Mateyu 15 – CCL & HHH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 15:1-39

Miyambo ya Makolo

1Pamenepo Afarisi ena ndi aphunzitsi amalamulo anabwera kwa Yesu kuchokera ku Yerusalemu ndipo anamufunsa kuti, 2“Chifukwa chiyani ophunzira anu amaphwanya mwambo wa akuluakulu? Iwo sasamba mʼmanja pakudya!”

3Yesu anayankha kuti, “Nanga chifukwa chiyani inu mumaphwanya lamulo la Mulungu chifukwa cha mwambo wa makolo anu? 4Pakuti Mulungu anati, ‘Lemekeza abambo ako ndi amayi ako’ ndipo ‘aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa.’ 5Koma inu mumati, ngati munthu anena kwa abambo ake kapena amayi ake kuti, ‘Thandizo lililonse mukalirandira kuchokera kwa ine ndi mphatso yoperekedwa kwa Mulungu,’ 6iye sakulemekeza nayo abambo ake ndipo ndi khalidwe lotere inu mumapeputsa nalo Mawu a Mulungu chifukwa cha mwambo wanu. 7Inu anthu achiphamaso, Yesaya ananenera za inu kuti,

8“ ‘Anthu awa amandilemekeza Ine ndi milomo yawo,

koma mitima yawo ili kutali ndi Ine.

9Amandilambira Ine kwachabe

ndi kuphunzitsa malamulo ndi malangizo a anthu.’ ”

10Yesu anayitana gulu la anthu nati, “Mverani ndipo zindikirani. 11Chimene chimalowa mʼkamwa mwa munthu sichimuchititsa kukhala woyipa, koma chimene chimatuluka mʼkamwa mwake, icho ndi chimene chimamuchititsa kukhala woyipa.”

12Pamenepo ophunzira anabwera kwa Iye ndipo anamufunsa kuti, “Kodi mukudziwa kuti Afarisi anakhumudwa pamene anamva mawu aja?”

13Iye anayankha kuti, “Mbewu iliyonse imene Atate anga akumwamba sanadzale idzazulidwa ndi mizu yomwe. 14Alekeni, ndi atsogoleri osaona. Ngati munthu wosaona atsogolera wosaona mnzake, onse awiri adzagwera mʼdzenje.”

15Petro anati, “Timasulireni fanizoli.”

16Yesu anawafunsa kuti, “Kani ngakhale inunso simumvetsa? 17Kodi inu simudziwa kuti chilichonse cholowa mʼkamwa chimapita mʼmimba ndipo kenaka chimatuluka kunja kwa thupi? 18Koma zinthu zimene zituluka mʼkamwa zimachokera mu mtima ndipo zimenezi zimamuchititsa munthu kukhala woyipa. 19Pakuti mu mtima mumatuluka maganizo oyipa, zakupha, zachigololo, zadama, zakuba, zaumboni wonama ndi zachipongwe. 20Izi ndi zimene zimachititsa munthu kukhala woyipa; koma kudya ndi mʼmanja mosasamba sikumuchititsa munthu kukhala woyipa.”

Mayi wa ku Kanaani

21Yesu atachoka kumalo amenewo anapita kudera la ku Turo ndi ku Sidoni. 22Mayi wa Chikanaani wochokera dera la komweko anabwera kwa Iye akulira, nati, “Ambuye, Mwana wa Davide, ndichitireni chifundo! Mwana wanga wamkazi akuzunzika kwambiri ndi chiwanda.”

23Yesu sanayankhe kanthu. Ndipo ophunzira ake anabwera namupempha Iye kuti, “Muwuzeni achoke chifukwa akulira mofuwula pambuyo pathu.”

24Iye anayankha kuti, “Ine ndinatumidwa kwa nkhosa zotayika za Israeli zokha.”

25Mayiyo anabwera ndi kugwada pamaso pake, nati, “Ambuye ndithandizeni!”

