Masalimo 99 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 99:1-9

Salimo 99

1Yehova akulamulira,

mitundu ya anthu injenjemere;

Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi,

dziko lapansi ligwedezeke.

2Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova;

Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.

3Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri,

Iye ndi woyera.

4Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo

Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera;

mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.

5Kwezani Yehova Mulungu wathu

ndipo mulambireni pa mapazi ake;

Iye ndi woyera.

6Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake,

Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake;

iwo anayitana Yehova

ndipo Iyeyo anawayankha.

7Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo;

iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.

8Inu Yehova Mulungu wathu,

munawayankha iwo;

Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka,

ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.

9Kwezani Yehova Mulungu wathu

ndipo mumulambire pa phiri lake loyera,

pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.

New International Version

Psalms 99:1-9

Psalm 99

1The Lord reigns,

let the nations tremble;

he sits enthroned between the cherubim,

let the earth shake.

2Great is the Lord in Zion;

he is exalted over all the nations.

3Let them praise your great and awesome name—

he is holy.

4The King is mighty, he loves justice—

you have established equity;

in Jacob you have done

what is just and right.

5Exalt the Lord our God

and worship at his footstool;

he is holy.

6Moses and Aaron were among his priests,

Samuel was among those who called on his name;

they called on the Lord

and he answered them.

7He spoke to them from the pillar of cloud;

they kept his statutes and the decrees he gave them.

8Lord our God,

you answered them;

you were to Israel a forgiving God,

though you punished their misdeeds.99:8 Or God, / an avenger of the wrongs done to them

9Exalt the Lord our God

and worship at his holy mountain,

for the Lord our God is holy.