Masalimo 99 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 99:1-9

Salimo 99

1Yehova akulamulira,

mitundu ya anthu injenjemere;

Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi,

dziko lapansi ligwedezeke.

2Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova;

Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.

3Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri,

Iye ndi woyera.

4Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo

Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera;

mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.

5Kwezani Yehova Mulungu wathu

ndipo mulambireni pa mapazi ake;

Iye ndi woyera.

6Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake,

Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake;

iwo anayitana Yehova

ndipo Iyeyo anawayankha.

7Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo;

iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.

8Inu Yehova Mulungu wathu,

munawayankha iwo;

Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka,

ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.

9Kwezani Yehova Mulungu wathu

ndipo mumulambire pa phiri lake loyera,

pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.

Hoffnung für Alle

Psalm 99:1-9

Betet den heiligen Gott an!

1Der Herr ist König! In Ehrfurcht erschauern die Völker.

Er thront über den Keruben, darum erzittert die Erde.

2Ja, der Herr regiert auf dem Berg Zion,

über alle Völker ist er hoch erhaben.

3Seinen großen und furchterregenden Namen sollen sie preisen,

denn er ist der heilige Gott!

4Du, Herr, bist ein mächtiger König!

Weil du die Gerechtigkeit liebst,

hast du uns den Maßstab für gerechtes Handeln gegeben,

in ganz Israel99,4 Wörtlich: in Jakob. sorgtest du für Ordnung und Recht.

5Betet den Herrn an, unseren Gott!

Fallt vor seinem Thron99,5 Wörtlich: Fußschemel. nieder,

denn er ist der heilige Gott!

6Schon Mose und Aaron gehörten zu seinen Priestern,

auch Samuel betete zum Herrn.

Sie alle riefen zu ihm, und er gab ihnen Antwort.

7Gott sprach zu ihnen aus der Wolkensäule,

und sie gehorchten den Geboten, die er ihnen gab.

8Herr, unser Gott! Du hast sie erhört.

Du hast deinem Volk die Schuld vergeben,

aber auch ihre Vergehen bestraft.

9Betet den Herrn an, unseren Gott!

Auf seinem heiligen Berg Zion fallt vor ihm nieder,

denn heilig ist er – der Herr, unser Gott!