Salimo 99
1Yehova akulamulira,
mitundu ya anthu injenjemere;
Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi,
dziko lapansi ligwedezeke.
2Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova;
Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.
3Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri,
Iye ndi woyera.
4Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo
Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera;
mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.
5Kwezani Yehova Mulungu wathu
ndipo mulambireni pa mapazi ake;
Iye ndi woyera.
6Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake,
Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake;
iwo anayitana Yehova
ndipo Iyeyo anawayankha.
7Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo;
iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.
8Inu Yehova Mulungu wathu,
munawayankha iwo;
Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka,
ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.
9Kwezani Yehova Mulungu wathu
ndipo mumulambire pa phiri lake loyera,
pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.
Psalm 99
1The Lord reigns,
let the nations tremble;
he sits enthroned between the cherubim,
let the earth shake.
2Great is the Lord in Zion;
he is exalted over all the nations.
3Let them praise your great and awesome name—
he is holy.
4The King is mighty, he loves justice—
you have established equity;
in Jacob you have done
what is just and right.
5Exalt the Lord our God
and worship at his footstool;
he is holy.
6Moses and Aaron were among his priests,
Samuel was among those who called on his name;
they called on the Lord
and he answered them.
7He spoke to them from the pillar of cloud;
they kept his statutes and the decrees he gave them.
8Lord our God,
you answered them;
you were to Israel a forgiving God,
though you punished their misdeeds.99:8 Or God, / an avenger of the wrongs done to them
9Exalt the Lord our God
and worship at his holy mountain,
for the Lord our God is holy.