Mateyu 10 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 10:1-42

Yesu Atuma Ophunzira Ake

1Yesu anayitana ophunzira ake khumi ndi awiri ndipo anawapatsa ulamuliro otulutsa mizimu yoyipa ndi kuchiritsa nthenda iliyonse ndi zofowoka zilizonse.

2Mayina a atumwi khumi ndi awiriwo ndi awa: woyamba, Simoni (wotchedwa Petro) ndi mʼbale wake Andreya; Yakobo mwana wa Zebedayo ndi mʼbale wake Yohane, 3Filipo ndi Bartumeyu, Tomasi ndi Mateyu wolandira msonkho, Yakobo mwana wa Alufeyo ndi Tadeyo; 4Simoni Mzerote ndi Yudasi Isikarioti, amene anamupereka Iye.

5Yesu anatuma khumi ndi awiriwo ndi kuwalamula kuti, “Musapite kwa anthu a mitundu ina kapena kulowa mʼmudzi uliwonse wa Asamariya. 6Koma pitani kwa nkhosa zotayika za banja la Israeli. 7Pamene mukupita, muzikalalikira uthenga uwu: ‘Ufumu wakumwamba wayandikira.’ 8Chiritsani odwala, ukitsani akufa, chiritsani akhate, tulutsani ziwanda. Munalandira kwaulere, perekani kwaulere.

9“Musatenge ndalama zagolide kapena zasiliva kapena zakopala mʼzikwama mwanu; 10musatenge thumba la paulendo, kapena malaya awiri kapena nsapato kapena ndodo; pakuti wantchito ayenera kulandira chakudya chake. 11Mukalowa mu mzinda ndi mʼmudzi uliwonse, funafunani munthu woyenera ndipo mukhale mʼnyumba mwake kufikira mutachoka. 12Pamene mulowa mʼnyumba mupereke moni. 13Mtendere wanu ukhale pa a mʼnyumbayo ngati ndi oyenera. Koma ngati siwoyenera, mtendere wanu ubwerere kwa inu. 14Ngati wina aliyense sakakulandirani kapena sakamvera mawu anu, musase fumbi la kumapazi anu pamene mutuluka mʼnyumbayo kapena mu mzindawo. 15Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti pa tsiku lachiweruziro, mlandu wa Sodomu ndi Gomora udzachepa kusiyana ndi wa mzindawo.

16“Taonani ndikukutumizani inu monga nkhosa pakati pa mimbulu. Chifukwa chake khalani ochenjera ngati njoka ndi woona mtima ngati nkhunda. 17Chenjerani ndi anthu pakuti adzakuperekani ku mabwalo amilandu nadzakukwapulani mʼmasunagoge mwawo. 18Chifukwa cha Ine, mudzaperekedwa kwa olamulira ndi kwa mafumu kuti mukhale mboni kwa iwo ndi kwa a mitundu ina. 19Koma pamene akumangani, inu musadandaule kuti mukanena bwanji kapena mukanena chiyani. Mudzapatsidwa pa nthawi imeneyo zoti munene, 20pakuti sindinu mudzanena, koma Mzimu Woyera wa Atate anu, adzayankhula mwa inu.

21“Mʼbale adzapereka mʼbale kuti aphedwe ndi abambo mwana wawo: ndipo ana adzawukira makolo awo ndi kuwapereka kuti aphedwe. 22Anthu onse adzada inu chifukwa cha Ine, koma iye amene apirira mpaka kumapeto, adzapulumuka. 23Pamene akuzunzani pamalo ena thawirani kwina. Pakuti ndikuwuzani zoonadi kuti simudzamaliza mizinda yonse ya Israeli Mwana wa Munthu asanabwere.

24“Wophunzira saposa mphunzitsi wake ndipo wantchito saposa bwana wake. 25Nʼkoyenera kuti wophunzira akhale ngati mphunzitsi wake, ndi wantchito akhale ngati bwana wake. Ngati mwini banja atchedwa Belezebabu, koposa kotani a mʼnyumba mwake!

26“Chifukwa chake musaope iwo. Pakuti palibe chinthu chobisika chimene sichidzavundukulidwa, ndi chobisika chimene sichidzadziwika. 27Chimene ndikuwuzani Ine mu mdima, muchiyankhule poyera; chimene akunongʼonezani mʼkhutu, muchilalikire muli pa denga. 28Musamaope amene amapha thupi koma sangathe kuchotsa moyo. Koma muziopa Iye amene akhoza kupha mzimu ndi kuwononga thupi mu gehena. 29Kodi suja amagulitsa mbalame ziwiri ndi ndalama imodzi? Koma palibe imodzi ya izo imene idzagwa pansi wopanda chifuniro cha Atate anu. 30Ndipo ngakhale tsitsi la mʼmutu mwanu linawerengedwa kale. 31Potero musaope; inu ndinu a mtengo woposa mbalame zambiri.

32“Aliyense amene avomereza Ine pamaso pa anthu, Inenso ndidzavomereza pamaso pa Atate anga akumwamba. 33Koma iye amene andikana Ine pamaso pa anthu, Inenso ndidzamukana pamaso pa Atate anga akumwamba.

34“Musaganize kuti Ine ndabweretsa mtendere pa dziko lapansi. Sindinabwere kudzapereka mtendere koma lupanga. 35Pakuti Ine ndabwera kudzalekanitsa

“ ‘Munthu ndi abambo ake,

mwana wamkazi ndi amayi ake,

mtengwa kulekanitsidwa ndi apongozi ake,

36adani a munthu adzakhala a mʼbanja mwake momwe.’

