Masalimo 99 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 99:1-9

Salimo 99

1Yehova akulamulira,

mitundu ya anthu injenjemere;

Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi,

dziko lapansi ligwedezeke.

2Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova;

Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.

3Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri,

Iye ndi woyera.

4Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo

Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera;

mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.

5Kwezani Yehova Mulungu wathu

ndipo mulambireni pa mapazi ake;

Iye ndi woyera.

6Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake,

Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake;

iwo anayitana Yehova

ndipo Iyeyo anawayankha.

7Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo;

iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.

8Inu Yehova Mulungu wathu,

munawayankha iwo;

Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka,

ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.

9Kwezani Yehova Mulungu wathu

ndipo mumulambire pa phiri lake loyera,

pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 99:1-9

Herren er en god og retfærdig konge

1Herren er konge, og alle folkeslag bæver.

Han sidder på en trone af keruber,

og hele jorden skælver.

2Han sidder som konge på Zions bjerg,

han hersker over alle jordens folkeslag.

3De skal ære hans store og herlige navn.

Hans navn er helligt.

4Du store konge, som elsker retfærdighed,

du har sørget for lighed og retfærdighed i Israel.

5Lovpris Herren, vor hellige Gud,

bøj jer ned for hans fødder,

for han er hellig.

6Moses og Aron var hans præster,

Samuel en profet, der bad til Gud.

De påkaldte Herren, og han svarede dem.

7Han talte til dem fra skysøjlen,

og de fulgte den vejledning, han gav dem,

adlød hans bud og befalinger.

8Herre, vor Gud, du svarede dem og var villig til at tilgive,

selv om du måtte straffe dem for deres synder.

9Lovpris Herren, vor Gud,

tilbed ham på hans hellige bjerg.

Hellig er Herren.