Masalimo 99 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 99:1-9

Salimo 99

1Yehova akulamulira,

mitundu ya anthu injenjemere;

Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi,

dziko lapansi ligwedezeke.

2Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova;

Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.

3Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri,

Iye ndi woyera.

4Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo

Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera;

mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.

5Kwezani Yehova Mulungu wathu

ndipo mulambireni pa mapazi ake;

Iye ndi woyera.

6Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake,

Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake;

iwo anayitana Yehova

ndipo Iyeyo anawayankha.

7Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo;

iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.

8Inu Yehova Mulungu wathu,

munawayankha iwo;

Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka,

ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.

9Kwezani Yehova Mulungu wathu

ndipo mumulambire pa phiri lake loyera,

pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.

Священное Писание

Забур 99:1-5

Песнь 99

Хвалебная песнь.

1Воскликни Вечному, вся земля!

2Служите Вечному с радостью,

с песнопением приходите к Нему.

3Знайте, что Вечный – Бог!

Он сотворил нас, и мы принадлежим Ему;

мы – народ Его и овцы Его стада.

4Входите в ворота Его с благодарением

и во дворы Его с хвалою;

благодарите Его и славьте имя Его.

5Ведь Вечный благ, милость Его – навеки,

и верность Его – во все поколения.