26Iye anayankha kuti, “Sibwino kutenga chakudya cha ana ndi kuponyera agalu.”

27Mayiyo anati, “Inde Ambuye. Komatu ngakhale agalu amadya nyenyeswa zimene zimagwa kuchokera pa tebulo la mbuye wawo.”

28Pomwepo Yesu anayankha kuti, “Mayi iwe uli ndi chikhulupiriro chachikulu! Pempho lako lamveka.” Ndipo mwana wake wamkazi anachira nthawi yomweyo.

Yesu Adyetsa Anthu 4,000

29Yesu anachoka kumeneko napita mʼmbali mwa nyanja ya Galileya. Ndipo anakwera ku phiri nakhala pansi. 30Gulu lalikulu la anthu linabwera kwa Iye ndi anthu olumala, osaona, ofa ziwalo, osayankhula ndi ena ambiri nawagoneka pa mapazi ake ndipo Iye anawachiritsa. 31Anthu ataona osayankhula akuyankhula, ofa ziwalo akuchira, olumala miyendo akuyenda ndi osaona akuona anadabwa kwambiri. Ndipo analemekeza Mulungu wa Israeli.

32Yesu anayitana ophunzira ake nati, “Ndili ndi chifundo ndi anthu awa; akhala kale ndi Ine masiku atatu ndipo alibe chakudya. Ine sindifuna kuti apite kwawo ndi njala chifukwa angakomoke pa njira.”

33Ophunzira anayankha kuti, “Ndikuti kumene tingakapeze buledi mʼtchire muno okwanira kudyetsa gulu lotere?”

34Yesu anawafunsa kuti, “Muli ndi malofu a buledi angati?”

Iwo anayankha kuti, “Asanu ndi awiri ndi tinsomba pangʼono.”

35Iye anawuza gululo kuti likhale pansi. 36Kenaka anatenga malofu asanu ndi awiri aja ndi tinsombato ndipo atayamika anagawa napatsa ophunzira ake ndipo iwo anagawira anthuwo. 37Onse anadya ndipo anakhuta. Pomaliza ophunzira anatolera zotsalira nadzaza madengu asanu ndi awiri. 38Chiwerengero cha anthu amene anadya chinali 4,000 kupatula amayi ndi ana. 39Yesu atatha kuwuza gululo kuti lipite kwawo, analowa mʼbwato ndipo anapita kudera la Magadala.

Habrit Hakhadasha/Haderekh

הבשורה על-פי מתי 15:1-39

1יום אחד הגיעו מירושלים מספר פרושים וסופרים כדי לחקור את ישוע.

2”מדוע תלמידיך אינם מקיימים את המסורת היהודית העתיקה?“ דרשו לדעת. ”מדוע תלמידיך אינם נוטלים את ידיהם לפני האוכל?“

3השיב להם ישוע: ”ומדוע עוברת המסורת שלכם על מצוותיו של אלוהים? 4למשל, כתוב בתורה:15‏.4 טו 4 שמות כ 12, כא 17 ’כבד את אביך ואת אמך… ומקלל אביו ואמו מות יומת!‘ 5‏-6אולם אתם אומרים שמותר לאדם להתעלם מצרכי הוריו העניים, אם ייתן ’לעבודת האלוהים‘ את מה שיכול היה לתת להם. וכך אתם מפרים את מצוותו של אלוהים, כדי לקיים מסורת וחוקים שהומצאו על־ידי בני־אדם. 7צבועים שכמוכם! הנביא ישעיהו תיאר אתכם נכונה כשאמר:15‏.7 טו 7 ישעיהו כט 13

8’ניגש העם הזה בפיו,

ובשפתיו כבדוני ולבו רחק ממני;

9ותהי יראתם אותי מצות אנשים מלומדה‘. “

10ישוע אסף סביבו את הקהל ואמר: ”הקשיבו לדבריי והשתדלו להבינם: 11מה שמטמא את האדם זה לא מה שנכנס לפה אלא מה שיוצא מהפה – זה מטמא את האדם!“