37“Aliyense amene akonda abambo kapena amayi ake koposa Ine sayenera kukhala wanga; aliyense amene akonda mwana wake wamwamuna kapena wamkazi koposa Ine sayenera kukhala wanga. 38Aliyense amene satenga mtanda wake ndi kunditsata Ine sayenera kukhala wanga. 39Aliyense amene asunga moyo wake adzawutaya koma aliyense amene ataya moyo chifukwa cha Ine adzawupeza.

40“Iye amene alandira inu alandira Ine, ndipo amene alandira Ine alandiranso amene anandituma Ine. 41Aliyense amene alandira mneneri chifukwa chakuti ndi mneneri alandira mphotho ya mneneri, ndipo aliyense amene alandira munthu wolungama chifukwa chakuti ndi munthu wolungama, adzalandira mphotho ya wolungama. 42Ngati aliyense apereka madzi ozizira a mʼchikho kwa mmodzi wa angʼonoangʼono awa chifukwa cha kuti ndi ophunzira anga, ndikuwuzani zoona, ndithudi sadzataya mphotho yake.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

马太福音 10:1-42

差遣使徒

1耶稣叫了十二位门徒来,将权柄赐给他们,使他们能够赶出污鬼、医治各样的疾病。 2以下是这十二位使徒的名字:

首先是西门,又名彼得,还有彼得的兄弟安得烈西庇太的儿子雅各雅各的兄弟约翰3腓力巴多罗买多马、税吏马太亚勒腓的儿子雅各达太4激进党人10:4 激进党人”指当时激进的犹太民族主义者,常以行动反抗统治他们的罗马政府。西门和出卖耶稣的加略犹大

5耶稣差遣这十二个人出去,嘱咐他们:“外族人的地方不要去,撒玛利亚人的城镇也不要进, 6要到以色列人当中寻找迷失的羊。

7“你们要边走边传,‘天国临近了!’ 8要医好病人,叫死人复活,使麻风病人痊愈,赶走邪灵。你们白白地得来,也应当白白地给人。 9出门时钱袋里不要带金、银、铜币, 10不要带行李、备用的衣服、鞋子或手杖,因为做工的理应得到供应。 11你们无论到哪座城、哪个村,要在那里寻找愿意接待你们的人,然后住在他家,一直住到离开。 12你们进他家的时候,要为他们祝福。 13如果那家配得福气,你们的祝福必临到他们;如果那家不配蒙福,祝福仍归给你们。 14如果有人不接待你们,不听你们传的信息,你们离开那家或那城时,就把脚上的尘土跺掉作为对他们的警告。 15我实在告诉你们,在审判之日,他们所受的痛苦比所多玛蛾摩拉所受的还大!

将临的迫害

16“听着,我差你们出去,就好像使羊走进狼群一般。所以,你们要像蛇一样机灵,像鸽子一样驯良。

17“你们要小心谨慎,因为人们要把你们送上法庭,也要在会堂里鞭打你们。 18你们要因我的缘故被带到官长和君王面前,在他们和外族人面前为我做见证。 19当你们被押送公堂时,不用顾虑如何应对,或说什么话,那时必会赐给你们当说的话。 20因为那时候说话的不是你们自己,乃是你们父的灵借着你们说话。

21“那时,人必把自己的弟兄置于死地,父亲必把儿子置于死地,儿女必反叛父母,置他们于死地。 22你们将为我的名而被众人憎恨,但坚忍到底的必定得救。 23如果你们在一个地方遭迫害,就避到另一个地方。我实在告诉你们,没等你们走遍以色列的城镇,人子就来了。

24“学生不能高过老师,奴仆也不能大过主人。 25学生顶多和老师一样,奴仆顶多和主人一样。连一家之主都被骂成是别西卜10:25 别西卜”是鬼王的名字。,更何况祂的家人呢?

26“不要害怕那些迫害你们的人。因为掩盖的事终会暴露出来,隐藏的秘密终会被人知道。 27你们要把我私下告诉你们的当众讲出来,你们要在屋顶上把听到的悄悄话宣告出来。 28那些只能杀害身体,不能毁灭灵魂的人,不用怕他们。但要畏惧那位有权将身体和灵魂一同毁灭在地狱里的上帝。 29两只麻雀不是只卖一个铜钱吗?然而没有天父的许可,一只也不会掉在地上。 30就连你们的头发都被数过了。 31所以不要害怕,你们比许多麻雀更贵重!

32“凡公开承认我的,我在天父面前也必承认他; 33凡公开不承认我的,我在天父面前也必不承认他。

跟从主的代价

34“不要以为我来了会让天下太平,我并非带来和平,乃是带来刀剑。 35因为我来是要叫儿子与父亲作对,女儿与母亲作对,媳妇与婆婆作对, 36家人之间反目成仇。

37“爱父母过于爱我的人不配做我的门徒;爱儿女过于爱我的人不配做我的门徒; 38不肯背起他的十字架跟从我的人不配做我的门徒。 39试图保全自己生命的反而会失去生命,但为我舍弃生命的反而会得到生命。

得赏赐

40“人接待你们就是接待我,接待我就是接待差我来的那位。 41因为某人是先知而接待他的,必得到和先知一样的赏赐;因为某人是义人而接待他的,必得到和义人一样的赏赐。 42人若接待我门徒中最卑微的人,并因为他是我的门徒而给他一杯凉水喝,我实在告诉你们,那人必得到赏赐。”