Masalimo 99 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 99:1-9

Salimo 99

1Yehova akulamulira,

mitundu ya anthu injenjemere;

Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi,

dziko lapansi ligwedezeke.

2Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova;

Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.

3Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri,

Iye ndi woyera.

4Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo

Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera;

mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.

5Kwezani Yehova Mulungu wathu

ndipo mulambireni pa mapazi ake;

Iye ndi woyera.

6Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake,

Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake;

iwo anayitana Yehova

ndipo Iyeyo anawayankha.

7Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo;

iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.

8Inu Yehova Mulungu wathu,

munawayankha iwo;

Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka,

ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.

9Kwezani Yehova Mulungu wathu

ndipo mumulambire pa phiri lake loyera,

pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.

New Serbian Translation

Псалми 99:1-9

Псалам 99

1Господ влада –

нек народи дрхте!

Над херувимима он седи –

нек се земља тресе!

2Велики је Господ на Сиону,

узвишен је над свим народима.

3Велико ти име нека славе,

јер је страшно –

он је свет!

4Моћан је цар који воли правду;

Јакову си учврстио подједнако

и правду и праведност,

ти си то учинио.

5Уздижите Господа, Бога нашег!

Поклоните се пред подножјем његових ногу,

јер је он свет.

6Мојсије и Арон, свештеници његови;

Самуило, један од оних што су му се молили,

звали су Господа

и он их је услишио.

7У стубу од облака им је говорио,

а они су држали прописе

и уредбе које им је дао.

8О, Господе, Боже наш,

ти си их услишио!

Био си им Бог који опрашта

али и онај што кажњава њихова злодела.

9Уздижите Господа, Бога нашег!

Поклоните се на његовој светој гори,

јер наш Господ, Бог је свети.