12תלמידיו באו אליו ואמרו: ”בדבריך אלה העלבת את הפרושים!“

13ישוע השיב להם: ”כל צמח שלא נשתל על־ידי אבי – ייעקר. 14התעלמו מהם; הפרושים אינם אלא מורי־דרך עיוורים המדריכים עיוורים אחרים, ובסופו של דבר יפלו כולם יחד לתוך בור!“

15שמעון פטרוס ביקש מישוע שיסביר למה התכוון באמרו שאנשים מטמאים את עצמם ממה שיוצא מן הפה.

16”האם אינך מבין?“ שאל אותו ישוע. 17”האם אינך רואה שכל מה שאתה אוכל עובר דרך מערכת העיכול ויוצא שוב החוצה? 18אולם מילים רעות יוצאות מתוך לב רע ומטמאות את האומר אותן. 19כי מתוך הלב יוצאות מחשבות רעות, מעשי רצח, ניאוף, זנות, גניבה, שקר ורכילות. 20דברים אלה הם המטמאים את האדם. אכילה ללא נטילת ידיים אינה מטמאת את האדם.“

21ישוע עזב את האזור ההוא והלך אל אזור צור וצידון.

22אישה כנענית שגרה שם באה אל ישוע והתחננה: ”אדוני, בן־דוד, רחם עלי! שד אחז בבתי והוא מענה אותה ללא הרף.“ 23אולם ישוע לא ענה לה – אף לא מילה אחת. תלמידיו ביקשו ממנו לגרש אותה: ”אמור לה ללכת מכאן, כי היא מציקה לנו כל היום בתחינותיה.“

24”נשלחתי אל צאן האובדות של בית ישראל בלבד“, אמר ישוע לאישה. 25אולם האישה נפלה לרגליו ושוב ביקשה: ”אדוני, עזור לי!“

26”אין זה צודק לקחת את לחמם של הילדים ולהשליכו לכלבים“, ענה לה ישוע.

27”נכון, אדוני,“ השיבה האישה, ”אבל גם לגורי הכלבים מותר לאכול את הפירורים שנופלים מעל שולחן אדוניהם.“

28”אישה,“ אמר לה ישוע, ”יש בך אמונה רבה, ולכן תתמלא בקשתך.“ באותו רגע בתה נרפאה.

29ישוע חזר לכינרת, עלה על גבעה והתיישב שם. 30ההמונים הביאו אליו פיסחים, עיוורים, בעלי־מום, אילמים וחולים אחרים, הניחו אותם לפניו, והוא ריפא את כולם. 31כאשר העם ראה את האילמים מפטפטים בהתרגשות, קטועי האיברים מקבלים איברים חדשים, נכים קופצים ורוקדים והעיוורים מביטים סביבם, נדהמו ושבחו את אלוהי ישראל.

32לאחר מכן קרא ישוע לתלמידיו ואמר: ”אני מרחם על אנשים אלה; הם נמצאים אתי כאן שלושה ימים, ולא נשאר להם מה לאכול. אינני רוצה לשלוח אותם רעבים, כי הם עלולים להתעלף בדרך.“

33”מאין נשיג במדבר הזה מספיק אוכל לכל ההמון?“ שאלו התלמידים.

34”כמה ככרות לחם יש לכם?“ שאל אותם ישוע. ”שבע,“ ענו, ”וכמה דגים קטנים.“

35ישוע ציווה על העם לשבת על הארץ, 36לקח את שבע ככרות הלחם ואת הדגים, הודה לאלוהים עליהם, חילק אותם למנות ונתן לתלמידים, כדי שיגישו ליושבים. 37‏-38אכלו לשובע (כארבעת־אלפים איש לא כולל נשים וילדים), כאשר אספו את השאריות הם מילאו שבעה סלים!

39לאחר מכן שלח ישוע את האנשים לביתם, והוא עצמו עלה לסירה ושט למגדל.