взять с собой хлеба.

6Иисус же сказал им:

– Смотрите, берегитесь закваски фарисеев и саддукеев.

7Ученики стали рассуждать между собой:

– Он говорит это потому, что мы не взяли с собой хлеба.

8Иисус, зная, о чем они говорят, сказал:

– Маловеры, почему вы рассуждаете между собой о том, что у вас нет хлеба? 9Неужели вы еще не поняли? Разве вы не помните, как пяти хлебов хватило на пять тысяч человек? Сколько вы тогда собрали корзин с остатками? 10А сколько корзин остатков вы собрали, когда четыре тысячи16:10 См. Мк. 8:9. мужчин наелись семью хлебами? 11Как вы не можете понять, что, говоря: «Берегитесь закваски фарисеев и саддукеев», Я говорю не о хлебе?

12Тогда ученики поняли, что Он предостерегал их не от закваски, которую кладут в хлеб, а от учения фарисеев и саддукеев.

Петр признает Иисуса Мессией

(Мк. 8:27-30; Лк. 9:18-21)

13Когда Иисус пришел в окрестности Кесарии Филипповой, Он спросил Своих учеников:

– За кого люди принимают Сына Человеческого?

14Ученики ответили:

– Одни говорят, что Ты – Иоанн Креститель, другие – что Илия, а третьи – что Иеремия или один из других пророков.

15– А вы кем считаете Меня? – спросил их Иисус.

16Симон Петр ответил:

– Ты – Христос, Сын живого Бога.

17Тогда Иисус сказал:

– Блажен ты, Симон, сын Ионы, потому что это было открыто тебе не людьми, а Моим Небесным Отцом. 18И Я говорю тебе: ты – Петр16:18 Имя Петр означает «камень»., и на этой скале Я построю Мою Церковь, и врата ада не одолеют ее. 19Я дам тебе ключи от Небесного Царства, и что ты запретишь на земле, то будет запрещено на небесах, и все, что ты разрешишь на земле, будет разрешено и на небесах.

20Затем Иисус велел ученикам никому не говорить о том, что Он – Христос.

Иисус впервые говорит о Своей смерти и воскресении

(Мк. 8:31-33; Лк. 9:22)

21С этого времени Иисус начал объяснять ученикам, что Он должен идти в Иерусалим и там много пострадать от старейшин, первосвященников и учителей Закона, что Он будет убит, но на третий день воскреснет.

22Тогда Петр отвел Его в сторону и стал возражать:

– Да помилует Тебя Бог! Пусть не случится с Тобой этого, Господи!

23Иисус же, обернувшись, сказал Петру:

– Прочь от Меня, сатана! Ты Мне камень преткновения, потому что рассуждаешь по-человечески и не понимаешь того, что хочет Бог.

Что значит быть последователем Иисуса Христа

(Мк. 8:34–9:1; Лк. 9:23-27)

24Потом Иисус сказал ученикам:

– Если кто желает быть Моим последователем, пусть отречется от самого себя, возьмет свой крест и пусть следует за Мной. 25Потому что тот, кто хочет сберечь свою жизнь, потеряет ее, а кто потеряет свою жизнь ради Меня, тот обретет ее. 26Ведь что пользы человеку, если он приобретет весь мир, но при этом повредит своей душе? Или что даст человек в обмен за свою душу? 27Когда Сын Человеческий придет в славе Своего Отца, окруженный Своими ангелами, тогда Он воздаст каждому по его делам. 28Говорю вам истину: некоторые из вас, стоящих здесь, не умрут, пока не увидят прежде Сына Человеческого, пришедшего в Своем Царстве.